< 1 Samuel 2 >
1 Then Hannah prayed, saying, “I rejoice in [what] you, [, have done]. I am strong [MET] because I belong to you. I (laugh at/ridicule) my enemies, because you, Yahweh have rescued me [from being taunted by them].
Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
2 There is no one who is holy like you, Yahweh. There is no other god like you. There is no one like you, our God, who can protect us [as though you were putting us beneath] a huge rock [where we can hide from danger].
“Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
3 [You people who oppose God], stop boasting! Yahweh is a God who knows [everything], and he will evaluate/judge everyone’s actions. So don’t speak so arrogantly!
“Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
4 Yahweh, you break the bows/weapons of mighty soldiers, and you give strength to those who stumble [because of being weak].
“Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
5 Many people who previously had plenty to eat, now have to work for other people [to earn money] to buy food, but many who were always hungry are not hungry any more. The woman who did not have any children before, now has given birth to many/seven children, and the woman who had many children before, now is very lonely [because they have all died].
Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
6 Yahweh, you cause some people to die, and you restore some people who are almost dead. For some people, [it seems that they will soon] go to where the dead people are, but you cause them to become healthy again. (Sheol )
“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
7 Yahweh, you cause some people to be poor and you cause some people to be rich, you humble some people and you honor some people.
Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
8 [Sometimes] you lift poor people up so that they are no longer [despondent, sitting in the dust, ] or sitting on heaps of ashes; you cause them to sit next to princes; you cause them to sit on chairs/thrones where people who are highly honored sit. Yahweh, you are the one who laid the foundations of the earth, and you have set the whole world on those foundations.
Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
9 You will protect your loyal/faithful people [SYN], but you will cause the wicked to die [EUP] and descend to the dark [place where dead people are]. We do not defeat [our enemies] by our own strength;
Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
10 Yahweh, you will break into pieces those who oppose you. You will cause thunder in the sky to show that you (oppose/are angry with) them. Yahweh, you will judge [people everywhere, even those who live in] the most remote places on the earth. You will give strength to the king whom you will appoint, and give him great power [over his enemies].”
Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
11 Then Elkanah [and his family] returned to Ramah, but Samuel, the little boy, stayed to help Eli the priest serve Yahweh.
Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
12 Eli’s two [, who were also priests, ] were very wicked. They did not revere (OR, respect/obey) Yahweh.
Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
13 While the people were boiling the meat from their sacrifices [in the huge pot at the temple], one of Eli’s sons, [would send his servant to come with a large three-pronged fork in his hand].
Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
14 [He] would stick the fork into [the meat in] the pot, and whatever meat fastened onto the fork, he would take [and give it] to the priest who sent him. Eli’s sons did this to all the Israeli people who came to Shiloh [to offer sacrifices].
Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
15 Furthermore, before the fat [on the meat] was [cut off and] and burned [as a sacrifice to Yahweh], the servant of the priest would [sometimes] come to the man who was making the sacrifice and say to him, “Give me some meat [now to take] to the priest for him to roast! He wants raw meat; he does not want boiled meat.”
Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
16 If the man said to the servant, “Let the priests [cut off and] burn the fat first; then you can take what you want,” the servant would reply, “No, give it to me now; if you do not give it to me, I will take it forcefully!”
Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
17 Yahweh considered that the young [sons of Eli] were committing a very great sin, because they were treating very disrespectfully the offerings that were being given to Yahweh.
Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
18 As for Samuel, who was still a very young boy, he continued to do work for Yahweh, wearing a little sacred linen vest [like the Supreme Priest wore].
Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
19 Each year his mother made a [new] little robe for him and took it to him when she went up [to Shiloh] with her husband to offer a sacrifice.
Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
20 Then Eli would [ask God to] bless Elkanah and his wife, and he would say to Elkanah, “I hope/desire that Yahweh will enable your wife to give birth to other children, to take the place of the one whom she dedicated to Yahweh.” Then Elkanah and his family would return home.
Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
21 And Yahweh was very kind to Hannah, and enabled her to give birth to three [other] sons and two daughters. Their son Samuel grew up while he was doing work for Yahweh [in the Sacred Tent].
Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
22 Eli became very old. He often heard about all the [evil] things that his sons were doing to the Israeli people. He heard that they [sometimes] (slept with/had sex with) the women who worked at the entrance to the tent where [God] spoke to [his people].
Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
23 He said to them, “(It is terrible that you do such things!/Why do you do such things?) [RHQ] Many people keep telling me about the evil things that you do.
Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
24 My sons, stop it! The reports [about you] that the people who belong to Yahweh tell others are terrible [EUP]!
Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
25 If one person sins against another person, God can (intercede/act as a referee) between them. But if someone sins against Yahweh, no one can [RHQ] (intercede/act as a referee) between them!” But Eli’s sons would not listen to what their father said. This was because Yahweh had decided [that someone should] them.
Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
26 The boy Samuel continued to grow up, and the things that he did pleased Yahweh and the people.
Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
27 One day, a prophet came to Eli and told him, “This is what Yahweh has told me: ‘When your ancestors were slaves of the king of Egypt, I appeared to Aaron.
Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
28 From all the tribes of the Israeli people, I chose him [and his male descendants] to be priests for me. I appointed them to go up to my altar, to burn incense, to wear a sacred apron [as they worked] for me. And I declared that they could take [and eat some of the meat] that the Israeli people burned [on the altar].
Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
29 So why do you show disrespect for the sacrifices and offerings that I commanded [the people to bring] to me [RHQ]? You are honoring your sons more than you are honoring me, by allowing them to get fat from eating the best parts of all the sacrifices that the Israeli people bring to me!’
Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
30 “Therefore, this is what Yahweh, the God whom we Israelis [worship], declares: ‘I definitely promised that Aaron and his descendants would continue to serve [IDM] me forever.’ But now I declare this: ‘It will not continue like that! I will honor those who honor me, but I will despise those who despise me.
“Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
31 Listen carefully! There will soon be a time when I will cause all the strong [young men] in your family to die. The result will be that no men in your family will [live long enough to] become old men.
Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
32 You will be distressed and envious as you see the blessings that I will give to [the other people in] Israel. And [I repeat that] no men in your family will ever live long enough to become old men.
Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
33 There is one of your descendants whom I will spare, and not prevent him from serving me as a priest. But he will become blind, and then he will always be sad and grieving. But all your other descendants will die violently.
Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
34 And your two sons, Hophni and Phinehas, will both die on the same day. And that will prove to you [that all that I have said will come true/happen].
“‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
35 ‘have chosen another man to be my priest. He is one who will serve me faithfully: He will do everything I want [DOU] him to do. And I will enable him to have many descendants [IDM] who will be priests and will always serve me by helping the king whom I will choose.
Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
36 All of your descendants who remain alive will have to go to that priest and ask him to give them money and food, and they will each have to say, “Please allow me to help the other priests, in order that I may [earn some money to] buy some food.”’”
Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”