< 2 Kings 20 >
1 About that time, Hezekiah became very ill. [He thought that he] was about to die. Isaiah the prophet came to him and said, “This is what Yahweh says: ‘You should tell the people in your palace what you want them to do after you die, because you are not going to recover from this illness. You are going to die.’”
Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
2 Hezekiah turned his face toward the wall and prayed,
Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
3 “Yahweh, do not forget that I have always served you faithfully, and I have done things that pleased you.” Then Hezekiah started to cry loudly.
“Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
4 Isaiah left the king, but before he had crossed the middle courtyard of the palace, Yahweh gave him a message
Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
5 which said, “Go back to Hezekiah, the ruler of my people, and say to him, ‘I, Yahweh, the God whom your ancestor King David [worshiped], have heard what you prayed. And I have seen your tears. So, listen: I will heal you. Two days from now you will [be able to] go up to my temple.
“Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
6 I will enable you to live for 15 more years. And I will rescue you and this city again from the power [MTY] of the king of Assyria. I will defend this city for the sake of my own reputation and because of what I promised King David, who served me [well].’”
Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
7 So Isaiah [returned to the palace and told Hezekiah what Yahweh had said. Then he] [to Hezekiah’s servants], “Bring a paste made of boiled figs. Put some of it on his boil, and he will get well.”
Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
8 Then Hezekiah replied to Isaiah, “What will Yahweh do to prove that he will heal me and that two days from now I will be able to go up to the temple?”
Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
9 Isaiah replied, “Yahweh will do something that will prove to you that he will do what he promised. Do you want him to cause the shadow on the stairway/sundial to go back ten steps/degrees, or to go forward ten steps/degrees?”
Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
10 Hezekiah replied, “It is easy to cause the shadow to move forward, [because that is what it always does]. Tell him to cause it to move backward ten steps/degrees.”
Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
11 So Isaiah prayed earnestly to Yahweh, and Yahweh caused the shadow to go backward ten steps/degrees on the stairway/sundial that King Ahaz had made (OR, that workers had built for King Ahaz).
Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
12 At that time, King Merodach-Baladan, the son of Baladan the [previous] King of Babylonia, heard a report that King Hezekiah had been very sick. So he wrote some letters and gave them to some messengers to take to Hezekiah, along with a gift.
Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
13 [When the messengers arrived], Hezekiah welcomed them gladly. Then he showed them everything that was in his (treasure houses/places where very valuable things were stored)—the silver and gold, the spices, the nice-smelling olive oil, and all the weapons [for his soldiers]. He showed them all the [valuable] things in his storerooms and everywhere else in his kingdom [HYP]; he showed them everything.
Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
14 Then the prophet Isaiah went to Hezekiah and asked him, “Where did those men come from, and what did they say to you?” Hezekiah replied, “They came from a country very far from here. They came from Babylonia.”
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
15 Isaiah asked, “What did they see in your palace?” Hezekiah replied, “They saw everything. I showed them absolutely everything that I own—all my valuable things.”
Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
16 [Isaiah knew that Hezekiah had done a very foolish thing]. So Isaiah said to him, “Listen to what Yahweh says to you.
Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
17 There will be a time when everything that is still in your palace, all the valuable things that were put there by you and your ancestors, will be carried away to Babylon. There will be nothing left here! [That is what] Yahweh says [to you]
Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
18 Furthermore, some of your own descendants will be forced to go there, and they will be castrated in order that they may become servants in the palace of the King of Babylon.”
Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
19 Then Hezekiah replied to Isaiah, “That message from Yahweh that you have given to me is good.” He said that because he was thinking, “Even if that happens, there will be peace and security [in Israel] all the rest of my life.”
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
20 [If you want to know more about] [RHQ] all the other things that Hezekiah did, about his brave deeds in battle, about his ordering a reservoir to be built in the city and a tunnel [to be dug] to bring water into the reservoir, they are all written in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’.
Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
21 Later Hezekiah died [EUP], and his son Manasseh became the king.
Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.