< Romans 6 >
1 WHAT, then, shall we say, Let us remain in sin, that grace may abound?
Nanga tinene chiyani? Kodi tipitirire kuchimwa kuti chisomo chichulukebe?
2 Not so. For how shall they who are dead to sin live yet in it?
Ayi. Mʼnjira iliyonse! Popeza tinafa ku tchimo, nanga tidzapitirira bwanji kukhalabe mʼmenemo?
3 Or do you not know, that they who have been baptized into Jeshu Meshiha, into his death have been baptized?
Kodi simukudziwa kuti tonse amene tinabatizidwa mwa Khristu Yesu tinabatizidwa mu imfa yake?
4 For we are buried with him by baptism into death; that as Jeshu Meshiha arose from among the dead by the glory of his Father, so also we in a new life shall walk.
Chifukwa chake ife tinayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Iye mwa ubatizo. Tinalowa mu imfa ndi cholinga choti monga momwe Khristu anaukitsidwa kwa akufa ndi ulemerero wa Atate, ifenso tikakhale mʼmoyo watsopano.
5 For if together we have been planted with him in the likeness of his death, so also in his resurrection shall we be.
Pakuti ngati ife tinakhala amodzi ndi Iye mu imfa yake, tidzakhalanso ndithu amodzi ndi Iye mu kuuka kwake.
6 For we know that our old man is crucified with him, that the body of sin might be abolished, that more we should not serve sin.
Ife tikudziwa kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye kuti thupi la uchimo likhale lopanda mphamvu ndi kuti tisakakhalenso akapolo a tchimo
7 For he who is dead is set free from sin.
chifukwa aliyense amene anafa anamasuka ku tchimo.
8 If then we are dead with the Meshiha, we believe that with him, with the Meshiha, we shall live:
Koma ngati tinafa pamodzi ndi Khristu, tikhulupirira kuti tidzakhalanso ndi moyo pamodzi ndi Iye.
9 for we know that the Meshiha rose from among the dead, and no more dieth, nor hath death dominion over him.
Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye.
10 For he who died on account of sin died once, and he who liveth liveth unto Aloha;
Imfa imene Iye anafa, anafa ku tchimo kamodzi kokha, koma moyo umene akhala ndi wa kwa Mulungu.
11 so also reckon yourselves to be dead unto sin, and alive unto Aloha by our Lord Jeshu Meshiha.
Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu.
12 Let not sin then reign in your dead body, as that you may obey the lusts of it:
Nʼchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa.
13 nor prepare your members the instruments of iniquity unto sin, but prepare yourselves for Aloha, as men who from the dead have been made alive, and your members instruments to be for the righteousness of Aloha.
Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. Mʼmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo.
14 For sin shall not rule over you; for you are not under law, but under grace.
Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.
15 What, then, shall we sin, because we are not under law, but under grace? Not so.
Nʼchiyani tsono? Kodi tidzichimwa chifukwa sitikulamulidwa ndi Malamulo koma chisomo? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi!
16 Know you not, that to whomsoever you prepare yourselves to obey him unto service, of him you are the servants, of him whom you obey; whether of sin, or of the hearing of the ear of righteousness?
Kodi inu simudziwa kuti pamene mudzipereka kwa wina wake, kumumvera ngati akapolo, ndinu akapolo a amene mumumvera? Ngati ndinu akapolo a tchimo mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo akumvera, mudzakhala olungama pamaso pake.
17 But praise to Aloha that you were the servants of sin, but have obeyed from the heart the form of doctrine to which you have been delivered.
Koma ayamikidwe Mulungu pakuti ngakhale munali akapolo a tchimo, munamvera ndi mtima wonse chiphunzitso chimene munalandira.
18 And when you were made free from sin, you became obedient to righteousness.
Inu munamasulidwa ku tchimo ndipo tsopano mwasanduka akapolo achilungamo.
19 As among men I speak, because of the infirmity of your flesh, that as you have prepared your members for the service of uncleanness and of iniquity, so also now prepare ye your members for the service of righteousness and of holiness.
Ine ndikufanizira zinthu za tsiku ndi tsiku chifukwa chikhalidwe chanu nʼchofowoka. Monga momwe munkapereka ziwalo za matupi kukhala akapolo a zonyansa ndi makhalidwe oyipa, zimene zimanka zichulukirabe, choncho tsopano dziperekeni ziwalozo kuti zikhale akapolo achilungamo ndi a kuyera mtima.
20 For when you were the servants of sin, you were free from righteousness.
Pomwe munali akapolo atchimo, simunkalabadira za chilungamo.
21 And what product had you then from that of which to-day you are ashamed? For the end of it is death.
Kodi munapeza phindu lanji pochita zinthu zimenezi, zomwe tsopano mukuchita nazo manyazi? Zinthu zimenezo zotsatira zake ndi imfa!
22 And now made free from sin, and become servants to Aloha, you have holy fruits, of which the end is the life of eternity. (aiōnios )
Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. (aiōnios )
23 For the wages of sin is death; and the gift of Aloha the life of eternity by our Lord Jeshu Meshiha. (aiōnios )
Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōnios )