< 1 Kings 12 >
1 All [HYP] the people of [northern] Israel went to Shechem [city] in order to appoint Rehoboam to be their king. So Rehoboam also went there.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse nʼkuti atapita kumeneko kukamulonga ufumu.
2 When Jeroboam, who was still in Egypt, heard about that, he returned from Egypt [to Israel].
Yeroboamu mwana wa Nebati anamva zimenezi. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamuyo akukhala ku Igupto, pakuti atathawa Mfumu Solomoni iyeyo anakakhala ku Igupto.
3 The [leaders of the northern tribes] summoned him, and they went together [to talk] to Rehoboam. They said to him,
Tsono anthu anayitanitsa Yeroboamu, ndipo iye pamodzi ndi gulu lonse la ku Israeli anapita kwa Rehobowamu ndipo anamuwuza kuti,
4 “Your father [Solomon] forced us to work very hard [MET] for him. If you (lighten these loads/do not force us to work that hard), and if you charge us less taxes than we were paying to him, we will serve you [faithfully].”
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa kwambiri, koma inu chepetsani ntchito yowawa pa ife ndipo peputsani goli lolemetsa limene anatisenzetsa. Mukatero tidzakutumikirani.”
5 He replied, “Go away, and come back three days from now [and I will give you my answer].” So those leaders and Jeroboam left.
Rehobowamu anayankha kuti, “Pitani, ndipo pakatha masiku atatu, mudzabwerenso.” Choncho anthuwo anapitadi.
6 Then King Rehoboam consulted the older men who had advised his father Solomon while he was still living. He asked them, “What shall I say to answer those men?”
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapempha nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira Solomoni abambo ake pamene anali ndi moyo. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu amenewa?”
7 They replied, “If you want to serve your people well, speak kindly to those men when you reply to them. If you do that, your people will always serve you faithfully.”
Iwo anayankha kuti, “Ngati lero mudzakhala mtumiki wa anthu amenewa ndi kuwatumikira ndipo mukawayankha bwino, iwowo adzakhala atumiki anu nthawi zonse.”
8 But he ignored what the older men advised him to do. Instead, he consulted the younger men who had grown up with him, who were now (his advisors/the ones who told him what would be good to do).
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakuluwo anamupatsa ndipo anafunsira nzeru kwa anyamata anzake amene anakulira nawo limodzi omwe ankamutumikira.
9 He said to them, “What should I say to the men who are asking me to reduce the [work and taxes] that my father required from them?”
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ngotani? Kodi ndiwayankhe chiyani anthu amene akunena kwa ine kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anatisenzetsa’?”
10 They replied, “This is what you should tell them: ‘My little finger is thicker than my father’s waist.
Anyamata anzake amene anakula nawo limodzi aja anamuyankha kuti, “Anthu amene ananena kwa iwe kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa, koma inu peputsani goli lathu,’ uwawuze kuti ‘Chala changa chakanise nʼchachikulu kupambana chiwuno cha abambo anga.
11 What I mean is that my father required you [to work hard and pay high taxes]. But I will make those loads heavier. [It was as though] my father whipped you, but [it will be as though] I will whip you with whips that have pieces of metal in them.’”
Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 So three days later, Jeroboam and all the leaders came to Rehoboam again, as he had told them to do.
Patapita masiku atatu, Yeroboamu pamodzi ndi anthu onse anabwera kwa Rehobowamu, monga momwe inanenera mfumu kuti, “Mudzabwere pakatha masiku atatu.”
13 The king ignored the advice of the older men and spoke harshly to the Israeli leaders.
Mfumuyo inawayankha anthuwo mwankhanza. Kukana malangizo amene akuluakulu anayipatsa.
14 [He told them what the younger men had advised.] He said, “My father put heavy burdens [of work and taxes] on you, but I will put heavier burdens on you. [It was as though] he beat you with whips, but I will beat you with whips that have pieces of metal in them!”
