< Psalms 143 >

1 melody to/for David LORD to hear: hear prayer my to listen [emph?] to(wards) supplication my in/on/with faithfulness your to answer me in/on/with righteousness your
Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
2 and not to come (in): come in/on/with justice: judgement with servant/slave your for not to justify to/for face: before your all alive
Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
3 for to pursue enemy soul my to crush to/for land: soil living thing my to dwell me in/on/with darkness like/as to die forever: antiquity
Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
4 and to enfeeble upon me spirit my in/on/with midst me be desolate: appalled heart my
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
5 to remember day from front: old to mutter in/on/with all work your in/on/with deed: work hand your to muse
Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
6 to spread hand my to(wards) you soul my like/as land: country/planet faint to/for you (Selah)
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
7 to hasten to answer me LORD to end: finish spirit my not to hide face your from me and to liken with to go down pit
Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
8 to hear: hear me in/on/with morning kindness your for in/on/with you to trust to know me way: conduct this to go: went for to(wards) you to lift: kindness soul my
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
9 to rescue me from enemy my LORD to(wards) you to cover
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 to learn: teach me to/for to make: do acceptance your for you(m. s.) God my spirit your pleasant to lead me in/on/with land: soil plain
Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
11 because name your LORD to live me in/on/with righteousness your to come out: send from distress soul my
Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 and in/on/with kindness your to destroy enemy my and to perish all to vex soul my for I servant/slave your
Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.

< Psalms 143 >