< 1 Corinthians 2 >

1 My fellow believers, when I came to you, I proclaimed to you the message that God had revealed to me. But I did not proclaim it using eloquent words that would make people think highly of me, nor did I argue in a way that unbelievers would think was very wise.
Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu.
2 I did that because I decided that I would speak only about Jesus Christ. Specifically, I told you [what he accomplished for us when] he was killed by being nailed {[when they] killed him by nailing him} to a cross.
Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo.
3 Furthermore, when I was with you, I felt that I was not adequate [to do what Christ wanted me to do]. I was afraid [that I would not be able to do it], and because of that I was trembling very much.
Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri.
4 When I taught you and preached to you, I did not speak words that [unbelievers would consider] [IRO] wise in order to convince them that my message was true. Instead, [God’s] Spirit showed that it was true by [enabling me to] powerfully [perform miracles].
Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu,
5 [I taught and preached that way] in order that you might believe [my message], not because you heard words that people [considered to be] [IRO] wise, but [because you recognized] God’s power.
kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.
6 I do teach a message that people who are [spiritually] mature [consider to] be wise. But I do not teach a message that unbelievers [consider to be] wise. I also do not teach a message that unbelieving rulers in the world consider to be wise. [What they think about it does not matter], because [some day] (they will lose their power/not be ruling any more). (aiōn g165)
Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. (aiōn g165)
7 Instead, I teach about what God planned wisely [long ago]. It is something that people did not know about previously because [God] did not reveal it previously. But God determined before he created the world that he would greatly benefit us by his wise plan. (aiōn g165)
Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. (aiōn g165)
8 None of those who rule this world knew that wise plan. If they had known it, they would not have nailed our wonderful Lord to the cross. (aiōn g165)
Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. (aiōn g165)
9 But [we believers need to remember these words that a prophet] wrote [in the Scriptures]: Things that no one has ever seen, things that no one ever heard, things that no one ever thought could happen, those are the things that God has prepared for those who love him.
Komabe monga zalembedwa kuti, “Palibe diso linaona, palibe khutu linamva, palibe amene anaganizira, zimene Mulungu anakonzera amene amukonda”
10 God has caused his Spirit to reveal those things to us [(inc)] believers. His Spirit can do that because he knows thoroughly the meaning of all things. He even knows the things about God that are very difficult to understand.
koma Mulungu waululira ife mwa Mzimu wake. Mzimu amafufuza zinthu zonse, ndi zozama za Mulungu zomwe.
11 Only a person himself (OR, a person’s spirit) knows what he is thinking. Similarly, only God’s Spirit knows what God is thinking.
Kodi ndani mwa anthu angadziwe maganizo a munthu wina, kupatula mzimu wa munthuyo wokhala mʼkati mwake? Chimodzimodzinso palibe amene adziwa maganizo a Mulungu kupatula Mzimu wa Mulunguyo.
12 It was not the ideas that unbelievers teach that we accepted. Instead, it was the Spirit who came from God that we received, in order that we might know the things that God has freely done for us.
Mzimu amene tinalandira ife si wa dziko lapansi koma Mzimu wochokera kwa Mulungu wotipatsa ife mwaulere.
13 Those are the things that I tell you about. As I do that, I do not tell you things that someone [whom others thought] was [IRO] wise taught me. Instead, I tell you truths that [God’s] Spirit taught [me], and I explain those spiritual truths to people whose thinking is guided by God’s Spirit (OR, I teach spiritual [truths to] spiritual [people]).
Izi ndi zimene timayankhula osati mʼmawu wophunzitsidwa ndi nzeru za munthu koma mʼmawu wophunzitsidwa ndi Mzimu, kufotokozera zoonadi zauzimu mʼmawu auzimu.
14 Those who are unbelievers reject the truths that [God’s] Spirit teaches us [(inc)], because they [consider those truths to be] foolish. They cannot understand them, because it is God’s Spirit who enables us to evaluate those truths correctly, [and those people do not have God’s Spirit].
Munthu wopanda Mzimu savomereza zinthu zimene zichokera kwa Mzimu wa Mulungu, popeza ndi zopusa kwa iyeyo, ndipo sangazimvetsetse chifukwa zimazindikirika mwa Mzimu.
15 We who have God’s Spirit can judge correctly the [value of] all truths [that the Spirit reveals], but [unbelievers] cannot evaluate us correctly.
Munthu wauzimu amaweruza pa zinthu zonse, koma iye mwini saweruzidwa ndi munthu aliyense.
16 As [one of our prophets wrote: ] No human [RHQ] has known what the Lord is thinking. No human [RHQ] is able to instruct him. But we believers are able to think about things [MTY] in the way that Christ thinks about them.
Pakuti “Ndani anadziwa malingaliro a Ambuye, kuti akhoza kumulangiza Iye.” Koma tili nawo mtima wa Khristu.

< 1 Corinthians 2 >