< 1 Kings 1 >

1 When King David was very old [IDM, DOU], even though his servants put many blankets on top of him, he was unable to become warm.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 So they said to him, “Your Majesty, allow us to search for a young virgin who can stay with you and take care of you. She can sleep close to you and enable you to become warm.”
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 [The king gave them permission, ] so they searched throughout Israel for a beautiful young woman. They found a woman named Abishag, from Shunem [town], and brought her to the king.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 She was [truly] very beautiful. She took care of [DOU] the king, but the king did not have sexual relations with her.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 [After Absalom died], David’s oldest surviving son was Adonijah, whose mother was Haggith. He was a very handsome/good-looking man. But David had never rebuked him about anything he did. [After Absalom died, Adonijah thought that he would become king]. So he started to boast, saying “I will become king [now].” Then he provided for himself some chariots, and men to drive them, and horses [to pull them], and 50 men to run [as his bodyguards] in front of those chariots [wherever he went].
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 One day he conferred with Joab, [David’s army commander], and Abiathar the priest, and they promised/agreed to help/support Adonijah.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 But Zadok, who was also a priest, Benaiah [who had supervised David’s bodyguards], Nathan the prophet, Shimei and Rei, and David’s most capable soldiers refused to help/support Adonijah.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 One day Adonijah went to Snake Rock near En-Rogel [Spring, which is near Jerusalem], to sacrifice some sheep and oxen and fattened cattle. He invited most of his brothers, King David’s other sons, to come. He also invited all of the king’s officials from Judah to come to the celebration.
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 But he did not invite Nathan or Benaiah or the king’s most capable soldiers or his [younger/half]-brother Solomon.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Nathan [found out what they were doing, so he went to] Solomon’s mother Bathsheba [and] asked her, “Have you not heard that Haggith’s son Adonijah is declared himself to be the king? And King David does not know about it!
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 So if you want to save yourself and your son Solomon from being killed, allow me to tell you what you should do.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Go immediately to King David. Say to him, ‘Your Majesty, you solemnly promised me [RHQ] that my son Solomon would become the king after you [die], and that he would sit on your throne [and rule]. So why is it that Adonijah [has said that he] is now the king?’
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Then, while you are still talking to the king, I will come in and tell him that what you are saying to him [about Adonijah] is true.”
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 So Bathsheba went to see the king in his bedroom. He was very old, and Abishag was taking care of him.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Bathsheba bowed very low in front of the king, and the king asked her, “What do you want?”
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 She replied, “Your Majesty, you solemnly promised me, knowing that Yahweh our God [was listening] [IDM], that my son Solomon would become king after you [die], and that he would sit on your throne [and rule].
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 But now, believe it or not, Adonijah has become king, and you do not know anything about it.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 He has sacrificed a lot of oxen and fattened cattle and sheep, and he has invited all of your other sons to the celebration. He has also invited Abiathar the priest and Joab the commander of your army, but he did not invite your son Solomon.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Your Majesty, all the people [SYN] of Israel are expecting you to tell them who is the one who will become king after you are no longer the king.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 If you do not do that, what will happen is that after you die [EUP] people will consider that my son Solomon and I are rebelling, [and they will execute us because we did not help Adonijah to become king].”
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 While she was still talking to the king, Nathan came [to the palace].
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 The king’s servants/advisors told David, “Nathan the prophet has come.” So [Bathsheba left, and] Nathan went into where the king was and knelt down, with his face on the ground.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Then Nathan said, “Your Majesty, have you declared that Adonijah will become king after you are no longer the king?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 [I say that] because today he has gone down [to En-Rogel Spring] and has sacrificed a lot of oxen, fattened cattle, and sheep. And he has invited all of your other sons, Joab the army commander, and Abiathar the priest. They are all eating and drinking with him and saying ‘We hope/desire that King Adonijah will live a long time!’
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 But he did not invite me or Zadok the priest or Benaiah or Solomon.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Did you, as the king, say that they should do this without telling your other officials who you want to become king [MTY] after you are no longer the king?”
