< Psalms 27 >
1 to/for David LORD light my and salvation my from who? to fear: revere LORD security life my from who? to dread
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 in/on/with to present: come upon me be evil to/for to eat [obj] flesh my enemy my and enemy my to/for me they(masc.) to stumble and to fall: fall
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 if to camp upon me camp not to fear heart my if to arise: rise upon me battle in/on/with this I to trust
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 one to ask from with LORD [obj] her to seek to dwell I in/on/with house: temple LORD all day life my to/for to see in/on/with pleasantness LORD and to/for to enquire in/on/with temple his
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 for to treasure me in/on/with lair his in/on/with day distress: harm to hide me in/on/with secrecy tent his in/on/with rock to exalt me
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 and now to exalt head my upon enemy my around me and to sacrifice in/on/with tent his sacrifice shout to sing and to sing to/for LORD
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 to hear: hear LORD voice my to call: call to and be gracious me and to answer me
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 to/for you to say heart my to seek face my [obj] face your LORD to seek
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 not to hide face your from me not to stretch in/on/with face: anger servant/slave your help my to be not to leave me and not to leave: forsake me God salvation my
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 for father my and mother my to leave: forsake me and LORD to gather me
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 to show me LORD way: conduct your and to lead me in/on/with way plain because enemy my
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 not to give: give me in/on/with soul: appetite enemy my for to arise: attack in/on/with me witness deception and breathing violence
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 unless be faithful to/for to see: see in/on/with goodness LORD in/on/with land: country/planet alive
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 to await to(wards) LORD to strengthen: strengthen and to strengthen heart your and to await to(wards) LORD
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.