< 2 Kings 16 >

1 When Pekah had been ruling Israel for almost 17 years, Ahaz, the son of Jotham, became the king of Judah.
Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 He was 20 years old when he became the king [of Judah]. He ruled from Jerusalem for 16 years. He did not do things that pleased Yahweh his God, good things like his ancestor King David had done.
Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
3 Instead, he was as sinful as the kings of Israel had been. He even sacrificed his son as an offering to idols. That was worse than the disgusting things that the people who previously lived there had done, people whom Yahweh had expelled as the Israelis were advancing through the land.
Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
4 Ahaz offered sacrifices and burned incense [to honor Yahweh] on the tops of many hills and under many [HYP] big trees, [instead of in Jerusalem as Yahweh had commanded].
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
5 While he was the king of Judah, King Rezin of Assyria and King Pekah of Israel [came with their armies] and attacked Jerusalem. They surrounded the city, but they could not conquer it.
Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
6 At that time the [army of the] king of Edom expelled the people of Judah who were living in Elath [city]. Some of the people of Edom started to live there, and they are still living there.
Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
7 King Ahaz sent messengers to King Tiglath-Pileser of Assyria, to tell this message to him: “I promise that I will completely do what you tell me to do, [as though] I [was] your son. Please come and rescue us from the armies of Syria and Israel who are attacking my country.”
Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
8 Ahaz took the silver and gold that was in the palace and in the temple and sent it to Assyria to be a present/gift for the king of Assyria.
Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
9 So Tiglath-Pileser did what Ahaz requested. His army marched to Damascus and captured it, and they took the people of Damascus as prisoners to live in the capital city of Assyria, and executed [King] Rezin.
Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
10 When King Ahaz went to Damascus to meet King Tiglath-Pileser, he saw the altar that was there. So he sent to Uriah, the Supreme Priest [in Jerusalem], a drawing of the altar and a model that was exactly like the altar in Damascus.
Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
11 So Uriah built an altar [in Jerusalem], following the drawing that King Ahaz had sent. Uriah finished the altar before Ahaz returned [to Jerusalem] from Damascus.
Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
12 When the king returned from Damascus, he saw the altar. He went to it
Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
13 and burned animal sacrifices and a grain offering on it. He also poured a wine offering on it and threw on it the blood of the offerings to maintain fellowship with God.
Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
14 The old bronze altar which had been dedicated long ago to Yahweh was between the new altar and the temple, so Ahaz moved it to the north side of his new altar, [which was bigger than the old altar].
Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
15 Then King Ahaz ordered Uriah: “Each morning put on this new altar the sacrifices that will be completely burned, and in the evening put on it the grain offering, along with my offering and the offerings that the people bring, ones that will be completely burned, and my grain offering and the people’s grain and wine offerings. Pour against the sides of the altar the blood of all the animals that are sacrificed. But the old bronze altar will be only for me to use to find out what Yahweh wants me to do.”
Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
16 So Uriah did what the king commanded him to do.
Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
17 King Ahaz told his workers to take off the frames of the carts [that were outside the temple] and to take down the basins that were on them. They also took down the bronze tank from the backs of the bronze [statues of the] oxen and put it on a stone foundation.
Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
18 Then to please the king of Assyria, Ahaz had them remove from the temple the roof under which the people walked into the temple on the Sabbath Day, and closed up the private entrance into the temple for the kings of Judah.
Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
19 [If you want to know about] the other things that Ahaz did, they are written [RHQ] in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’.
Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 Ahaz died [EUP], and he was buried in [the part of Jerusalem called] ‘The City of David’, where his ancestors had been buried. Then his son Hezekiah became the king.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kings 16 >