< 2 Kings 12 >

1 When Jehu had been ruling Israel for almost seven years, Joash became the king of Judah. He ruled in Jerusalem for 40 years. His mother was Zibiah, from Beersheba [city].
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 All his life, he did what pleased Yahweh, because Jehoiada the priest instructed/taught him.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
3 But the places where the people worshiped [Yahweh] on the tops of hills were not destroyed, and they continued to offer sacrifices and burn incense at those places, [instead of at the place that God had chosen for them in Jerusalem].
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
4 Joash said to the priests, “You must take all the money which the people contribute, both the money they are required to give and the money that they themselves decide to give, as sacred offerings to buy things for the temple.
Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
5 Each priest must take the money from people who know him (OR, from one of the treasurers), and he must use that money to repair the temple whenever he sees that there is something that needs to be repaired.”
Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
6 But after Joash had been ruling for almost twenty-three years, the priests still had not repaired anything in the temple.
Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
7 So Joash summoned Jehoiada and the other priests and said to them, “(Why are you not repairing things in the temple?/You should have been repairing things in the temple!) [RHQ] From now on, you must not keep the money that you receive from people who know you (OR, the treasurers). You must give it to the people who will be repairing things in the temple!”
Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
8 The priests agreed to do that, and they also agreed that they themselves would not do the repair work.
Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
9 Then Jehoiada took a chest and bored a hole in the lid. He placed it alongside the altar [for burning incense/sacrifices] that was on the right as anyone enters the temple. The priests who guarded the entrance to the temple put in the box the money that was brought to the temple.
Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
10 Whenever they saw that there was a lot of money in the chest, the king’s secretary and the Supreme Priest would come and count the money. Then they would put it in bags and tie the bags shut.
Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
11 Then, after they weighed it, they would give the money to the men who supervised the work in the temple. Then the supervisors would use that money to pay the carpenters and builders who did the repair work in the temple,
Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
12 and the masons and the stone cutters. Also with some of that money they bought timber and stones that had been cut to be used in the repair work, and to pay all the other expenses for the repair work.
amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
13 But they did not use any of that money [to pay men] to make silver cups or wick trimmers or bowls or trumpets or any other items made of silver or gold to be used in the temple.
Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
14 All that money was given to the men who were doing the work of repairing the temple.
Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
15 The men who supervised the work always did things honestly, so the king’s secretary and the Supreme Priest never required that the supervisors report what they had spent the money for.
Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
16 But the money that people gave to pay for the wrong things that they had done and the money they gave to purify themselves because of the sins that they had committed was not put in the chest. That money belonged to the priests.
Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
17 At that time, Hazael, the king of Syria, went [with his army] and attacked Gath [city] and conquered it. Then he decided that they would attack Jerusalem.
Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
18 So Joash, the king of Judah, took all the money that the previous kings, Jehoshaphat and Jehoram and Ahaziah, had dedicated to Yahweh. He added some of his own money, and all the gold that was in the rooms in the temple where valuable things were kept/stored, and the gold in his palace, and sent it all to King Hazael, [to (appease him/persuade him to not attack Jerusalem)]. So King Hazael [took his army] away from Jerusalem.
Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
19 [If you want to read more of] what Joash did, [it] is all written [RHQ] in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’.
Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 Joash’s officials plotted against him, and two of them killed Joash on the road that goes down to [the] Silla [district]. The two men who did that were Jozabad, the son of Shimeath, and Jehozabad, the son of Shomer. Joash was buried in the place where his ancestors were buried, [in the part of Jerusalem called] ‘The City of David’. Then Joash’s son Amaziah became the king of Judah.
Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kings 12 >