< Psalms 3 >

1 melody to/for David in/on/with to flee he from face: before Absalom son: child his LORD what? to multiply enemy my many to arise: attack upon me
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 many to say to/for soul my nothing salvation to/for him in/on/with God (Selah)
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 and you(m. s.) LORD shield about/through/for me glory my and to exalt head my
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 voice my to(wards) LORD to call: call out and to answer me from mountain: mount holiness his (Selah)
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 I to lie down: lay down and to sleep [emph?] to awake for LORD to support me
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 not to fear from myriad people which around to set: make upon me
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 to arise: rise [emph?] LORD to save me God my for to smite [obj] all enemy my jaw tooth wicked to break
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 to/for LORD [the] salvation upon people your blessing your (Selah)
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)

< Psalms 3 >