< Proverbs 6 >

1 son: child my if to pledge to/for neighbor your to blow to/for be a stranger palm your
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 to snare in/on/with word lip your to capture in/on/with word lip your
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 to make: do this then son: child my and to rescue for to come (in): come in/on/with palm neighbor your to go: went to stamp and to be assertive neighbor your
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 not to give: give sleep to/for eye your and slumber to/for eyelid your
Usagone tulo, usawodzere.
5 to rescue like/as gazelle from hand and like/as bird from hand fowler
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 to go: went to(wards) ant sluggish to see: examine way: conduct her and be wise
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 which nothing to/for her chief official and to rule
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 to establish: prepare in/on/with summer food: bread her to gather in/on/with harvest food her
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 till how sluggish to lie down: lay down how to arise: rise from sleep your
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 little sleep little slumber little folding hand to/for to lie down: sleep
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 and to come (in): come like/as to go: follow poverty your and need your like/as man shield
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 man Belial: worthless man evil: wickedness to go: walk crookedness lip: word
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 to wink (in/on/with eye his *Q(K)*) to rub (in/on/with foot his *Q(K)*) to show in/on/with finger his
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 perversity in/on/with heart his to plow/plot bad: evil in/on/with all time (contention *Q(K)*) to send: depart
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 upon so suddenly to come (in): come calamity his suddenness to break and nothing healing
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 six they(fem.) to hate LORD and seven (abomination *Q(K)*) soul: myself his
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 eye to exalt tongue deception and hand to pour: kill blood innocent
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 heart to plow/plot plot evil: wickedness foot to hasten to/for to run: run to/for distress: evil
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 to breathe lie witness deception and to send: depart strife between brother: male-sibling
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 to watch son: child my commandment father your and not to leave instruction mother your
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 to conspire them upon heart your continually to bind them upon neck your
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 in/on/with to go: walk you to lead [obj] you in/on/with to lie down: lay down you to keep: guard upon you and to awake he/she/it to muse you
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 for lamp commandment and instruction light and way: conduct life argument discipline
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 to/for to keep: guard you from woman bad: evil from smoothness tongue foreign
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 not to desire beauty her in/on/with heart your and not to take: take you in/on/with eyelid her
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 for about/through/for woman to fornicate till talent food: bread and woman man: husband soul: life precious to hunt
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 to snatch up man fire in/on/with bosom: lap his and garment his not to burn
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 if to go: walk man upon [the] coal and foot his not to burn
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 so [the] to come (in): come to(wards) woman: wife neighbor his not to clear all [the] to touch in/on/with her
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 not to despise to/for thief for to steal to/for to fill soul: appetite his for be hungry
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 and to find to complete sevenfold [obj] all substance house: home his to give: give
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 to commit adultery woman lacking heart to ruin soul: myself his he/she/it to make: do her
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 plague and dishonor to find and reproach his not to wipe
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 for jealousy rage great man and not to spare in/on/with day vengeance
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 not to lift: kindness face: kindness all ransom and not be willing for to multiply bribe
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.

< Proverbs 6 >