< 1 Timothy 5 >
1 Do not rebuke/scold older men. Instead, exhort/advise them [respectfully] as you would [exhort/advise] your father. Exhort/advise younger men [gently] as you would exhort/advise your brothers.
Usadzudzule munthu wachikulire mokalipa, koma umuchenjeze ngati abambo ako. Achinyamata uwatenge ngati abale ako.
2 [Exhort/advise] older women [respectfully] as [you would exhort/advise] your mother. [Exhort/advise] younger women [gently] as [you would exhort/advise] your sisters; but you must act in a completely proper way as you do that.
Amayi achikulire uwatenge ngati amayi ako ndipo amayi achitsikana uwatenge ngati alongo ako, nʼkuyera mtima konse.
3 [Make sure that the congregation] takes care of widows who have no one to care for them.
Uziwachitira ulemu akazi amasiye amene ali okhaokha.
4 If a widow has children or grandchildren, these [children or grandchildren] should learn that they are to take care of their own family first. By doing that they can repay their parents and grandparents for all that they did for them when they were young, because doing that pleases God.
Koma ngati mkazi wamasiye ali ndi ana ndi zidzukulu, anawo ayambe aphunzira kukwaniritsa udindo wawo pa banja lawo moopa Mulungu, potero akubweza zabwino kwa makolo awo ndi agogo awo. Pakuti zimenezi ndiye zimakondweretsa Mulungu.
5 The widows who are really alone and have no one [to help them] confidently expect that God [will help them]. So night and day they pray, earnestly asking [DOU] [God that he will help them and others].
Mkazi wamasiye amene ali yekha ndi wopanda womuthandiza, ameneyo wayika chiyembekezo chake pa Mulungu, ndipo amapemphera kosalekeza usana ndi usiku kuti Mulungu azimuthandiza.
6 But widows who just want to have a lot of pleasure are [spiritually] [MET] dead, although they are [physically] alive.
Koma mkazi wamasiye amene amangokhalira kuchita zosangalatsa moyo wake, wafa kale ngakhale akanali ndi moyo.
7 And tell [the congregation] that [the children or grandchildren should do] these things in order that [no one] can (criticize the believers/say that the believers are doing anything that is wrong).
Pereka malangizo amenewa kwa anthu kuti akhale opanda zolakwa.
8 If anyone does not take care of those who live in his own house, and especially if he does not take care of his own family, he has (denied/quit believing) what we believe and [we should consider that] he is worse than a person who does not believe [in Christ].
Ngati wina sasamalira abale ake, makamaka a mʼbanja mwake mwenimweni, ameneyo wakana chikhulupiriro ndipo ndi woyipa kuposa wosakhulupirira.
9 [You have a list of] widows [who will do work for the congregation and receive money]. Put women’s names on the list [only if] they are more than 60 years old, and if they were faithful to their husbands.
Mayi wamasiye aliyense amene sanakwanitse zaka 60 zakubadwa, asakhale mʼgulu la akazi amasiye. Akhale woti anakwatiwapo ndi mwamuna wake mmodzi yekha.
10 [Put women’s names on that list only] if it is known that they have wholeheartedly done every kind of good deed, if they have helped [children] who were afflicted/suffering, if they have (brought up/cared for) their children [properly/well], if they have welcomed and cared for guests, and if they have humbly served [MTY] other believers.
Akhale mayi woti amadziwika bwino pa ntchito zake zabwino monga kulera ana, kusamalira alendo, kusambitsa mapazi a anthu a Mulungu, kuthandiza amene ali pa mavuto ndi kudzipereka pa ntchito zonse zabwino.
11 As for younger widows, do not put their names on that list, because they [promise to do work for the congregation, but instead of doing that, they usually] want to marry [again] (OR, marry an unbeliever) when they have a strong desire to get married.
Akazi amasiye achitsikana, usawayike mʼgulu limeneli. Pakuti zilakolako zawo zikayamba kuwavutitsa nʼkuwalekanitsa ndi Khristu, amafuna kukwatiwanso.
12 If that happens, they may become guilty of not having done what they had promised [to do for the congregation] (OR, promised [Christ that they would do].)
Zikatero amadziweruza okha chifukwa aphwanya lonjezo lawo loyamba.
13 In addition, they [generally] become lazy. Specifically, as they [just] go about from house to house, they also begin (to gossip/to talk about people) and to meddle in other people’s affairs, saying what they should not say.
Komanso amakhala ndi chizolowezi cha ulesi ndi kumangoyenda khomo ndi khomo. Ndipo sikungokhala aulesi kokha komanso kuchita miseche, kududukira za eni ake, kumangokamba zinthu zosayenera kukamba.
14 So I advise that [instead of putting the names of younger widows on the list, they] marry again, that they bear/have children, that they manage their homes [well], and that they do nothing for which an enemy can say bad things about [them].
Kotero, ndikulangiza akazi amasiye achitsikana kuti akwatiwe, akhale ndi ana, asamalire makomo awo ndipo asamupatse mdani mpata wonyoza
15 [I say this] because some [younger widows] have stopped [obeying Christ] in order to obey Satan.
Akazi amasiye ena apatuka kale nʼkumatsatira Satana.
16 If any woman who believes [in Christ] has widows [in her household/family], she should take care of them. The congregation should not be burdened by having {She should not depend on the congregation} to take care of their [needs]. The congregation should take care of the widows who truly [have no one to care for them].
Ngati mayi aliyense wokhulupirira ali ndi akazi amasiye amene akuwasamalira, apitirizebe kuwasamalira ndipo asalemetse mpingo, kuti mpingo uthandize akazi amasiye amene ali okhaokha.
17 [Each congregation] should pay well the elders who lead [well. They should] greatly honor them, especially those who preach and those who teach.
Akulu ampingo amene amayangʼanira bwino zochitika za mu mpingo, ndi oyenera ulemu wowirikiza, makamaka amene ntchito yawo ndi kulalikira ndi kuphunzitsa.
18 [Long ago Moses] wrote in the Scriptures, “While an ox is threshing [grain], you must not tie its mouth [so that it cannot eat the grain],” and [Jesus said], “[People] should pay those who work [for their benefit].” [So we know that congregations should support their leaders].
Pakuti Mawu a Mulungu amati, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu,” ndi “Wantchito ngoyenera kulandira malipiro ake.”
19 When some person accuses an elder [about doing wrong], accept what he says only if there are [at least] two or three persons who (testify/say [that]) [they saw him do that wrong].
Usamamvere mawu oneneza akulu ampingo pokhapokha patakhala mboni ziwiri kapena zitatu.
20 But as for any [elder] who repeatedly sins, rebuke him before the whole congregation, in order that the rest [of the elders] will be afraid [to sin].
Akulu ampingo amene akuchimwa, uwadzudzule poyera kuti ena aphunzirepo.
21 I solemnly tell you that [as you keep in mind that] God and Christ Jesus and the holy angels know everything that you do, obey these commands [about elders]! [As you consider what others say about an elder doing wrong], do not easily/quickly decide that what they say is true. And treat them all equally.
Ndikukulamulira pamaso pa Mulungu, pamaso pa Yesu Khristu ndi pamaso pa angelo osankhika, kuti usunge malangizowa mosachotsera ndipo usachite kalikonse mokondera.
22 Do not be in a hurry to put your hands on a man ([to set him apart/to appoint him]) [as an elder. Wait until you have examined him to see how he conducts his life], because [God will consider] that you are responsible if [you approve] a person who sins, saying that he should [become an elder]. Keep your life pure in every way.
Usafulumire kusanjika manja munthu, ndipo usavomerezane ndi anthu ena pa machimo. Usunge bwino kuyera mtima kwako.
23 [And Timothy], no longer drink [only] water, but instead, drink a little wine [also], because [that may help to cure] your stomach’s frequent illnesses.
Uleke kumangomwa madzi okha, koma uzimwako vinyo pangʼono chifukwa cha vuto lako la mʼmimba ndi kudwala kwako kwa pafupipafupi.
24 [I tell you not] ([to set apart/appoint]) [elders hastily, without seeing how they conduct their lives, because] some people [sin secretly], so that it is not known what they have done until after someone examines them (OR, before God judges them). But some people sin openly, so that people know what they have done before anyone examines them.
Anthu ena machimo awo amaonekeratu poyera, amakafika pa mpando wachiweruzo eni akewo asanakafike. Machimo a anthu ena amabwera mʼmbuyo mwawo.
25 Similarly, although [some people] do good things openly, with the result that people know what they have done, some people [do good things secretly], yet the good things that they have done cannot remain secret either.
Momwemonso, ntchito zabwino zimaonekera poyera, ndipo ngakhale zipande kutero, sizingatheke kubisika.