< Joshua 13 >

1 and Joshua be old to come (in): advanced in/on/with day: year and to say LORD to(wards) him you(m. s.) be old to come (in): advanced in/on/with day: year and [the] land: country/planet to remain to multiply much to/for to possess: take her
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 this [the] land: country/planet [the] to remain all border [the] Philistine and all [the] Geshurite
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 from [the] Shihor which upon face: surface Egypt and till border: boundary Ekron north [to] to/for Canaanite to devise: count five lord Philistine [the] Gaza and [the] Ashdod [the] Ashkelonite [the] Gittite and [the] Ekron and [the] Avvim
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 from south all land: country/planet [the] Canaanite and Mearah which to/for Sidonian till Aphek [to] till border: boundary [the] Amorite
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 and [the] land: country/planet [the] Gebalite and all [the] Lebanon east [the] sun from Baal-gad Baal-gad underneath: under mountain: mount (Mount) Hermon till Lebo-(Hamath) Hamath
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 all to dwell [the] mountain: hill country from [the] Lebanon till Misrephoth-maim Misrephoth-maim all Sidonian I to possess: take them from face: before son: descendant/people Israel except to fall: allot her to/for Israel in/on/with inheritance like/as as which to command you
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 and now to divide [obj] [the] land: country/planet [the] this in/on/with inheritance to/for nine [the] tribe and half [the] tribe [the] Manasseh
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 with him [the] Reubenite and [the] Gad to take: recieve inheritance their which to give: give to/for them Moses in/on/with side: beyond [the] Jordan east [to] like/as as which to give: give to/for them Moses servant/slave LORD
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 from Aroer which upon lip: edge torrent: valley Arnon and [the] city which in/on/with midst [the] torrent: valley and all [the] plain Medeba till Dibon
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 and all city Sihon king [the] Amorite which to reign in/on/with Heshbon till border: boundary son: descendant/people Ammon
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 and [the] Gilead and border: area [the] Geshurite and [the] Maacathite and all mountain: mount (Mount) Hermon and all [the] Bashan till Salecah
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 all kingdom Og in/on/with Bashan which to reign in/on/with Ashtaroth and in/on/with Edrei he/she/it to remain from remainder [the] Rephaim and to smite them Moses and to possess: take them
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 and not to possess: take son: descendant/people Israel [obj] [the] Geshurite and [obj] [the] Maacathite and to dwell Geshur and Maacah in/on/with entrails: among Israel till [the] day: today [the] this
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 except to/for tribe [the] Levi not to give: give inheritance food offering LORD God Israel he/she/it inheritance his like/as as which to speak: speak to/for him
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 and to give: give Moses to/for tribe son: descendant/people Reuben to/for family their
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 and to be to/for them [the] border: area from Aroer which upon lip: edge torrent: valley Arnon and [the] city which in/on/with midst [the] torrent: valley and all [the] plain upon Medeba
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 Heshbon and all city her which in/on/with plain Dibon and Bamoth (Bamoth)-baal and Beth-(baal-meon) Baal-meon Baal-meon
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 and Jahaz [to] and Kedemoth and Mephaath
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 and Kiriathaim and Sibmah and Zereth-shahar [the] Zereth-shahar in/on/with mountain: mount [the] valley
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 and Beth-peor Beth-peor and Slopes (of Pisgah) [the] Pisgah and Beth-jeshimoth [the] Beth-jeshimoth
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 and all city [the] plain and all kingdom Sihon king [the] Amorite which to reign in/on/with Heshbon which to smite Moses [obj] him and [obj] leader Midian [obj] Evi and [obj] Rekem and [obj] Zur and [obj] Hur and [obj] Reba prince Sihon to dwell [the] land: country/planet
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 and [obj] Balaam son: child Beor [the] to divine to kill son: descendant/people Israel in/on/with sword to(wards) slain: killed their
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 and to be border: boundary son: descendant/people Reuben [the] Jordan and border: boundary this inheritance son: descendant/people Reuben to/for family their [the] city and village their
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 and to give: give Moses to/for tribe Gad to/for son: descendant/people Gad to/for family their
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 and to be to/for them [the] border: area Jazer and all city [the] Gilead and half land: country/planet son: descendant/people Ammon till Aroer which upon face: surface Rabbah
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 and from Heshbon till Ramath-mizpeh [the] Ramath-mizpeh and Betonim and from Mahanaim till border: area Debir
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 and in/on/with valley Beth-haram Beth-haram and Beth-nimrah Beth-nimrah and Succoth and Zaphon remainder kingdom Sihon king Heshbon [the] Jordan and border: boundary till end sea (Sea of) Chinnereth side: beyond [the] Jordan east [to]
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 this inheritance son: descendant/people Gad to/for family their [the] city and village their
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 and to give: give Moses to/for half tribe Manasseh and to be to/for half tribe son: descendant/people Manasseh to/for family their
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 and to be border: area their from Mahanaim all [the] Bashan all kingdom Og king [the] Bashan and all village Jair which in/on/with Bashan sixty city
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 and half [the] Gilead and Ashtaroth and Edrei city kingdom Og in/on/with Bashan to/for son: descendant/people Machir son: child Manasseh to/for half son: descendant/people Machir to/for family their
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 these which to inherit Moses in/on/with Plains (of Moab) (Plains of) Moab from side: beyond to/for Jordan Jericho east [to]
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 and to/for tribe [the] Levi not to give: give Moses inheritance LORD God Israel he/she/it inheritance their like/as as which to speak: speak to/for them
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Joshua 13 >