< Job 37 >
1 also to/for this to tremble heart my and to start from place his
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 to hear: hear to hear: hear in/on/with turmoil voice his and moaning from lip his to come out: come
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 underneath: under all [the] heaven to free him and light his upon wing [the] land: country/planet
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 after him to roar voice to thunder in/on/with voice pride his and not to assail them for to hear: hear voice his
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 to thunder God in/on/with voice his to wonder to make: do great: large and not to know
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 for to/for snow to say to fall land: country/planet and rain rain and rain rain strength his
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 in/on/with hand all man to seal to/for to know all human deed: work his
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 and to come (in): come living thing in/at/by ambush and in/on/with habitation her to dwell
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 from [the] chamber to come (in): come whirlwind and from scattering wind cold
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 from breath God to give: give ice and width water in/on/with constraint
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 also in/on/with moisture to burden cloud to scatter cloud light his
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 and he/she/it surrounds to overturn (in/on/with counsel his *Q(K)*) to/for to work they all which to command them upon face: surface world land: country/planet [to]
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 if to/for tribe: staff if to/for land: country/planet his if to/for kindness to find him
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 to listen [emph?] this Job to stand: stand and to understand to wonder God
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 to know in/on/with to set: put god upon them and to shine light cloud his
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 to know upon swaying cloud wonder unblemished knowledge
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 which garment your hot in/on/with to quiet land: country/planet from south
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 to beat with him to/for cloud strong like/as mirror to pour: firm
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 to know us what? to say to/for him not to arrange from face: because darkness
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 to recount to/for him for to speak: speak if: surely no to say man: anyone for to swallow up
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 and now not to see: see light bright he/she/it in/on/with cloud and spirit: breath to pass and be pure them
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 from north gold to come upon god to fear: revere splendor
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 Almighty not to find him great strength and justice and abundance righteousness not to afflict
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 to/for so to fear: revere him human not to see: see all wise heart
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”