< Zephaniah 1 >

1 word LORD which to be to(wards) Zephaniah son: child Cushi son: child Gedaliah son: child Amariah son: child Hezekiah in/on/with day Josiah son: child Amon king Judah
Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
2 to gather to cease all from upon face: surface [the] land: planet utterance LORD
“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
3 to cease man and animal to cease bird [the] heaven and fish [the] sea and [the] ruins with [the] wicked and to cut: eliminate [obj] [the] man from upon face: surface [the] land: planet utterance LORD
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
4 and to stretch hand my upon Judah and upon all to dwell Jerusalem and to cut: cut from [the] place [the] this [obj] remnant [the] Baal [obj] name [the] pagan priest with [the] priest
Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
5 and [obj] [the] to bow upon [the] roof to/for army [the] heaven and [obj] [the] to bow [the] to swear to/for LORD and [the] to swear in/on/with Milcom
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
6 and [obj] [the] to turn from after LORD and which not to seek [obj] LORD and not to seek him
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7 to silence from face: before Lord YHWH/God for near day LORD for to establish: prepare LORD sacrifice to consecrate: consecate to call: call to his
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
8 and to be in/on/with day sacrifice LORD and to reckon: punish upon [the] ruler and upon son: child [the] king and upon all [the] to clothe garment foreign
Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
9 and to reckon: punish upon all [the] to leap upon [the] threshold in/on/with day [the] he/she/it [the] to fill house: home lord their violence and deceit
Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
10 and to be in/on/with day [the] he/she/it utterance LORD voice cry from gate [the] Fish (Gate) and wailing from [the] Second [Quarter] and breaking great: large from [the] hill
“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 to wail to dwell [the] Mortar for to cease all people merchant to cut: eliminate all laden silver: money
Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 and to be in/on/with time [the] he/she/it to search [obj] Jerusalem in/on/with lamp and to reckon: punish upon [the] human [the] to congeal upon dreg their [the] to say in/on/with heart their not be good LORD and not be evil
Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
13 and to be strength: rich their to/for plunder and house: home their to/for devastation and to build house: home and not to dwell and to plant vineyard and not to drink [obj] wine their
Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
14 near day LORD [the] great: large near and quick much voice: sound day LORD bitter to cry there mighty man
Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 day fury [the] day [the] he/she/it day distress and distress day devastation and desolation day darkness and darkness day cloud and cloud
Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 day trumpet and shout upon [the] city [the] to gather/restrain/fortify and upon [the] corner [the] high
Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
17 and to constrain to/for man and to go: walk like/as blind for to/for LORD to sin and to pour: pour blood their like/as dust and intestine their like/as dung
Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 also silver: money their also gold their not be able to/for to rescue them in/on/with day fury LORD and in/on/with fire jealousy his to eat all [the] land: country/planet for consumption surely to dismay to make with all to dwell [the] land: country/planet
Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.

< Zephaniah 1 >