< 1 Samuel 15 >
1 [One day] Samuel said to Saul, “Yahweh sent me to appoint you to be the king of the Israeli people. So now listen to this message from Yahweh:
Samueli anawuza Sauli kuti, “Yehova anandituma ine kuti ndikudzozeni kukhala mfumu ya anthu ake, Aisraeli. Tsopano imvani zimene Yehova akunena.
2 Yahweh, [the commander] of the armies [of angels] has declared this: ‘I am going to punish [the descendants of] Amalek for [attacking] the Israeli people after the Israelis left Egypt.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzalanga Aamaleki chifukwa cha zimene anawachita Aisraeli. Paja iwo analimbana ndi Aisraeli pa njira pamene Aisraeliwo ankachoka ku Igupto.
3 So now go [with your army] and attack the Amalek people-group. Destroy them completely—destroy them and everything that belongs to them—the men and women, their children and infants, their cattle and sheep and camels and donkeys. Do not (spare any of them/allow any of them to remain alive)!’”
Tsopano pita kathire nkhondo Aamaleki ndi kuwononga kwathunthu zinthu zonse zimene ali nazo. Musakasiyeko munthu ndi mmodzi yemwe. Mukaphe amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ngʼombe ndi nkhosa, ngamira ndi abulu.’”
4 So Saul summoned the army, and they gathered at Telaim [town]. There were 200,000 soldiers. 10,000 of them were from Judah, [and the others were from the other Israeli tribes].
Kotero Sauli anayitana ankhondo ake nawawerenga ku Telaimu. Ankhondo oyenda pansi analipo 200,000 ndipo mwa iwowa 10,000 anali a fuko la Yuda.
5 Then Saul went [with his army] to a town where some of the Amalek people-group lived. [His army prepared to attack them suddenly by] hiding in the valley.
Sauli anapita ku mzinda wa Aamaleki nawubisalira mʼkhwawa.
6 Then Saul sent this message to the Ken people-group [who lived in that area]: “You acted kindly toward all our Israeli [ancestors] when they left Egypt. But we are going to kill all of the Amalek people-group, [because they opposed/attacked our ancestors]. So move away from where the Amalek people-group live. [If you do not move away], you will be killed when they are killed.” So [when] the Ken people-group [heard that, they immediately] left that area.
Tsono Sauli anawuza Akeni kuti, “Samukani, muchoke pakati pa Aamaleki kuti ine ndisakuwonongeni pamodzi ndi iwo pakuti inu munaonetsa kukoma mtima kwa Aisraeli onse pamene ankatuluka mʼdziko la Igupto,” Choncho Akeni anachoka pakati pa Aamaleki.
7 Then Saul’s [army] slaughtered the Amalek people-group, from Havilah [town in the east] to Shur [town in the west]. Shur was at the border [between Israel and] Egypt.
Tsono Sauli anakantha Aamaleki kuchokera ku Havila mpaka ku Suri, kummawa kwa Igupto.
8 Saul’s army captured Agag, the king of the Amalek people-group, but they killed everyone else.
Sauli anatenga Agagi mfumu ya Aamaleki, koma anthu ake onse anawapha ndi lupanga.
9 They not only (spared/did not kill) Agag, but they also took the best sheep and goats and cattle. They took everything that was good. They destroyed only the animals that they considered to be worthless.
Koma Sauli ndi ankhondo ake sanaphe Agagi, sanaphenso nkhosa ndi ngʼombe zabwino ngakhalenso ana angʼombe ndi ana ankhosa onenepa. Chilichonse chimene chinali chabwino sanachiphe. Koma zonse zimene zinali zoyipa ndi zachabechabe anaziwononga.
10 Then Yahweh said to Samuel,
Kenaka Yehova anawuza Samueli kuti,
11 “I am sorry that I appointed Saul to be your king, because he has turned away from me and has not obeyed what I commanded him to do.” Samuel was very disturbed/upset [when he heard that], and he cried out to Yahweh all that night.
“Ine ndikumva chisoni chifukwa ndinayika Sauli kukhala mfumu. Wabwerera mʼmbuyo, waleka kunditsata ndipo sanamvere malangizo anga.” Samueli anapsa mtima, ndipo analira kwa Yehova usiku wonse.
12 Early the next morning, Samuel got up and went to talk with Saul. But someone told Samuel, “Saul went to Camel [city], where he has set up a monument to honor himself. Now he has left there and gone down to Gilgal.”
Samueli anadzuka mmamawa ndipo anapita kukakumana ndi Sauli. Koma anthu anamuwuza kuti, “Sauli anabwera ku Karimeli, ndipo kumeneko wadziyimikira mwala wachikumbutso cha iye mwini. Tsopano wachokako ndipo wapita ku Giligala.”
13 When Samuel arrived [at Gilgal] he approached Saul, and Saul said to him, “I wish/desire that Yahweh will bless you! I have obeyed what Yahweh told me to do.”
Samueli atamupeza Sauli, Sauliyo anati kwa Samueli, “Yehova akudalitseni! Ndachita zonse zimene Yehova analamula.”
14 But Samuel replied, “If that is true, why is it that I hear cattle mooing and I hear sheep bleating?”
Koma Samueli anati, “Nanga bwanji ndikumva kulira kwa nkhosa ndi ngʼombe?”
15 Saul replied, “The soldiers took them from the Amalek people-group. They saved the best sheep and cattle, in order to offer them as sacrifices to Yahweh, your God. But we have completely destroyed all the others.”
Sauli anayankha, “Zimenezi Asilikali azitenga kuchokera kwa Aamaleki. Iwo anasungako nkhosa ndi ngʼombe zabwino kuti akapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma zina zonse anaziwononga.”
16 Samuel said to Saul, “Stop [talking]! Allow me to tell you what Yahweh said to me last night.” Saul replied, “Tell me [what he said].”
Koma Samueli anati kwa Sauli, “Khala chete! Ima ndikuwuze zimene Yehova wandiwuza usiku wathawu.” Sauli anayankha kuti, “Ndiwuzeni.”
17 Samuel said, “Previously you did not think that you were important. But now you have become [RHQ] the leader of the tribes of Israel. Yahweh appointed you to be their king.
Apo Samueli anati, “Munali wamngʼono pa maso pa anthu, koma tsopano mwasanduka mtsogoleri wa mafuko a Israeli. Yehova anakudzozani kuti mukhale mfumu yolamulira Aisraeli.
18 And Yahweh sent you to do something [for him]. He said to you, ‘Go and get rid of all those sinful people, the Amalek people-group. Attack them and kill all of them.’
Ndipo Yehova anakutumani kuti, ‘Pitani mukawononge kwathunthu Aamaleki, anthu oyipa aja. Mukachite nawo nkhondo mpaka kuwatheratu.’
19 So why did you not obey Yahweh [RHQ]? Why did your men take the best animals [RHQ]? Why did you do what Yahweh said was evil?” [RHQ]
Chifukwa chiyani simunamvere mawu a Yehova? Chifukwa chiyani munathamangira zofunkha ndi kuchita choyipira Yehova?”
20 Saul replied to Samuel, “Hey, I did what Yahweh sent me to do! I brought back King Agag, but we killed everyone else!
Koma Saulo anawuza Samueli kuti, “Ine ndinamveradi mawu a Yehova. Ndinapita kukachita zimene Yehova anandituma. Ndinabwera naye Agagi, mfumu ya Amaleki, koma Aamaleki ena onse anaphedwa.
21 My men brought back only the best sheep and cattle and other things, in order to sacrifice them to Yahweh your God here at Gilgal.”
Koma pa zofunkhazo anthu anatengapo nkhosa, ngʼombe ndi zabwino zina zoyenera kuwonongedwa kuti akapereke ngati nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ku Giligala.”
22 But Samuel replied, “Which [do you think] pleases Yahweh more, animals that are completely burned [on the altar] and other sacrifices, or people obeying him [SYN]? It is better to obey [Yahweh] than [to offer] sacrifices [to him]. It is better to pay attention to what he says than [to burn] the fat of rams, [even though God said they should be sacrificed to him].
Koma Samueli anayankha kuti, “Kodi Yehova amakondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zina kapena kumvera mawu a ake? Taona, kumvera ndi kwabwino kuposa nsembe, ndipo kutchera khutu ndi kwabwino kuposa kupereka mafuta a nkhosa.
23 To rebel [against God] is as sinful as doing sorcery/black magic, and being stubborn is as sinful as worshiping idols. So, because you disobeyed what Yahweh told you to do, he has declared that you will no longer be king.”
