< Judges 7 >
1 and to rise Jerubbaal he/she/it Gideon and all [the] people: soldiers which with him and to camp upon Harod Harod and camp Midian to be to/for him from north from hill [the] Moreh in/on/with valley
Yeru-Baala (Gideoni) ndi anthu ake onse anadzuka mʼmamawa nakamanga misasa pambali pa kasupe ku Harodi. Misasa ya Amidiyani inali mʼchigwa kumpoto kwa phiri la More.
2 and to say LORD to(wards) Gideon many [the] people: soldiers which with you from to give: give I [obj] Midian in/on/with hand: power their lest to beautify upon me Israel to/for to say hand: power my to save to/for me
Yehova anati kwa Gideoni, “Anthu uli nawowa andichulukira kwambiri kuti ndigonjetse Amidiyani chifukwa Aisraeli angamadzitukumule pamaso panga ndi kumanena kuti, ‘Tadzipulumutsa ndi mphamvu zathu.’
3 and now to call: call out please in/on/with ear: to ears [the] people: soldiers to/for to say who? afraid and trembling to return: return and to depart from mountain: mount [the] (Mount) Gilead and to return: return from [the] people: soldiers twenty and two thousand and ten thousand to remain
Tsono lengeza kwa anthu kuti, ‘Aliyense amene akuchita mantha ndi kunjenjemera abwerere kwawo, ndipo achoke kuno ku phiri la Giliyadi.’” Choncho anthu 22,000 anachoka, ndipo anatsalira anthu 10,000.
4 and to say LORD to(wards) Gideon still [the] people: soldiers many to go down [obj] them to(wards) [the] water and to refine him to/for you there and to be which to say to(wards) you this to go: went with you he/she/it to go: went with you and all which to say to(wards) you this not to go: went with you he/she/it not to go: went
Koma Yehova anawuza Gideoni kuti, “Anthuwa achulukabe. Uwatenge upite nawo ku mtsinje ndipo ndikawayesa kumeneko mʼmalo mwako. Ndikadzanena kuti, ‘Uyu apite nawe’ adzapita nawe; koma ndikanena kuti ‘Uyu asapite nawe,’ sadzapita nawe.”
5 and to go down [obj] [the] people: soldiers to(wards) [the] water and to say LORD to(wards) Gideon all which to lick in/on/with tongue his from [the] water like/as as which to lick [the] dog to set [obj] him to/for alone and all which to bow upon knee his to/for to drink
Choncho Gideoni anatenga anthuwo ndi kupita nawo ku madzi. Kumeneko Yehova anamuwuza kuti, “Amene amwe madzi mokhathira ndi manja ngati galu uwayike pawokha, ndipo amene amwe atagwada pansi uwayikenso pawokha.”
6 and to be number [the] to lick in/on/with hand their to(wards) lip their three hundred man and all remainder [the] people: soldiers to bow upon knee their to/for to drink water
Ndipo anthu 300 anamwa mokhathira, pamene ena onse anagwada pansi pakumwa.
7 and to say LORD to(wards) Gideon in/on/with three hundred [the] man [the] to lick to save [obj] you and to give: give [obj] Midian in/on/with hand: power your and all [the] people: soldiers to go: went man: anyone to/for place his
Yehova anati kwa Gideoni, “Ndi anthu 300 amene anamwa madzi mokhathira ndi manja awo ndidzakupulumutsani ndipo ndidzapereka Amidiyani mʼmanja mwanu. Koma anthu ena onse apite ku nyumba kwawo.”
8 and to take: take [obj] provision [the] people: soldiers in/on/with hand their and [obj] trumpet their and [obj] all man Israel to send: depart man: anyone to/for tent his and in/on/with three hundred [the] man to strengthen: hold and camp Midian to be to/for him from underneath: under in/on/with valley
Choncho analola anthu ena onse kuti apite ku nyumba zawo kupatula anthu 300 osankhika aja. Iwowa anatenga zakudya ndi malipenga a anthuwo. Ndipo misasa ya ankhondo Amidiyani inali kumunsi kwa chigwa.
