< 1 Chronicles 28 >

1 David summoned all the leaders of Israel to come to Jerusalem. He summoned the leaders of the tribes, the leaders/commanders of the groups that worked for the king, the commanders of 100 soldiers, the commanders of 1,000 soldiers, those who were in charge of the property and livestock that belonged to the king and his sons, all the palace officials, and his mighty soldiers and bravest warriors.
Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
2 David stood up and said, “My fellow Israelis, listen to me. I wanted [IDM] to build a temple to be a place where we would put the Sacred Chest of Yahweh, where it would stay permanently. And I made plans to build it.
Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
3 But God said to me, ‘You are not the one who will [arrange to] build a temple for me [MTY], because you are a warrior and you have killed many people [MTY] [in battles].’
Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
4 “But Yahweh, the God to whom we Israelis belong, had chosen me and my descendants to be the kings of Israel forever. [First] he chose the tribe of Judah, and from the people [MTY] of Judah he chose my family, and from my father’s sons he chose me to be the king over all of Israel.
“Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
5 Yahweh has given me many sons, but from them he chose my son Solomon to be the next king to rule [MTY] the kingdom of Israel.
Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
6 He said to me, ‘Solomon your son is the one who will [arrange to] build my temple and the courtyards around it, because I have chosen him to be [like] my son and I will be [like] [MET] his father.
Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
7 I will enable his kingdom to endure forever if he continues to obey my laws and commands, like you are doing now.’
Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
8 “So now, while all [you people of] Israel, all of you who belong to Yahweh, are watching, and while God is listening, I command you [leaders] to carefully obey all the commands of Yahweh our God, in order that you may continue to possess this good land and enable your descendants to inherit it forever.
“Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
9 “And you, my son Solomon, must know God like I know him, and you must serve him faithfully and because you want to. You must do that because he knows what everyone is thinking and he understands the reasons that people do what they do. If you seek [to know] him, he will heed your prayers. But if you abandon/reject him, he will abandon/reject you forever.
“Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
10 Yahweh has chosen you to [arrange to] build a temple for him. So think about [what I have said], and be strong and do what [he is wanting you to do].”
Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
11 Then David gave to his son Solomon [the scroll on which were written] the plans for the main rooms of the temple, its porch, its storerooms, all the other upper and lower rooms, and the Very Holy Place where God would forgive the sins that people had committed.
Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
12 David wrote for him the plans that God’s Spirit had put into his mind for building the courtyards and all the rooms that surrounded the temple, including the room where the money and other valuable things that were dedicated to God would be kept.
Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
13 He gave Solomon instructions for the groups of priests and other descendants of Levi, about all the work that they must do to serve in Yahweh’s temple, and about taking care of all the things that would be used in the work at the temple.
Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
14 He wrote down how much gold and how much silver should be used to make all the items in the temple:
Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
15 how much gold for making the gold lampstands and the lamps, how much silver to make the silver lamps and lampstands,
kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
16 how much gold for making the table on which [the priests would put] the sacred bread, how much silver to use to make the other tables,
kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
17 how much pure gold for the meat forks and the bowls and the cups, how much gold for each gold dish, how much silver for each silver dish,
muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
18 and how much pure gold to make the altar for [burning] incense. He also gave to Solomon his plans for making the golden statues of winged creatures that would be above the Sacred Chest of Yahweh, [like] a chariot for him.
ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
19 Then David said, “I have written [all these plans] while Yahweh was directing [MTY] me. He has enabled me to understand all the details of his plan [for the temple that is to be built].”
Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
20 David also said to his son Solomon, “Be strong and courageous, and do this work. Do not be afraid or discouraged, because Yahweh our God will be with/helping you. He will not fail [to help] you or abandon you until you finish all the work of making his temple.
Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
21 The groups of priests and [other] descendants of Levi are ready to begin their work at the temple, and every man who has a special skill will help you in all the work. And my officials and the other people will obey you, whatever you command them to do.”
Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”

< 1 Chronicles 28 >