Pakuti kuwukira kuli ngati tchimo lowombeza, ndipo kukhala nkhutukumve kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Chifukwa mwakana mawu a Yehova. Iyenso wakukana kuti iweyo ukhale mfumu.”
24 Then Saul said to Samuel, “[Yes], I have sinned. I disobeyed what you told me to do, which is what Yahweh commanded. I did that because I was (afraid of/worried about) what my men would say [if I did not do what they wanted]. So I did what they demanded.
Tsono Sauli anati kwa Samueli, “Ine ndachimwa. Ndaphwanya malamulo a Yehova ndiponso malangizo anu. Ndinkaopa anthu ndipo ndinawamvera.
25 But now, please forgive me for having sinned. And come back with me [to where the people are] in order that I may worship Yahweh.”
Tsopano ndikukupemphani, khululukireni tchimo langa ndipo mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova.”
26 But Samuel replied, “No, I will not go back with you. You have rejected/disobeyed what Yahweh commanded you to do. So he has rejected you, [and declared that you will no longer] be the king of Israel. [So I do not want to talk any more with you].”
Koma Samueli anawuza Sauli kuti, “Ine sindibwerera nawe. Inu mwakana mawu a Yehova. Choncho Iyenso wakukanani kuti musakhale mfumu yolamulira Aisraeli.”
27 As Samuel turned to leave, Saul tried to stop him by grabbing the edge of Samuel’s robe, and it tore.
Samueli akutembenuka kuti azipita, Sauli anagwira mpendero wa mkanjo wake, ndipo unangʼambika.
28 Samuel said to him, “[You tore my robe! And] today Yahweh has torn away from you the kingdom of Israel! He will appoint someone else to be king, someone who is a better man than you are.
Samueli anati kwa iye, “Yehova wangʼamba ufumu wanu kuchoka kwa inu, ndipo waupereka kwa mnzanu woposa inu.
29 And since the one who is the glorious [God] of the Israeli people does not lie, he will not change (his mind/what he has said). Humans sometimes change their minds, but God does not do that, because he is not a human.”
Mulungu wa ulemerero wa Israeli sanama kapena kusintha maganizo ake; pakuti iye si munthu, kuti asinthe maganizo ake.”
30 Then Saul [pleaded again. He] said, “I know that I have sinned. But please honor me in front of the leaders of the Israeli people and in front of all the other Israeli people by coming back [to them] with me in order that I may worship Yahweh your God.”
Sauli anati, “Ine ndachimwa. Komabe, chonde mundilemekeze pamaso pa akuluakulu, anthu anga, ndiponso pamaso pa Israeli. Mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova Mulungu wanu.”
31 So Samuel finally agreed to do that, and they went together back [to where the people were], and Saul worshiped Yahweh there.
Pamenepo Samueli anabwerera ndi Sauli, ndipo Sauli anapembedza Yehova.
32 Then Samuel said, “Bring King Agag to me.” So they brought Agag to him. Agag was confidently expecting that they would spare him/not kill him. He was thinking, “Surely I will not have to endure an agonizing death!”
Kenaka Samueli anati, “Bwera nayeni kuno Agagi, mfumu ya Amaleki ija.” Choncho Agagi anapita kwa Samueli mokondwa chifukwa ankaganiza kuti, “Ndithu zowawa za imfa zapita.”
33 But Samuel said to him, “You have killed the sons of many women with your sword, so now your mother will no longer have a son.” And Samuel cut Agag into pieces [with his sword], there at Gilgal, in the presence of Yahweh.
Koma Samueli anati, “Monga momwe lupanga lako linasandutsira amayi kukhala wopanda ana, momwemonso amayi ako adzakhala opanda mwana pakati pa amayi.” Ndipo Samueli anapha Agagi pamaso pa Yehova ku Giligala.
34 Then Samuel left there and returned to his home in Ramah, and Saul went to his home in Gibeah.
Ndipo Samueli anapita ku Rama, koma Sauli anapita ku mudzi kwawo ku Gibeya wa Sauli.
35 Samuel never saw Saul again, but he was very sad about [what] Saul [had done]. And Yahweh was very sorry that he had appointed Saul to be the king of Israel.
Samueli sanamuonenso Sauli mpaka imfa yake ngakhale kuti ankamulira Sauliyo. Yehova anamva chisoni kuti anasankha Sauli kuti akhale mfumu ya Israeli.