< Luke 1 >
1 BECAUSE many have willed to record histories of those transactions of which we are persuaded, according to that which they have delivered to us,
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
2 (they) who from the first were eye-witnesses and ministers of his doctrine;
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 it appeared also to me, that having been intimately near to them all, I should record every thing in its order for thee, illustrious Theophile,
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 that thou mayest know the truth of those doctrines in which thou hast been instructed.
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 THERE was in the days of Herodes, king of the Jihudoyee, a certain priest whose name was Zakaria, of the service of the house of Abia, and his wife (was) of the daughters of Aharun; her name was Elishaba.
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 And they were both just before Aloha, and walked in all his commandments, and in the righteousness of the Lord, without blame.
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 But they had no son because Elishaba was barren, and both had become many in their days.
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 But it was while he was acting-as-priest in the order of his ministry before Aloha,
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 according to the custom of the priesthood he came to set on incense, and entered into the temple of the Lord.
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 And all the congregation of the people were praying without at the time of incense.
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 And there appeared to him, to Zakaria, the angel of the Lord, standing on the right hand of the altar of incense.
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 And Zakaria trembled when he saw him, and fear fell upon him.
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 And the angel said to him, Fear not, Zakaria, for thy prayer is heard, and thy wife Elishaba shall bear thee a son, and thou shalt call his name Juchanon.
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 And to thee shall be joy and exultation, and many shall rejoice in his birth:
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 for he shall be great before the Lord, and wine and strong liquor shall he not drink, and with the Spirit of Holiness shall he be filled, from the womb of his mother.
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 And many of the sons of Isroel shall he convert to the Lord their Aloha.
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 And he shall go before him in the spirit and the power of Elia the prophet, to turn the hearts of the fathers unto the children, and those who believe not to the knowledge of the righteous, and to prepare for the Lord a perfect people.
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 And Zakaria said to the angel, How shall I know this? for I am old, and my wife many in her days.
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 And the angel answered and said to him, I am Gabriel, I stand before Aloha, and I have been sent to speak with thee and to announce to thee these things.
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 From henceforth thou shalt be dumb, and shalt not be able to speak, till the day when these things shall be done, because thou hast not believed these words, which shall be fulfilled in their time.
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 But the people were standing, and expecting Zakaria. and were wondering at his delay in the temple.
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 But when Zakaria had come forth, he could not speak to them; and he made them understand that he had seen a vision in the temple, and signing he signed to them, and remained dumb.
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 And when the days of his service were fulfilled, he came to his house.
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 And it was after those days Elishaba his wife conceived, and she secluded herself five months.
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 And she said, These things hath the Lord done for me in the days of my desolation, to take away my reproach from among the children of men.
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 BUT in the sixth month Gabriel the angel was sent from before Aloha to Galila, to a city whose name (is) Natsrath,
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 unto a Virgin espoused to a man whose name was Jauseph, of the house of David, and the name of the Virgin was Mariam.
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 And the angel entered to her, and said to her, Peace to thee, full of grace! our Lord is with thee, thou blessed among women!
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 But she, when she saw, was troubled at his words, and reasoned what this salutation was.
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 And the angel said to her, Fear not, Mariam, for thou hast found favour with Aloha.
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 For, behold, thou shalt conceive, and shalt bring forth a son, and thou shalt call his name Jeshu.
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 He will be great, and the Son of the Most High shall he be called, and Aloha the Lord shall give unto him the throne of David his father.
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 And he shall reign over the house of Jakub for ever, and of his kingdom there shall be no end. (aiōn )
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn )
34 And Mariam said to the angel, How shall this be, because a man is not known to me?
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 The angel answered and said to her, The Spirit of Holiness shall come, and the Power of the Most High shall shadow over thee; on account of this He who (shall be) born from thee is the Holy, and the Son of Aloha shall be called.
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 And behold, Elishaba thy kinswoman, she also beareth a son in her old age, and this is the sixth month to her, -to her who is called the barren.
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 For nothing is difficult to Aloha.
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 And Mariam said, Behold, I am the handmaid of the Lord, be it unto me as thou hast said. And the angel went from her.
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 AND Mariam arose in those days, and went with haste to the mountain to a city of Jehud;
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 and she entered into the house of Zakaria, and saluted Elishaba.
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 And it was that when Elishaba heard the salutation of Mariam, the infant leaped in her womb. And she was filled with the Spirit of Holiness;
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 and she cried with a loud voice, and said unto Mariam, Blessed art thou among women, And blessed is the fruit of thy womb!
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 Whence unto me is this, That the mother of my Lord should come to me?
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 For, lo, as fell the voice of thy salutation on my ears, For great Joy leaped the infant in my womb.
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 And happy is she who hath believed, For there is a fulfilment of those things which have been spoken to her from the Lord.
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 And Mariam said: My soul doth magnify the Lord,
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 And my spirit rejoiceth in Aloha my Saviour,
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 Who hath looked upon the lowliness of his handmaid: For, behold, from now all generations shall give blessedness to me.
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 Because he hath done for me great things, he who is mighty, And holy is his name.
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 And his grace is for ages and generations Upon those who fear him.
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 He hath wrought victory with his arm; He hath scattered the proud in the thoughts of their hearts.
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 He hath overturned the mighty from their thrones, And hath exalted the humble.
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 The hungry he hath satisfied with good things, And the rich he hath sent away empty.
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 He hath helped Isroel his servant, And hath remembered his mercy;
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 As he spake with our fathers, With Abraham and with his seed for ever. (aiōn )
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn )
56 And Mariam stayed with Elishaba three months, and returned to her house.
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 BUT to Elishaba had come the time that she should give birth, and she gave birth to a son.
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 And her neighbours and the sons of her family heard that Aloha had magnified his grace upon her; and they rejoiced with her.
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 And it was the eighth day, and they came to circumcise the child; and they called him by the name of his father, Zakaria.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 And his mother answered and said to them, Not so; but he shall be called Juchanon.
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 And they said to her, No man in thy kindred is called by this name.
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 And they signed to his father (to show) how he willed they should call him.
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 And he requested a tablet, and wrote, and said, Juchanan is his name. And every man wondered.
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 And immediately his mouth and his tongue were opened, and he spake, and blessed Aloha.
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 And there was fear upon all around them; and in all the hill country of Jehud were these things spoken.
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 And all who heard reasoned in their hearts, and said, What is this child to be? And the hand of the Lord was with him.
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 And Zakaria his father was filled with the Spirit of Holiness, and he prophesied, and said:
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 Blessed be the Lord, the Aloha of Israel; For he hath visited his people, and wrought for him redemption,
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 And hath raised up for us the horn of redemption In the house of David his servant;
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 As he spake by the mouth of his holy prophets, Who have been from of old, (aiōn )
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn )
71 That we should be delivered from our adversaries, And from the hand of all who hate us;
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 To perform his grace with our fathers, And to remember his holy covenant;
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 The oath which he sware to Abraham our father, -
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 That to us he would grant That, being delivered from the hand of our adversaries, Without fear we might serve before him
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 All our days in righteousness.
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 And thou, child, the Prophet of the Most High Shalt thou be called; For thou shalt go before the face of the Lord, And thou shalt prepare his way;
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 To give the knowledge of salvation to his people In the forgiveness of their sins,
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 Through the compassions of the grace of our Aloha; Whereby the morn-splendour shall visit us from on high,
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 To illumine those who sit in darkness and the shadow of death. And to direct our feet into the way of peace.
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 And the child grew, and was strong in the spirit, and was in the desert till the day of his manifestation unto Isroel.
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.