< 1 Samuel 19 >

1 Then Saul urged all his servants and his son Jonathan to kill David. But Jonathan liked David very much.
Sauli anawuza mwana wake Yonatani ndi nduna zake zonse kuti aphe Davide. Koma Yonatani amamukonda kwambiri Davide.
2 So he warned David, “My father Saul is seeking for a way to kill you. So be careful. Tomorrow morning go and find a place to hide [in the field].
Choncho anawuza Davide kuti, “Abambo anga Sauli akufuna kukupha. Tsono uchenjere. Mmawa upite ukabisale ndipo ukakhale komweko.
3 I will ask my father to go out there with me. [While we are out there], I will talk to him about you. Then I will tell you everything that he tells me.” [So David did what Jonathan told him to do].
Ine ndidzapita ndi kukayima pafupi ndi abambo anga ku munda kumene iwe ukabisale. Ndipo ndidzayankhula ndi abambo anga za iwe ndipo chilichonse chimene ndikamve ndidzakuwuza.”
4 [The next morning], Jonathan spoke with his father, saying many good things about David. He said, “You should never do anything to harm your servant David! He has never done anything to harm you! Everything that he has done has helped you very much.
Tsono Yonatani anakanena zabwino za Davide kwa abambo ake Sauli ndipo anati, “Mfumu musachimwire mtumiki wanu Davide, sanakuchimwireni, koma amakuchitirani zabwino kwambiri.
5 He was in danger of being killed when he fought against [Goliath, the champion of] the Philistia [army. By enabling David to kill him], Yahweh won a great victory for all the people of Israel. You were very happy when you saw that. Why would you want to do anything now to harm David [RHQ]? There is no reason for you to kill him, because he has not done anything wrong!”
Iye anayika moyo wake pa chiswe pamene anapha Mfilisiti uja. Choncho Yehova anachita zazikulu popambanitsa Aisraeli pa nkhondo. Inu munaona zonsezo ndipo munakondwera. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwira munthu wosalakwa pofuna kupha Davide?”
6 Saul listened to what Jonathan said. Then Saul said, “I solemnly promise that just as certain as Yahweh lives, I will not kill David.”
Sauli anamvera mawu a Yonatani ndipo analumbira kuti, “Pali Yehova, Davide sadzaphedwa.”
7 Afterward, Jonathan summoned David and told him what he and Saul had said. Then Jonathan brought David to Saul, and David served Saul as he had done before.
Pambuyo pake Yonatani anayitana Davide namuwuza zonsezi. Choncho Yonatani anabwera naye Davide kwa Sauli ndipo ankamutumikira Sauliyo monga kale.
8 One day a war started again, and David [led his soldiers to] fight against the Philistia army. David’s [army] attacked them very furiously, with the result that the Philistia army ran away.
Panabukanso nkhondo ina ndipo Davide anapita ndi kukamenyana ndi Afilisti. Iye anawakantha mwamphamvu kotero kuti Afilisti anathawa.
9 But one day when sitting in his house, an evil spirit [sent] from Yahweh [suddenly] came upon Saul. While David was playing his harp [for Saul],
Tsiku lina mzimu woyipa uja unafikanso pa Sauli. Nthawi imeneyi nʼkuti Sauli uja ali mʼnyumba mwake, mkondo uli mʼdzanja lake ndi Davide akuyimba zeze,
10 Saul hurled his spear at David to try to fasten him to the wall. David (dodged/jumped to one side), and the spear did not hit him. The spear stuck in the wall, but that night David escaped.
Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.
11 Then Saul sent messengers to David’s house. He told them to watch the house and to kill David [while he was leaving the house] the following morning. But David’s wife Michal [saw them and] warned him, “To survive, you must run away tonight, because if you do not do that, you will be killed tomorrow!”
Usiku womwewo Sauli anatumiza anthu ku nyumba ya Davide kuti akamubisalire ndi kumupha mmamawa. Koma Mikala mkazi wake anamuchenjeza nati, “Ngati usiku uno supulumutsa moyo wako, mawa udzaphedwa.”
12 So she enabled David to climb out through a window, and he ran away and escaped.
Choncho Mikala anamutulutsira Davide pa zenera, ndipo anathawa ndi kupulumuka.
13 Then Michal took an idol and put it in the bed. She covered it with some [of David’s] clothes, and put some goat’s hair on the head of the idol.
Kenaka Mikala anatenga fano naligoneka pa bedi nayika pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwa fanolo ndipo analifunditsa nsalu.
14 When the messengers came [to the house the next morning], she told them that David was sick [and could not get out of bed].
Pamene amithenga a Sauli aja anafika kuti akamugwire Davide, Mikala anati, “Davide akudwala.”
15 [When they reported that to] Saul, he told them to go back to David’s house. He said to them, “Bring him to me lying on his bed, in order that I can kill him!”
Koma Sauli anatumanso anthuwo kuti akamuone Davide, nati, “Mubwere naye kuno ali pa bedi pomwepo kuti ndidzamuphe.”
16 But when those men entered David’s house, they saw that there was only an idol in the bed, with goat’s hair on its head.
Koma pamene anthuwo analowa, anangoona fano pa bedipo ndi pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwake.
17 [When they reported that to Saul, ] Saul [summoned] Michal [and] said to her, “Why did you trick me like that? You allowed my enemy to escape!” Michal replied to Saul, “David told me that if I did not help him escape, he would kill me!” [RHQ]
Tsono Sauli anafunsa Mikala kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandinamiza chotere polola kuti mdani wanga athawe?” Mikala anayankha kuti, “Davide anandiwuza kuti, ‘Ukapanda kutero ndikupha.’”
18 After David had escaped from Saul, he went to Samuel, who was [at his home] at Ramah. He told Samuel everything that Saul had done to [try to kill] him. Then David and Samuel went to Naioth, [which was a section] of [Ramah city], and they stayed there.
Choncho Davide anathawa napulumuka. Pambuyo pake anapita kwa Samueli ku Rama nakamuwuza zonse zimene Sauli anamuchita. Kenaka iye ndi Samueli anapita kukakhala ku Nayoti.
19 Someone told Saul that David was in Naioth.
Sauli anamva kuti, “Davide ali ku Nayoti ku Rama.”
20 So Saul sent some messengers to capture David. [When] those messengers [arrived in Ramah, they] met some men who were proclaiming ecstatic messages, and Samuel was there, as their leader. When Saul’s messengers met them, the Spirit of God took control of Saul’s men, and they also spoke ecstatically.
Choncho iye anatumiza anthu kuti akamugwire Davide. Koma anaona gulu la aneneri likulosera ndi Samueli akuwatsogolera. Pomwepo Mzimu wa Mulungu unawafikira ndipo nawonso anayamba kulosera.
21 When Saul heard about that, he sent messengers a third time, but they also started to speak ecstatically.
Sauli atamva zimenezi anatumizanso anthu ena, koma nawonso anayamba kulosa. Anatumanso anthu ena kachitatu, koma nawonso anayamba kulosa.
22 Finally, Saul himself went to Ramah. When he arrived at the well at [a place named] Secu, he asked people there, “Where are Samuel and David?” The people replied, “They are at Naioth in Ramah [city].”
Pomaliza Sauli mwini wake ananyamuka kupita ku Rama ndipo anafika ku chitsime chachikulu cha ku Seku. Ndipo anafunsa, “Samueli ndi Davide ali kuti?” Munthu wina anamuyankha kuti, “Ali ku Nayoti ku Rama.”
23 While Saul was walking toward Naioth, the Spirit of God also took control of him. [While he walked on], he continued speaking ecstatic messages until he came to Naioth.
Choncho Sauli anapita ku Nayoti ku Rama. Koma Mzimu wa Mulungu unafikanso pa iye ndipo ankalosa akuyenda mpaka anafika ku Nayoti.
24 There he took off his clothes, and he spoke messages from God in front of Samuel. He lay on the ground doing that all day and all night. That is the reason that [when people see someone doing something that is very unexpected, they think about what happened to Saul, and] they say, “We are surprised, like the people were surprised to see Saul [acting like] a prophet?” [RHQ]
Nayenso anavula zovala zake nayamba kulosa pamaso pa Samueli. Kenaka anagona wamaliseche tsiku lonse ndi usiku wonse. Nʼchifukwa chake anthu amati, “Kodi Sauli alinso mmodzi wa aneneri?”

< 1 Samuel 19 >