< Psalms 60 >
1 to/for to conduct upon lily testimony Miktam to/for David to/for to learn: teach in/on/with to struggle he [obj] Aram-naharaim Aram-naharaim and [obj] Aram-zobah Aram-zobah and to return: return Joab and to smite [obj] Edom in/on/with (Salt) Valley (Valley of) Salt two ten thousand God to reject us to break through us be angry to return: rescue to/for us
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 to shake land: country/planet to split open her to heal [emph?] breaking her for to shake
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 to see: see people your severe to water: drink us wine reeling
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 to give: put to/for afraid your ensign to/for to shine from face: because bow (Selah)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 because to rescue [emph?] beloved your to save [emph?] right your (and to answer me *Q(K)*)
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 God to speak: speak in/on/with holiness his to exult to divide Shechem and valley Succoth to measure
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 to/for me Gilead and to/for me Manasseh and Ephraim security head: leader my Judah to decree me
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab pot washing my upon Edom to throw sandal my upon me Philistia to shout
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 who? to conduct me city siege who? to lead me till Edom
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 not you(m. s.) God to reject us and not to come out: come God in/on/with army our
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 to give [emph?] to/for us help from enemy and vanity: vain deliverance: salvation man
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 in/on/with God to make: do strength and he/she/it to trample enemy our
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.