< Nehemiah 11 >
1 and to dwell ruler [the] people in/on/with Jerusalem and remnant [the] people to fall: allot allotted to/for to come (in): bring one from [the] ten to/for to dwell in/on/with Jerusalem city [the] holiness and nine [the] hand: times in/on/with city
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 and to bless [the] people to/for all [the] human [the] be willing to/for to dwell in/on/with Jerusalem
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 and these head: leader [the] province which to dwell in/on/with Jerusalem and in/on/with city Judah to dwell man: anyone in/on/with possession his in/on/with city their Israel [the] priest and [the] Levi and [the] temple servant and son: descendant/people servant/slave Solomon
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 and in/on/with Jerusalem to dwell from son: descendant/people Judah and from son: descendant/people Benjamin from son: descendant/people Judah Athaiah son: child Uzziah son: child Zechariah son: child Amariah son: child Shephatiah son: child Mahalalel from son: descendant/people Perez
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 and Maaseiah son: child Baruch son: child Col-hozeh Col-hozeh son: child Hazaiah son: child Adaiah son: child Joiarib son: child Zechariah son: child [the] Shilonite
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 all son: descendant/people Perez [the] to dwell in/on/with Jerusalem four hundred sixty and eight human strength
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 and these son: descendant/people Benjamin Sallu son: child Meshullam son: child Joed son: child Pedaiah son: child Kolaiah son: child Maaseiah son: child Ithiel son: child Jeshaiah
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 and after him `men` `valor` nine hundred twenty and eight
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 and Joel son: child Zichri overseer upon them and Judah son: child [the] Hassenuah upon [the] city second
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 from [the] priest Jedaiah son: child Joiarib Jachin
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 Seraiah son: child Hilkiah son: child Meshullam son: child Zadok son: child Meraioth son: child Ahitub leader house: temple [the] God
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 and brother: male-relative their to make: do [the] work to/for house: temple eight hundred twenty and two and Adaiah son: child Jeroham son: child Pelaliah son: child Amzi son: child Zechariah son: child Pashhur son: child Malchijah
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 and brother: male-relative his head: leader to/for father hundred forty and two and Amashsai son: child Azarel son: child Ahzai son: child Meshillemoth son: child Immer
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 and brother: male-relative their mighty man strength hundred twenty and eight and overseer upon them Zabdiel son: child (Haggedolim *L(F)*)
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 and from [the] Levi Shemaiah son: child Hasshub son: child Azrikam son: child Hashabiah son: child Bunni
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 and Shabbethai and Jozabad upon [the] work [the] outer to/for house: temple [the] God from head: leader [the] Levi
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 and Mattaniah son: child Mica son: child Zabdi son: child Asaph head: leader [the] beginning to give thanks to/for prayer and Bakbukiah second from brother: male-relative his and Abda son: child Shammua son: child Galal son: child (Jeduthun *Q(K)*)
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 all [the] Levi in/on/with city [the] holiness hundred eighty and four
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 and [the] gatekeeper Akkub Talmon and brother: male-relative their [the] to keep: guard in/on/with gate hundred seventy and two
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 and remnant Israel [the] priest [the] Levi in/on/with all city Judah man: anyone in/on/with inheritance his
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 and [the] temple servant to dwell in/on/with Ophel and Ziha and Gishpa upon [the] temple servant
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 and overseer [the] Levi in/on/with Jerusalem Uzzi son: child Bani son: child Hashabiah son: child Mattaniah son: child Mica from son: descendant/people Asaph [the] to sing to/for before work house: temple [the] God
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 for commandment [the] king upon them and sure upon [the] to sing word: portion day in/on/with day: daily his
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 and Pethahiah son: child Meshezabel from son: descendant/people Zerah son: child Judah to/for hand: to [the] king to/for all word: thing to/for people
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 and to(wards) [the] village in/on/with land: country their from son: descendant/people Judah to dwell in/on/with Kiriath-arba [the] Kiriath-arba and daughter: village her and in/on/with Dibon and daughter: village her and in/on/with Jekabzeel and village her
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 and in/on/with Jeshua and in/on/with Moladah and in/on/with Beth-pelet Beth-pelet
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 and in/on/with Hazar-shual Hazar-shual and in/on/with Beersheba Beersheba and daughter: village her
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 and in/on/with Ziklag and in/on/with Meconah and in/on/with daughter: village her
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 and in/on/with En-rimmon En-rimmon and in/on/with Zorah and in/on/with Jarmuth
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 Zanoah Adullam and village their Lachish and land: country her Azekah and daughter: village her and to camp from Beersheba Beersheba till Valley (Topheth of) Hinnom
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 and son: descendant/people Benjamin from Geba Michmash and Ai and Bethel Bethel and daughter: village her
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 Lod and Ono valley [the] artificer
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 and from [the] Levi division Judah to/for Benjamin
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.