< Job 20 >
1 and to answer Zophar [the] Naamathite and to say
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 to/for so disquietings my to return: reply me and in/on/with for the sake of to hasten I in/on/with me
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 discipline shame my to hear: hear and spirit from understanding my to answer me
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 this to know from perpetuity from to set: put man upon land: country/planet
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 for triumphing wicked from near and joy profane till moment
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 if to ascend: rise to/for heaven loftiness his and head his to/for cloud to touch
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 like/as dung his to/for perpetuity to perish to see: see him to say where? he
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 like/as dream to fly and not to find him and to wander like/as vision night
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 eye to see him and not to add: again and not still to see him place his
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 son: child his to accept poor and hand his to return: return strength his
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 bone his to fill (youth his *Q(K)*) and with him upon dust to lie down: lay down
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 if be sweet in/on/with lip his distress: evil to hide her underneath: under tongue his
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 to spare upon her and not to leave: release her and to withhold her in/on/with midst palate his
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 food his in/on/with belly his to overturn gall cobra in/on/with entrails: among his
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 strength: rich to swallow up and to vomit him from belly: abdomen his to possess: take him God
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 poison cobra to suckle to kill him tongue viper
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 not to see: see in/on/with stream river torrent: river honey and curd
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 to return: return toil and not to swallow up like/as strength: rich exchange his and not to rejoice
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 for to crush to leave: neglect poor house: home to plunder and not to build him
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 for not to know at ease in/on/with belly: abdomen his in/on/with to desire his not to escape
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 nothing survivor to/for to eat he upon so not be firm goodness his
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 in/on/with to fill sufficiency his be distressed to/for him all hand labour(er) to come (in): come him
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 to be to/for to fill belly: abdomen his to send: depart in/on/with him burning anger face: anger his and to rain upon them in/on/with intestine his
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 to flee from weapon iron to pass him bow bronze
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 to draw and to come out: come from back and lightning from gall his to go: come upon him terror
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 all darkness to hide to/for to treasure his to eat him fire not to breathe be evil survivor in/on/with tent his
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 to reveal: reveal heaven iniquity: crime his and land: country/planet to arise: attack to/for him
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 to reveal: remove crops house: home his to pour in/on/with day face: anger his
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 this portion man wicked from God and inheritance word his from God
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”