< Psalms 4 >
1 to/for to conduct in/on/with music melody to/for David in/on/with to call: call to I to answer me God righteousness my in/on/with distress to enlarge to/for me be gracious me and to hear: hear prayer my
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
2 son: descendant/people man till what? glory my to/for shame to love: lover [emph?] vain to seek lie (Selah)
Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
3 and to know for be distinguished LORD pious to/for him LORD to hear: hear in/on/with to call: call to I to(wards) him
Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
4 to tremble and not to sin to say in/on/with heart your upon bed your and to silence: silent (Selah)
Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
5 to sacrifice sacrifice righteousness and to trust to(wards) LORD
Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
6 many to say who? to see: see us good to lift: kindness [emph?] upon us light face your LORD
Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
7 to give: put joy in/on/with heart my from time grain their and new wine their to multiply
Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
8 in/on/with peace together to lie down: lay down and to sleep for you(m. s.) LORD to/for isolation to/for security to dwell me
Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.