< Psalms 68 >
1 to/for to conduct to/for David melody song to arise: rise God to scatter enemy his and to flee to hate him from face: before his
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
2 like/as to drive smoke to drive like/as to melt wax from face: before fire to perish wicked from face: before God
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 and righteous to rejoice to rejoice to/for face: before God and to rejoice in/on/with joy
Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
4 to sing to/for God to sing name his to build to/for to ride in/on/with plain in/on/with LORD name his and to exult to/for face: before his
Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 father orphan and judge widow God in/on/with habitation holiness his
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 God to dwell only house: home [to] to come out: send prisoner in/on/with prosperity surely to rebel to dwell parched
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 God in/on/with to come out: come you to/for face: before people your in/on/with to march you in/on/with wilderness (Selah)
Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 land: country/planet to shake also heaven to drip/prophesy from face: before God this Sinai from face: before God God Israel
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 rain voluntariness to sprinkle God inheritance your and be weary you(m. s.) to establish: make her
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 community your to dwell in/on/with her to establish: prepare in/on/with welfare your to/for afflicted God
Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
11 Lord to give: give word [the] to bear tidings army many
Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
12 king Hosts to wander [emph?] to wander [emph?] and dwelling house: home to divide spoil
“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
13 if to lie down: lay down [emph?] between: among ash heep wing dove to cover in/on/with silver: money and pinion her in/on/with greenish gold
Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
14 in/on/with to spread Almighty king in/on/with her to snow in/on/with (Mount) Zalmon
Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
15 mountain: mount God mountain: mount Bashan mountain: mount peak mountain: mount Bashan
Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
16 to/for what? to watch with envy [emph?] mountain: mount peak [the] mountain: mount to desire God to/for to dwell him also LORD to dwell to/for perpetuity
Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
17 chariot God ten thousand thousand thousands Lord in/on/with them Sinai in/on/with holiness
Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
18 to ascend: rise to/for height to take captive captivity to take: recieve gift in/on/with man and also to rebel to/for to dwell LORD God
Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
19 to bless Lord day: daily day: daily to lift to/for us [the] God salvation our (Selah)
Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 [the] God to/for us God to/for salvation and to/for YHWH/God Lord to/for death outgoing
Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
21 surely God to wound head enemy his crown hair to go: walk in/on/with guilt (offering) his
Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
22 to say Lord from Bashan to return: return to return: return from depth sea
Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
23 because to wound foot your in/on/with blood tongue dog your from enemy portion his
Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
24 to see: see walk your God walk God my king my in/on/with holiness
Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
25 to meet to sing (after *L(S)*) to play in/on/with midst maiden to beat
Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
26 in/on/with assembly to bless God LORD from fountain Israel
Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
27 there Benjamin little to rule them ruler Judah crowd their ruler Zebulun ruler Naphtali
Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
28 to command God your strength your be strong [emph?] God this to work to/for us
Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
29 from temple your upon Jerusalem to/for you to conduct king gift
Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
30 to rebuke living thing branch: stem congregation mighty: ox in/on/with calf people to stamp in/on/with piece silver: money to scatter people battle to delight in
Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
31 to come ambassador from Egypt Cush to run: run hand his to/for God
Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
32 kingdom [the] land: country/planet to sing to/for God to sing Lord (Selah)
Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
33 to/for to ride in/on/with heaven heaven front: old look! to give: cry out in/on/with voice his voice strength
Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
34 to give: give strength to/for God upon Israel pride his and strength his in/on/with cloud
Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
35 to fear: revere God from sanctuary your God Israel he/she/it to give: give strength and power to/for people to bless God
Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!