< 1 Samuel 29 >

1 The Philistia army gathered at Aphek [Valley, which is near Shunem]. The Israelis set up their tents at Jezreel [city, which was in the same valley].
Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
2 The kings of Philistia divided their men into groups; some groups had 100 soldiers and some groups had 1,000 soldiers. David and his men were marching behind, with King Achish.
Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
3 But the Philistia commanders asked, “What are these Hebrews [doing here, marching with us to battle]?” Achish replied, “[Their leader is] David. [He] previously worked for King Saul of Israel, but now he has been living near me for more than a year. During all the time since he left Saul, I have not seen/found that he has any faults.”
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
4 But the Philistia army commanders were angry with Achish [for allowing David’s army to be going with them]. They said to him, “Send David [and his men] back to the city that you gave to him! We do not want him to go with us into the battle. [If he goes with us, ] we will have an enemy in our own midst! He would please King Saul by killing our own soldiers [RHQ]!
Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
5 [Have you forgotten that] David is the one about whom the Israelis dance and sing, saying, ‘Saul has killed 1000 of our enemies, but David has killed 10,000 of them!’?”
Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
6 So Achish summoned David, and said to him, “Just as surely as Yahweh lives, you have been loyal to me. I would like very much for you to fight along with my army. Since the day that you came to me, I have not found/seen that you have any faults. But the other Philistia rulers do not trust you.
Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
7 So all of you go back home, and I hope/desire that things will go well for you. I do not want you(sg) to do anything that the other rulers of Philistia will not be pleased with.”
Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
8 David replied, “What wrong have I done? Since the day that I first came to you until today, have I done anything that you think is evil? Your majesty, why will you not allow me to go and fight against your enemies?”
Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
9 Achish replied, “I know that you are as just as good as an angel from God. But the commanders of my army have said, ‘We will not allow David [and his men] to go with us into the battle.’
Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
10 So early tomorrow morning you and your men must leave. Get up as soon as it is light and leave.”
Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
11 So David and his men got up early the following morning and returned to the area where the Philistia people lived. And the Philistia army went up to Jezreel.
Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.

< 1 Samuel 29 >