< 2 Chronicles 19 >

1 When King Jehoshaphat was returning safely to his palace in Jerusalem,
Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
2 the prophet Jehu, the son of [the prophet] Hanani, went out of the city to meet the king, and said to him, “It was not right for you to help a wicked man and to love those who hate Yahweh. Because of what you have done, Yahweh is angry with you.
mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
3 But you have done some good things; you got rid of the poles in this country for [worshiping the goddess] Asherah, and you have strongly determined to do what pleases God.”
Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
4 Jehoshaphat lived in Jerusalem. But [one time], like he had done once previously, he went out among all the people in the country, from Beersheba [city in the far south] to the hilly area of [the tribe of] Ephraim [in the far north], and he convinced them to return to [worshiping] Yahweh, the God whom their ancestors [worshiped].
Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
5 He appointed judges throughout Judah, in each of the cities that had walls around them.
Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
6 He told them, “Make your decisions carefully, because you are judging cases not [in order] to [please] people but to [please] Yahweh. And he will be watching you whenever you make a decision.
Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
7 So now revere Yahweh, and judge cases carefully, [and do not forget that] Yahweh our God never acts unjustly, and he never does what people want because of their offering him money; he never accepts bribes.”
Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
8 In Jerusalem also, Jehoshaphat appointed some priests and other descendants of Levi and some leaders of Israeli families [to be judges]. He told them to do what Yahweh’s laws said was right when they settled disputes. Those men lived in Jerusalem.
Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
9 He told them this: “You must always do your work faithfully, revering Yahweh.
Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
10 In every dispute that your fellow Israelis who live in the cities want you to settle, you must warn them to not sin against Yahweh [by telling lies during the trial]. If you do not warn them, God will punish both you and your fellow Israelis. If you warn them, you will not be sinning. You must warn them whether [someone has accused them] of murdering someone, or of disobeying some other law or command or decree [of Yahweh].
Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
11 Amariah the Supreme Priest will supervise you in any matter that Yahweh is concerned about, and Zebadiah the son of Ishmael, the leader of the tribe of Judah, will supervise you in any matter that I am responsible for. And the descendants of Levi will assist you. Act courageously, and I pray that Yahweh will help those who do their work well.”
“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”

< 2 Chronicles 19 >