< Psalms 113 >

1 to boast: praise LORD to boast: praise servant/slave LORD to boast: praise [obj] name LORD
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 to be name LORD to bless from now and till forever: enduring
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 from east sun till entrance his to boast: praise name LORD
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 to exalt upon all nation LORD upon [the] heaven glory his
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 who? like/as LORD God our [the] to exult to/for to dwell
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 [the] to abase to/for to see: see in/on/with heaven and in/on/with land: country/planet
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 to arise: raise from dust poor from refuse to exalt needy
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 to/for to dwell with noble with noble people his
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 to dwell barren [the] house: home mother [the] son: child glad to boast: praise LORD
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Psalms 113 >