< 2 Chronicles 23 >

1 After Joash had been hidden in the temple for six years, Jehoiada the priest decided that it was necessary to do something. So he made an agreement with the army commanders of groups of 100 soldiers: Azariah the son of Jeroham, Ishmael the son of Jehohanan, Azariah the son of Obed, Maaseiah the son of Adaiah, and Elishaphat the son of Zicri.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
2 They went throughout Judah and gathered the descendants of Levi and the leaders of Israeli families from all the towns. When they came to Jerusalem,
Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
3 the whole group went to the temple and made an agreement with the young king there. Jehoiada said to them, “This is the son of the previous king of Judah. So he is the one who must rule, like Yahweh promised that the descendants of King David must do.
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
4 “So this is what you must do: One-third of you priests and other descendants of Levi who are starting their work on the Sabbath day must guard the doors [of the temple].
Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
5 One-third of you must guard the king’s palace, and one-third of you must guard the Foundation Gate. All the other people will be in the courtyards outside the temple.
ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
6 Only the priests and the descendants of Levi who work there will enter the temple. They will be allowed to enter the temple because they are set apart [for that work]. All the others must remain in the courtyards, obeying what Yahweh has commanded.
Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
7 You descendants of Levi must stand around the young king, each of you with your weapon in your hand. Anyone else who tries to enter the temple you must kill. And stay close to the young king, wherever he goes.”
Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
8 So the descendants of Levi and all [the men of] Judah did what Jehoiada had told them. He did not allow anyone to go home after having finished his work on that Sabbath day. Each commander took charge of his men, the ones who were finishing their work on that day and those who were starting their work on that day.
Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
9 Then Jehoiada gave each of the commanders the spears and the large and small shields that had been put there in the temple by King David.
Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
10 He commanded all the guards to stand in their positions, each with his sword in his hand, all around the king—around the altar and the temple, from the north side to the south side.
Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
11 Then Jehoiada and his sons brought Joash out. They put a crown on his head and gave him [a scroll] on which were written the rules [that the kings needed to obey], and proclaimed that he was now the king. They anointed him with olive oil and shouted, “We hope that the king will live for many years!”
Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
12 When Athaliah heard the noise being made by the people running [toward the king] and cheering, she ran to the temple.
Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
13 She saw the young king there, standing alongside the pillar at the entrance of the temple, [which is the place at the temple] where the kings usually stood. The army commanders and trumpet players were standing beside the king, and all the people of Judah were rejoicing and blowing trumpets, and singers with their musical instruments were leading the people while they praised God. Then Athaliah tore her robes and started screaming, “You are committing treason!”
Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
14 Jehoiada the Supreme Priest said to the army commanders, “Kill her, but do not kill her at the temple of Yahweh!” Then he said to them, “Bring Athaliah out in front of the troops and kill anyone who tries to follow her!”
Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
15 [She tried to flee, but] they seized her as she reached the gate where horses enter the palace area, and they killed her there.
choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
16 Then Jehoiada made an agreement that he and the king and all the other people would be Yahweh’s people.
Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
17 Then all the people who were there went to the temple of Baal and tore it down. They smashed the altars [of Baal]. They also killed Mattan, the priest of Baal, in front of those altars.
Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
18 Then Jehoiada appointed the priests, who were also descended from Levi, to work at the temple. They were part of the group to whom King David had given various jobs at the temple, to sacrifice the animals that were to be completely burned on the altar, doing what was written in the laws that Moses had given to them. He also told them to rejoice and sing, which was also what David had commanded.
Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
19 He also put guards at the gates of the temple in order that anyone who was unacceptable to God would not be allowed to enter.
Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
20 Jehoiada took with him the army commanders, the important men, the leaders and many others, and brought the king down from the temple. They went into the palace through the Upper Gate, and put the king on his throne.
Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
21 Then all the people of Judah rejoiced. And there was calm throughout the city, because Athaliah had been killed.
ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.

< 2 Chronicles 23 >