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Then [after Nathan left the room, ] King David said [to one of his servants], “Tell Bathsheba to come in here again.” So [he went and told her, and] she came in and stood in front of the king.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Then the king said, “Yahweh has rescued me from all my troubles. I promised you, with Yahweh the God whom we Israelis [worship] listening, that your son Solomon would be king after I am no longer the king. Today, as surely as Yahweh lives, [I solemnly declare that] I will do what I promised.”
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Bathsheba knelt down with her face on the ground and said, “Your Majesty, I hope/desire that you will live for many more years [HYP]!”
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Then King David said, “Summon Zadok the priest, Nathan the prophet, and Benaiah.” [So someone went and summoned them.] When they came in,
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 he said to them, “Put my son Solomon on my mule. Take him with my officials down to Gihon [Spring].
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 There, you two, Zadok and Nathan, should anoint him, [with olive oil to appoint him to be] the king of Israel. Then you must blow trumpets, and [all the people there must] shout, ‘We hope/desire that King Solomon will live for many years!’
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Then follow him back here, and he will come and sit on my throne. He will then become king instead of me. I have appointed him to be the ruler of [all the people of] Israel and of Judah.”
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Benaiah replied, “We will do that! We hope/wish that Yahweh, who is your God [and our God], will cause it to happen!
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 King David, Yahweh has helped you; we hope/wish that he will also help Solomon and enable him to become a greater king than you have been.”
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 So Zadok, Nathan, Benaiah, and the two groups of men who were the king’s bodyguards went and put Solomon on King David’s mule and escorted him down to Gihon [Spring].
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 There Zadok took the container of [olive] oil from the Sacred Tent and (anointed/poured some oil on) Solomon. Then the trumpets were blown, and all the people shouted, “We hope/wish that King Solomon will live for many years!”
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Then all the people followed him back up [to the city], shouting joyfully and playing flutes. They shouted very loudly, with the result that the ground shook.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 When Adonijah and all (his guests/the people whom he had invited) were finishing eating at their celebration, they heard the noise. When Joab heard the sound of the trumpets, he asked, “What is causing all that noise in the city?”
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 While he was still speaking, Jonathan, the son of Abiathar the priest, arrived. Adonijah said, “Come in! You are a man whom we can trust, so you must be bringing us good news!”
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Jonathan replied, “No, [I do not have good news]! His Majesty, King David, has caused Solomon to be the king!
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 He sent Zadok, Nathan, Benaiah, and his own group of bodyguards to go with Solomon. They put Solomon on King David’s mule.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 They [went down to] Gihon [Spring], and there Zadok and Nathan anointed him to become the king. Now they have returned from there to the city, shouting joyfully. That is why there is that great/loud noise that you are hearing.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 So Solomon is now our king [MTY].
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Furthermore, the palace officials came to His Majesty, King David, to tell him that they approved of what he had done. They said, ‘We wish/hope that our God will enable Solomon [MTY] to become more famous than you have been and enable him to be a better king than you have been.’ When they said that, the king, lying on his bed, bowed his head to worship [Yahweh].
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Then he said, ‘I praise Yahweh, the God whom we Israelis [worship], because he has allowed one of my sons to become the king today, and has permitted me to see it happen.’”
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Then all of Adonijah’s guests (trembled/were afraid), so they all immediately got up and left and scattered.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Adonijah was afraid of what Solomon [would do], so he went [to the Sacred Tent] and grabbed the projections at the corners of the altar, [because he knew that no one would kill him there].
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 But someone told Solomon, “Hey/Listen, Adonijah is afraid of you, so he [has gone to the Sacred Tent and] is holding on to the corners of the altar. He is saying, ‘[Before I leave, ] I want King Solomon to solemnly promise that he will not command that I be executed.’”
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Solomon replied, “If he proves that he is loyal to me, I will not harm him at all [IDM]. But if he does anything that is wrong, he will be executed.”
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 So King Solomon sent [some men to Adonijah], and they brought him back from the altar. He came to Solomon and bowed down in front of him. Then Solomon said to him, “Go home.”
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Kings 1 >