< Revelation 21 >

1 AND I saw new heavens and a new earth: for the first heaven and the first earth had gone, and the sea was no more.
Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
2 And the holy city, Urishlem the new, I saw descending from heaven from Aloha, prepared as the bride is decked for her husband.
Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
3 And I heard a great voice from heaven, saying, Behold, the tabernacle of Aloha is with men; and he will dwell with them, and they shall be his people; and Aloha himself will be with them, and will be their God.
Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
4 And every tear shall be wiped away from their eyes, and death shall be no more; nor sorrow, nor clamour, nor pain, shall be any more; for the former things are passed away.
‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
5 And He who sat upon the throne said, Behold, I make all things new. And he said, Write: for these are the faithful and true words of Aloha.
Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
6 And he said to me, I am Olaph and Thau, the Beginning and the End. To him who thirsteth I will give of the water of life freely.
Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
7 He who overcometh shall inherit these; and I will be to him Aloha, and he shall be my son.
Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
8 But the fearful, and the faithless, and sinners, and the unclean, and murderers, and fornicators, and sorcerers, and servers of idols, and all liars, (shall have) their portion in the lake which burneth with fire and sulphur; which is the second death. (Limnē Pyr g3041 g4442)
Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr g3041 g4442)
9 And one of the seven angels who had the seven vials full of the seven last plagues, came and spake with me. saying, Come, I will show thee the bride, the wife of the Lamb.
Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
10 And he led me in spirit upon a great and high mountain, and showed me the holy city Urishlem, descending from heaven from Aloha;
Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
11 having the glory of Aloha, as the clearness of light, like a stone of great price, as the stone Jaspon, resembling crystallos;
Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
12 having a wall great and high, which had twelve gates, and names written upon them, which are the names of the twelve tribes of the sons of Israel.
Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
13 On the east three gates, and on the north three gates, and on the south three gates, and on the west three gates.
Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
14 And the wall of the city had twelve foundations; and upon them the twelve names of the twelve apostles of the Lamb.
Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
15 And he who talked with me had a measure, a rod of gold, that he might measure the city and the gates and the walls thereof.
Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
16 And the city was set four-square, and the length of it was as the breadth: and he measured the city with the rod, upon twelve stadia of twelve thousand. And the length and the breadth and the height of it are equal.
Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
17 And he measured the wall of it, an hundred and forty and four measures of the cubits of a man, that is, of the angel.
Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
18 And the structure of the wall of it is (of) jaspis, and the city is of pure gold, like pure brightness.
Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
19 And the foundations of the wall of the city were adorned with every precious stone: the first foundation was of jaspis, the second sathphiros, the third caledon, the fourth zmoragdo,
Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
20 the fifth sardonicos, the sixth sardion, the seventh crisuthilos, the eighth berulla, the ninth topadion, the tenth chrosoposius, the eleventh hyacinthos, the twelfth amuthistos.
achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
21 And the twelve gates are twelve pearls, each of every one of the gates (a pearl), and each of every one of the pearls (a gate). And the wide street of the city was of pure gold as the brightness of light.
Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
22 And a temple I saw not in it; for the Lord, the Omnipotent, is the temple thereof and the Lamb.
Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
23 And the city hath no need of the sun nor of the moon to enlighten it; for the glory of Aloha illuminateth it, and the light thereof is the Lamb.
Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
24 And the nations of the saved walk by the light of it, and the kings of the earth bring their glory and the honour of the nations into it.
Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
25 And the gates of it shall not be shut by day, for night is not there.
Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
26 And they shall bring the glory and honour of the nations into it;
Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
27 and nothing shall enter into it that defileth, nor that worketh uncleanness; but they who are written in the book of life of the Lamb.
Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.

< Revelation 21 >