< Psalms 115 >
1 not to/for us LORD not to/for us for to/for name your to give: give glory upon kindness your upon truth: faithful your
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 to/for what? to say [the] nation where? please God their
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 and God our in/on/with heaven all which to delight in to make: do
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 idol their silver: money and gold deed: work hand man
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 lip to/for them and not to speak: speak eye to/for them and not to see: see
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 ear to/for them and not to hear: hear face: nose to/for them and not to smell [emph?]
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 hand their and not to feel [emph?] foot their and not to go: walk not to mutter in/on/with throat their
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 like them to be to make them all which to trust in/on/with them
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Israel to trust in/on/with LORD helper their and shield their he/she/it
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 house: household Aaron to trust in/on/with LORD helper their and shield their he/she/it
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 afraid LORD to trust in/on/with LORD helper their and shield their he/she/it
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 LORD to remember us to bless to bless [obj] house: household Israel to bless [obj] house: household Aaron
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 to bless afraid LORD [the] small with [the] great: large
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 to add LORD upon you upon you and upon son: child your
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 to bless you(m. p.) to/for LORD to make heaven and land: country/planet
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 [the] heaven heaven to/for LORD and [the] land: country/planet to give: give to/for son: child man
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 not [the] to die to boast: praise LORD and not all to go down silence
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 and we to bless LORD from now and till forever: enduring to boast: praise LORD
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.