Anatsatira malangizo amene anyamata anzake anamupatsa ndipo anati “Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa. Ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 So the king did not pay any attention to the Israeli leaders. But this happened in order that what Yahweh wanted would occur, what he had told the prophet Ahijah about Jeroboam [becoming king of the ten tribes].
Choncho mfumu sinamvere pempho la anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Yehova, kukwaniritsa mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 When the Israeli leaders realized that the king did not pay any attention to what they said, they shouted, “We do not [RHQ] want anything to do with this descendant of King David! We will not pay attention to what this grandson of Jesse says! You people of Israel, let’s go home! As for this descendant of David [MTY], he can rule his own kingdom [MTY]!” So the Israeli leaders returned to their homes.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kumva zopempha zawo, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, ndi gawo lanjinso mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli, bwererani ku matenti anu! Ziyangʼanira nyumba yako, Iwe Davide!” Kotero Aisraeli anachoka napita ku nyumba zawo.
17 And [after that, ] the [only Israeli] people whom Rehoboam ruled over were those who lived in the territory of [the tribe of] Judah.
Koma Aisraeli amene ankakhala mʼmizinda ya Yuda ankalamuliridwa ndi Rehobowamu.
18 Then King Rehoboam sent Adoniram [to talk to the Israeli people]. Adoniram was the man who supervised [all the men who were] forced to work [for Rehoboam]. But the Israeli people killed him by throwing stones at him. When that happened, King Rehoboam quickly got in his chariot and escaped to Jerusalem.
Mfumu Rehobowamu anatuma Adoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli onse anamugeda ndi miyala mpaka kumupha. Koma Mfumu Rehobowamu anakwera msangamsanga galeta wake nathawira ku Yerusalemu.
19 Ever since that time, the people of [the northern tribes of] Israel have been rebelling against the descendants [MTY] of [King] David.
Choncho Aisraeli akhala akuwukira nyumba ya Davide mpaka lero lino.
20 When the Israeli people heard that Jeroboam had returned [from Egypt], they invited him to come to a meeting, and there they appointed him to be the king of Israel. Only the people of the tribes of Judah [and Benjamin] continued to be loyal to [the kings descended from King] [MTY] David.
Aisraeli onse atamva kuti Yeroboamu wabwerera kuchokera ku Igupto, anatumiza mawu okamuyitana kuti abwere ku msonkhano ndipo anamuyika kukhala mfumu ya Aisraeli onse. Fuko la Yuda lokha ndi lomwe linkatsatira nyumba ya Davide.
21 When Rehoboam arrived in Jerusalem, he gathered 180,000 of the best soldiers from the tribes [MTY] of Judah and Benjamin. He wanted them to fight against the northern tribes of [MTY] Israel [and defeat them], in order that he could [rule all the tribes of] his kingdom again.
Rehobowamu atafika ku Yerusalemu, anasonkhanitsa nyumba yonse ya Yuda ndi fuko la Benjamini, nasankha ankhondo okwanira 180,000, kuti akamenyane ndi nyumba ya Israeli kuti amubwezere Rehobowamu mwana wa Solomoni ufumu wake.
22 But God spoke to the prophet Shemaiah and said this to him:
Koma Mulungu anayankhula ndi Semaya, munthu wa Mulungu kuti,
23 “Go and tell this to [Solomon’s son] Rehoboam, the king of Judah, and to all the people of the tribes of Judah and Benjamin and the people from the northern tribe who live in Judah:
“Nena kwa Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda, kwa nyumba yonse ya Yuda ndi Benjamini, ndiponso kwa anthu ena onse kuti,
24 ‘Yahweh says that you must not go to fight against your own relatives, the people of Israel. All of you must go home. What has happened is what Yahweh wanted to happen.’” [So Shemaiah went and told that to them, ] and they all paid attention to what Yahweh had commanded them to do, and they went home.
‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu Aisraeli. Aliyense wa inu abwerere kwawo, pakuti zimenezi ndachita ndine.’” Choncho anthuwo anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera kwawo, monga analamulira Yehova.
25 Then Jeroboam’s workers built [walls around] Shechem [city] in the hilly area [where the descendants] of Ephraim [lived], and he ruled from there for a while. He and his workers then left there and went to Peniel [town], and they built walls around that town.
Tsono Yeroboamu anamanga mzinda wa Sekemu mʼdziko la mapiri la Efereimu ndipo anakhala kumeneko. Kuchokera kumeneko anapita kukamanga mzinda wa Penueli.
26 Then Jeroboam said to himself, “If my people [continue to] go to Jerusalem and offer sacrifices to Yahweh at the temple there, soon they will again become loyal to Rehoboam, the king of Judah [DOU], and they will kill me.”
Yeroboamu anaganiza mu mtima mwake kuti, “Ndithu, ufumuwu udzabwereranso ku nyumba ya Davide.
Ngati anthuwa azipitabe kukapereka nsembe ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, adzayambanso kutsatira mbuye wawo Rehobowamu, mfumu ya Yuda. Adzandipha ndi kubwerera kwa Mfumu Rehobowamu.”
28 So he consulted [his advisors, and then he did what they suggested]. He [told his workers to] make gold [statues of] two calves. Then he said to the people, “You have been going to Jerusalem [to worship] for a long time. It is a big trouble for you to continue going there. You people of Israel, look! These statues are the gods that brought our [ancestors] up from Egypt! [So you can worship these, here!]”
Itapempha nzeru, mfumuyo inapanga mafano awiri a ana angʼombe. Mfumuyo inati kwa anthuwo, “Mwakhala mukupita ku Yerusalemu nthawi yayitali. Iwe Israeli, nayi milungu yako imene inakutulutsa mʼdziko la Igupto.”
29 He [told his workers to] place one of the statues in Bethel [city in the south] and one in Dan [city in the north].
Fano lina analiyika ku Beteli ndipo lina analiyika ku Dani.
30 So [what Jeroboam did caused] the people [to] sin. Some of them went and worshiped the calf at Bethel, and others went and worshiped the other calf at Dan.
Ndipo zimenezi zinachimwitsa anthu pakuti anthu ankapita mpaka ku Dani kukapembedza fano limene linali kumeneko.
31 [Moses had declared that only men from the tribe of Levi would be priests, but] Jeroboam also told his workers to build shrines on hilltops, and then he appointed men who were not from the tribe of Levi to be priests.
Yeroboamu anamanga Nyumba za Mulungu pa malo azipembedzo nasankha ansembe kuchokera pakati pa anthu wamba, ngakhale sanali Alevi.
32 He also appointed Adonijah and two priests, Elishama and Jehoram. They had a celebration at the end of October, like the celebration [of Living in Temporary Shelters] that occurred in Judah [each year]. On the altar [that they built] in Bethel, he offered sacrifices to the gold statues of calves that they had made, and he stationed the priests there at the shrines that his workers had built.
Iye anakhazikitsa chikondwerero pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, lofanana ndi tsiku la chikondwerero cha ku Yuda, ndipo ankapereka nsembe pa guwa. Izi ankachita ku Beteli, kupereka nsembe kwa ana angʼombe amene anapanga. Ndipo ku Beteliko anayikako ansembe pa malo achipembedzo amene anamanga.
33 Jeroboam went up to that altar on that day in October which he himself had chosen. There on that altar he burned incense [to be a sacrifice]. And he declared that the people should celebrate that festival [on that same day every year].
Tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, mwezi umene anawusankha yekha, anapereka nsembe pa guwa limene analimanga ku Beteli. Motero anakhazikitsa chikondwerero cha Aisraeli ndipo iye ankapita kukapereka nsembe yofukiza lubani pa guwa.