< Malachi 3 >

1 look! I to send: depart messenger my and to turn way: road to/for face: before my and suddenly to come (in): come to(wards) temple his [the] lord which you(m. p.) to seek and messenger [the] covenant which you(m. p.) delighting behold to come (in): come to say LORD Hosts
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
2 and who? to sustain [obj] day to come (in): come he and who? [the] to stand: stand in/on/with to see: see he for he/she/it like/as fire to refine and like/as lye to wash
Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
3 and to dwell to refine and be pure silver: money and be pure [obj] son: descendant/people Levi and to refine [obj] them like/as gold and like/as silver: money and to be to/for LORD to approach: bring offering in/on/with righteousness
Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
4 and to please to/for LORD offering Judah and Jerusalem like/as day forever: antiquity and like/as year eastern: older
ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
5 and to present: come to(wards) you to/for justice: judgement and to be witness to hasten in/on/with to practice sorcery and in/on/with to commit adultery and in/on/with to swear to/for deception and in/on/with to oppress wages hired widow and orphan and to stretch sojourner and not to fear: revere me to say LORD Hosts
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
6 for I LORD not to change and you(m. p.) son: descendant/people Jacob not to end: destroy
“Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
7 to/for from day father your to turn aside: turn aside from statute: decree my and not to keep: obey to return: return to(wards) me and to return: return to(wards) you to say LORD Hosts and to say in/on/with what? to return: return
Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
8 to rob man God for you(m. p.) to rob [obj] me and to say in/on/with what? to rob you [the] tithe and [the] contribution
“Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
9 in/on/with curse you(m. p.) to curse and [obj] me you(m. p.) to rob [the] nation all his
Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
10 to come (in): bring [obj] all [the] tithe to(wards) house: home [the] treasure and to be prey in/on/with house: home my and to test me please in/on/with this to say LORD Hosts if not to open to/for you [obj] window [the] heaven and to empty to/for you blessing till without sufficiency
Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
11 and to rebuke to/for you in/on/with to eat and not to ruin to/for you [obj] fruit [the] land: soil and not be bereaved to/for you [the] vine in/on/with land: country to say LORD Hosts
Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 and to bless [obj] you all [the] nation for to be you(m. p.) land: country/planet pleasure to say LORD Hosts
“Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
13 to strengthen: strengthen upon me word your to say LORD and to say what? to speak: speak upon you
Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
14 to say vanity: vain to serve: minister God and what? unjust-gain for to keep: obey charge his and for to go: walk mournfully from face: before LORD Hosts
“Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
15 and now we to bless arrogant also to build to make: [do] wickedness also to test God and to escape
Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
16 then to speak: speak afraid LORD man: anyone with neighbor his and to listen LORD and to hear: hear and to write scroll: book memorial to/for face: before his to/for afraid LORD and to/for to devise: count name his
Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
17 and to be to/for me to say LORD Hosts to/for day which I to make possession and to spare upon them like/as as which to spare man: anyone upon son: child his [the] to serve [obj] him
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
18 and to return: again and to see: see between righteous to/for wicked between to serve: minister God to/for which not to serve: minister him
Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”

< Malachi 3 >