9 and to be in/on/with night [the] he/she/it and to say to(wards) him LORD to arise: rise to go down in/on/with camp for to give: give him in/on/with hand: power your
Usiku umenewo Yehova anati kwa Gideoni, “Dzuka, pita kachite nkhondo ku misasayo, chifukwa ndayipereka mʼmanja mwako.
10 and if afraid you(m. s.) to/for to go down to go down you(m. s.) and Purah youth your to(wards) [the] camp
Ngati ukuopa, upite ku msasako ndi Pura wantchito wako,
11 and to hear: hear what? to speak: speak and after to strengthen: strengthen hand your and to go down in/on/with camp and to go down he/she/it and Purah youth his to(wards) end [the] armed which in/on/with camp
ndipo ukamvere zimene akunena ndipo pambuyo pake udzalimba mtima ndi kupita kukayithira nkhondo misasayo.” Choncho iye ndi wantchito wake Pura anapita kumbali ina ya msasawo kumene kunali ankhondo.
12 and Midian and Amalek and all son: descendant/people East to fall: fall in/on/with valley like/as locust to/for abundance and to/for camel their nothing number like/as sand which/that upon lip: shore [the] sea to/for abundance
Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena onse akummawa anadzaza chigwa chonse ngati dzombe. Ngamira zawo zinali zambiri zosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
13 and to come (in): come Gideon and behold man to recount to/for neighbor his dream and to say behold dream to dream and behold (bun *Q(K)*) food: bread barley to overturn in/on/with camp Midian and to come (in): come till [the] tent and to smite him and to fall: fall and to overturn him to/for above [to] and to fall: fall [the] tent
Gideoni atafika anangomva munthu wina akuwuza mnzake maloto ake kuti, “Ine ndinalota nditaona dengu la buledi wa barele likugubuduzika kupita ku misasa ya Amidiyani. Litafika linawomba tenti moti inagwa ndi kuphwasukaphwasuka.”
14 and to answer neighbor his and to say nothing this lest if: surely yes sword Gideon son: child Joash man Israel to give: give [the] God in/on/with hand: power his [obj] Midian and [obj] all [the] camp
Ndipo mnzakeyo anamuyankha kuti, “Iyi ndi nkhondo ya Gideoni mwana wa Yowasi, wa ku Israeli. Mulungu wapereka Amidiyani pamodzi ndi ankhondo ake onse mʼdzanja mwake.”
15 and to be like/as to hear: hear Gideon [obj] number [the] dream and [obj] breaking his and to bow and to return: return to(wards) camp Israel and to say to arise: rise for to give: give LORD in/on/with hand: power your [obj] camp Midian
Gideoni atamva za malotowo ndi kumasulira kwake, anapembedza Mulungu. Kenaka anabwerera ku msasa wa Israeli nawawuza kuti, “Dzukani popeza Yehova wapereka msasa wa Midiyani mʼmanja mwanu.”
16 and to divide [obj] three hundred [the] man three head: group and to give: put trumpet in/on/with hand all their and jar worthless and torch in/on/with midst [the] jar
Anawagawa anthu 300 aja magulu atatu, nawapatsa malipenga mʼmanja mwawo ndi mbiya zimene mʼkati mwake munali nsakali zoyaka.
17 and to say to(wards) them from me to see: see and so to make: do and behold I to come (in): come in/on/with end [the] camp and to be like/as as which to make: do so to make: do [emph?]
Anawuza anthuwo kuti, “Muzikayangʼana ine ndi kuchita zimene ndizikachita. Ndikakafika kumalire a msasa, mukachite zomwe ndikachita ine.
