< Zechariah 6 >

1 and to return: again and to lift: look eye my and to see: see and behold four chariot to come out: come from between two [the] mountain: mount and [the] mountain: mount mountain: mount bronze
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
2 in/on/with chariot [the] first horse red and in/on/with chariot [the] second horse black
Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
3 and in/on/with chariot [the] third horse white and in/on/with chariot [the] fourth horse spotted strong
lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
4 and to answer and to say to(wards) [the] messenger: angel [the] to speak: speak in/on/with me what? these lord my
Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
5 and to answer [the] messenger: angel and to say to(wards) me these four spirit: breath [the] heaven to come out: come from to stand upon lord all [the] land: country/planet
Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
6 which in/on/with her [the] horse [the] black to come out: come to(wards) land: country/planet north and [the] white to come out: come to(wards) after them and [the] spotted to come out: come to(wards) land: country/planet [the] south
Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
7 and [the] strong to come out: come and to seek to/for to go: went to/for to go: walk in/on/with land: country/planet and to say to go: went to go: walk in/on/with land: country/planet and to go: walk in/on/with land: country/planet
Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
8 and to cry out with me and to speak: speak to(wards) me to/for to say to see: behold! [the] to come out: come to(wards) land: country/planet north to rest [obj] spirit my in/on/with land: country/planet north
Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
9 and to be word LORD to(wards) me to/for to say
Yehova anayankhula nane kuti,
10 to take: take from with [the] captivity from Heldai and from with Tobijah and from with Jedaiah and to come (in): come you(m. s.) in/on/with day [the] he/she/it and to come (in): come house: home Josiah son: child Zephaniah which to come (in): come from Babylon
“Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
11 and to take: take silver: money and gold and to make crown and to set: make in/on/with head Joshua son: child Jehozadak [the] priest [the] great: large
Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
12 and to say to(wards) him to/for to say thus to say LORD Hosts to/for to say behold man branch name his and from underneath: because of him to spring and to build [obj] temple LORD
Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
13 and he/she/it to build [obj] temple LORD and he/she/it to lift: bear splendor and to dwell and to rule upon throne his and to be priest upon throne his and counsel peace to be between two their
Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
14 and [the] crown to be to/for Helem and to/for Tobijah and to/for Jedaiah and to/for Hen son: child Zephaniah to/for memorial in/on/with temple LORD
Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
15 and distant to come (in): come and to build in/on/with temple LORD and to know for LORD Hosts to send: depart me to(wards) you and to be if to hear: obey to hear: obey [emph?] in/on/with voice LORD God your
Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”

< Zechariah 6 >