< Job 2 >

1 and to be [the] day and to come (in): come son: child [the] God to/for to stand upon LORD and to come (in): come also [the] Satan in/on/with midst their to/for to stand upon LORD
Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
2 and to say LORD to(wards) [the] Satan where? from this to come (in): come and to answer [the] Satan [obj] LORD and to say from to rove in/on/with land: country/planet and from to go: walk in/on/with her
Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
3 and to say LORD to(wards) [the] Satan to set: consider heart your to(wards) servant/slave my Job for nothing like him in/on/with land: country/planet man complete and upright afraid God and to turn aside: turn aside from bad: evil and still he to strengthen: hold in/on/with integrity his and to incite me in/on/with him to/for to swallow up him for nothing
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
4 and to answer [the] Satan [obj] LORD and to say skin about/through/for skin and all which to/for man to give: give about/through/for soul: life his
Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
5 but to send: reach please hand your and to touch to(wards) bone his and to(wards) flesh his if: surely yes not to(wards) face your to bless you
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
6 and to say LORD to(wards) [the] Satan look! he in/on/with hand your surely [obj] soul: life his to keep: guard
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
7 and to come out: come [the] Satan from with face LORD and to smite [obj] Job in/on/with boil bad: harmful from palm: sole foot his (and till *Q(K)*) crown his
Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
8 and to take: take to/for him earthenware to/for to scrape in/on/with him and he/she/it to dwell in/on/with midst [the] ashes
Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
9 and to say to/for him woman: wife his still you to strengthen: hold in/on/with integrity your to bless God and to die
Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
10 and to say to(wards) her like/as to speak: speak one [the] foolish to speak: speak also [obj] [the] good to receive from with [the] God and [obj] [the] bad: evil not to receive in/on/with all this not to sin Job in/on/with lips his
Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
11 and to hear: hear three neighbor Job [obj] all [the] distress: evil [the] this [the] to come (in): come upon him and to come (in): come man: anyone from place his Eliphaz [the] Temanite and Bildad [the] Shuhite and Zophar [the] Naamathite and to appoint together to/for to come (in): come to/for to wander to/for him and to/for to be sorry: comfort him
Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
12 and to lift: look [obj] eye: seeing their from distant and not to recognize him and to lift: loud voice their and to weep and to tear man: anyone robe his and to scatter dust upon head their [the] heaven [to]
Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
13 and to dwell with him to/for land: soil seven day and seven night and nothing to speak: speak to(wards) him word for to see: see for to magnify [the] pain much
Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.

< Job 2 >