< Job 36 >

1 and to add: again Elihu and to say
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 to surround to/for me little and to explain you for still to/for god speech
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 to lift: bear knowledge my to/for from distant (and to/for to work me *LAB(h)*) to give: give righteousness
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 for truly not deception speech my unblemished knowledge with you
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 look! God mighty and not to reject mighty strength heart
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 not to live wicked and justice afflicted to give: give
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 not to dimish from righteous eye his and with king to/for throne and to dwell them to/for perpetuity and to exult
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 and if to bind in/on/with fetter to capture [emph?] in/on/with cord affliction
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 and to tell to/for them work their and transgression their for to prevail
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 and to reveal: uncover ear their to/for discipline: instruction and to say for to return: return [emph?] from evil: wickedness
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 if to hear: hear and to serve: minister to end: finish day their in/on/with good and year their in/on/with pleasant
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 and if not to hear: hear in/on/with missile to pass and to die like/as without knowledge
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 and profane heart to set: make face: anger not to cry for to bind them
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 to die in/on/with youth soul their and living thing their in/on/with male cult prostitute
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 to rescue afflicted in/on/with affliction his and to reveal: uncover in/on/with oppression ear their
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 and also to incite you from lip: opening enemy breadth not constraint underneath: stand her and quietness table your to fill ashes
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 and judgment wicked to fill judgment and justice to grasp
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 for rage lest to incite you in/on/with mockery and many ransom not to stretch you
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 to arrange cry your not in/on/with distress and all power strength
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 not to long for [the] night to/for to ascend: rise people underneath: stand them
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 to keep: careful not to turn to(wards) evil: wickedness for upon this to choose from affliction
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 look! God to exalt in/on/with strength his who? like him rain/teacher
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 who? to reckon: overseer upon him way: conduct his and who? to say to work injustice
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 to remember for to grow great work his which to sing human
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 all man to see in/on/with him human to look from distant
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 look! God great and not to know number year his and not search
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 for to dimish drop water to refine rain to/for mist his
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 which to flow cloud to drip upon man many
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 also if: surely yes to understand spreading cloud shout booth his
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 look! to spread upon him light his and root [the] sea to cover
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 for in/on/with them to judge people to give: give food to/for to increase
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 upon palm to cover light and to command upon her in/on/with to fall on
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 to tell upon him shouting his livestock also upon to ascend: rise
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >