< Psalms 83 >
1 song melody to/for Asaph God not quiet to/for you not be quiet and not to quiet God
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 for behold enemy your to roar [emph?] and to hate you to lift: kindness head
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 upon people your be shrewd counsel and to advise upon to treasure your
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 to say to go: come! and to hide them from nation and not to remember name Israel still
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 for to advise heart together upon you covenant to cut: make(covenant)
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 tent Edom and Ishmaelite Moab and Hagri
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebal and Ammon and Amalek Philistia with to dwell Tyre
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 also Assyria to join with them to be arm to/for son: descendant/people Lot (Selah)
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 to make: do to/for them like/as Midian like/as Sisera like/as Jabin in/on/with torrent: river Kishon
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 to destroy in/on/with En-dor En-dor to be dung to/for land: soil
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 to set: make them noble their like/as Oreb and like/as Zeeb and like/as Zebah and like/as Zalmunna all prince their
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 which to say to possess: take to/for us [obj] habitation God
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 God my to set: make them like/as wheel like/as stubble to/for face: before spirit: breath
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 like/as fire to burn: burn wood and like/as flame to kindle mountain: mount
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 so to pursue them in/on/with tempest your and in/on/with whirlwind your to dismay them
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 to fill face their dishonor and to seek name your LORD
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 be ashamed and to dismay perpetuity till and be ashamed and to perish
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 and to know for you(m. s.) name your LORD to/for alone you Most High upon all [the] land: country/planet
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.