18 and to blow in/on/with trumpet I and all which with me and to blow in/on/with trumpet also you(m. p.) around: side all [the] camp and to say to/for LORD and to/for Gideon
Ndikadzaliza lipenga ndi onse amene ali ndi ine, inunso mukalize malipenga kumbali zonse za misasa yonse ndi kufuwula kuti, ‘Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.’”
19 and to come (in): come Gideon and hundred man which with him in/on/with end [the] camp head: first [the] watch [the] middle surely to arise: guard to arise: guard [obj] [the] to keep: guard and to blow in/on/with trumpet and to shatter [the] jar which in/on/with hand their
Choncho Gideoni pamodzi ndi amuna 100 omwe anali nawo anafika ku malire a msasa pakati pa usiku, alonda atangosinthana kumene. Iwo analiza malipenga awo ndi kuphwanya mbiya zimene zinali mʼmanja mwawo.
20 and to blow three [the] head: group in/on/with trumpet and to break [the] jar and to strengthen: hold in/on/with hand left their in/on/with torch and in/on/with hand right their [the] trumpet to/for to blow and to call: call out sword to/for LORD and to/for Gideon
Magulu awiri ena aja anayimbanso malipenga ndi kuswa mbiya zawo. Aliyense ananyamula nsakali ya moto ku dzanja lamanzere ndi lipenga ku dzanja lamanja ndipo anafuwula kuti, “Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.”
21 and to stand: stand man: anyone underneath: stand him around to/for camp and to run: run all [the] camp and to shout (and to flee *Q(K)*)
Aliyense anayima pa malo pake kuzungulira misasa. Ankhondo a mʼmisasa muja anadzuka nayamba kuthawa akufuwula.
22 and to blow three hundred [the] trumpet and to set: make LORD [obj] sword man: anyone in/on/with neighbor his and in/on/with all [the] camp and to flee [the] camp till Beth-shittah [the] Beth-shittah Zererah till lip: edge Abel-meholah Abel-meholah upon Tabbath
Anthu 300 aja ataliza malipenga, Yehova anawasokoneza ankhondo a Midiyani aja motero kuti ankamenyana okhaokha. Ankhondowo anathawira ku Beti-Sita cha ku Zerera mpaka ku malire a Abeli-Mehola pafupi ndi Tabati.
23 and to cry man Israel from Naphtali and from Asher and from all Manasseh and to pursue after Midian
Aisraeli a fuko la Nafutali, fuko la Aseri, ndi fuko lonse la Manase anayitanidwa, ndipo iwo anathamangitsa Amidiyaniwo.
24 and messenger to send: depart Gideon in/on/with all mountain: hill country Ephraim to/for to say to go down to/for to encounter: toward Midian and to capture to/for them [obj] [the] water till Beth-barah Beth-barah and [obj] [the] Jordan and to cry all man Ephraim and to capture [obj] [the] water till Beth-barah Beth-barah and [obj] [the] Jordan
Gideoni anatumiza amithenga ku dziko lonse la ku mapiri la Efereimu kukanena kuti, “Tsikani mumenyane ndi Amidiyani ndipo mulande madooko awo owolokera mpaka ku Beti-Bara.” Choncho anthu onse a fuko la Efereimu anasonkhana ndipo analanda madooko awo owolokera mpaka ku Betibaala.
25 and to capture two ruler Midian [obj] Oreb and [obj] Zeeb and to kill [obj] Oreb in/on/with rock Oreb and [obj] Zeeb to kill in/on/with wine Zeeb and to pursue to(wards) Midian and head Oreb and Zeeb to come (in): bring to(wards) Gideon from side: beyond to/for Jordan
Iwo anagwiranso atsogoleri awiri a nkhondo a Amidiyani, Orebu ndi Zeebu. Anapha Orebu ku thanthwe la Orebu, koma Zeebu anamuphera ku malo ofinyira mphesa ku Zeebu pothamangitsa Amidiyani. Mitu ya Orebu ndi Zeebu anabwera nayo kwa Gideoni kutsidya kwa Yorodani.