< Jonah 4 >

1 and be evil to(wards) Jonah distress: evil great: large and to be incensed to/for him
Koma Yona anakhumudwa kwambiri ndipo anakwiya.
2 and to pray to(wards) LORD and to say Please! LORD not this word: speaking my till to be I upon land: country my upon so to meet to/for to flee Tarshish [to] for to know for you(m. s.) God gracious and compassionate slow face: anger and many kindness and to be sorry: relent upon [the] distress: harm
Iye anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, kodi izi si zimene ndinanena ndikanali kwathu? Nʼchifukwa chaketu ine ndinafulumira kuthawa kupita ku Tarisisi. Ine ndinadziwa kuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wa chikondi chopanda malire, Mulungu amene mumaleka kubweretsa tsoka.
3 and now LORD to take: take please [obj] soul: life my from me for pleasant death my from life my
Ndipo tsopano, Inu Yehova, ingondiphani basi, pakuti ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
4 and to say LORD be good to be incensed to/for you
Koma Yehova anayankha kuti, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye?”
5 and to come out: come Jonah from [the] city and to dwell from front: east to/for city and to make to/for him there booth and to dwell underneath: under her in/on/with shadow till which to see: see what? to be in/on/with city
Yona anatuluka mu mzindamo nakakhala pansi cha kummawa kwa mzindawo. Kumeneko anadzimangira chithando nakhala mʼmenemo mu mthunzi, kudikira kuti aone zimene zichitikire mzindawo.
6 and to count LORD God plant and to ascend: rise from upon to/for Jonah to/for to be shadow upon head his to/for to rescue to/for him from distress: harm his and to rejoice Jonah upon [the] plant joy great: large
Tsono Yehova Mulungu anameretsa msatsi ndi kuyikulitsa kuti ipereke mthunzi kwa Yona kuchotsa mavuto ake; ndipo Yona anasangalala kwambiri chifukwa cha msatsiyo.
7 and to count [the] God worm in/on/with to ascend: rise [the] dawn to/for morrow and to smite [obj] [the] plant and to wither
Koma tsiku linalo mmawa, Mulungu anabweretsa mbozi imene inadya msatsiyo ndipo inafota.
8 and to be like/as to rise [the] sun and to count God spirit: breath east scorching and to smite [the] sun upon head Jonah and to enwrap and to ask [obj] soul: myself his to/for to die and to say pleasant death my from life my
Dzuwa litatuluka, Yehova anabweretsa mphepo yotentha yochokera kummawa, ndipo dzuwa linatentha pamutu pa Yona kotero analenguka nalo. Iye anangofuna atafa, ndipo anati, “Ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
9 and to say God to(wards) Jonah be good to be incensed to/for you upon [the] plant and to say be good to be incensed to/for me till death
Koma Mulungu anati kwa Yona, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye chifukwa cha msatsi?” Iye anayankha kuti, “Inde nʼkoyenera. Kukwiya kwanga nʼkofuna kufa nako.”
10 and to say LORD you(m. s.) to pity upon [the] plant which not to toil in/on/with him and not to magnify him which/that son: type of night to be and son: type of night to perish
Koma Yehova anati, “Iwe ukumvera chisoni msatsiwo, ngakhale kuti sunawugwirire ntchito kapena kuwukulitsa. Inamera pa usiku umodzi ndipo inafanso pa usiku umodzi.
11 and I not to pity upon Nineveh [the] city [the] great: large which there in/on/with her to multiply from two ten ten thousand man which not to know between right his to/for left his and animal many
Koma mu Ninive muli anthu opitirira 120,000 amene sadziwa kusiyanitsa kuti chabwino nʼchiti ndipo choyipa nʼchiti, mulinso ziweto zochuluka. Kodi sindiyenera kumvera chisoni mzinda waukulu ngati uwu?”

< Jonah 4 >