< Jeremiah 50 >

1 [the] word which to speak: speak LORD to(wards) Babylon to(wards) land: country/planet Chaldea in/on/with hand: by Jeremiah [the] prophet
Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
2 to tell in/on/with nation and to hear: proclaim and to lift: raise ensign to hear: proclaim not to hide to say to capture Babylon be ashamed Bel to to be dismayed Merodach be ashamed idol her to to be dismayed idol her
“Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
3 for to ascend: rise upon her nation from north he/she/it to set: make [obj] land: country/planet her to/for horror: destroyed and not to be to dwell in/on/with her from man and till animal to wander to go: went
Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
4 in/on/with day [the] they(masc.) and in/on/with time [the] he/she/it utterance LORD to come (in): come son: descendant/people Israel they(masc.) and son: descendant/people Judah together to go: come and to weep to go: come and [obj] LORD God their to seek
“Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
5 Zion to ask way: road here/thus face their to come (in): come and to join to(wards) LORD covenant forever: enduring not to forget
Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
6 flock to perish (to be *Q(K)*) people my to pasture their to go astray them mountain: mount (turning back them *Q(K)*) from mountain: mount to(wards) hill to go: went to forget rest their
“Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
7 all to find them to eat them and enemy their to say not be guilty underneath: because of which to sin to/for LORD pasture righteousness and hope father their LORD
Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
8 to wander from midst Babylon and from land: country/planet Chaldea (to come out: come *Q(K)*) and to be like/as goat to/for face: before flock
“Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
9 for behold I to rouse and to ascend: establish upon Babylon assembly nation great: large from land: country/planet north and to arrange to/for her from there to capture arrow his like/as mighty man be prudent not to return: return emptily
Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
10 and to be Chaldea to/for spoil all to loot her to satisfy utterance LORD
Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
11 for (to rejoice *Q(K)*) for (to exult *Q(K)*) to plunder inheritance my for (to leap *Q(K)*) like/as heifer to tread (and to cry out *Q(K)*) like/as mighty: stallion
“Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
12 be ashamed mother your much be ashamed to beget you behold end nation wilderness dryness and plain
Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
13 from wrath LORD not to dwell and to be devastation all her all to pass upon Babylon be desolate: appalled and to whistle upon all wound her
Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
14 to arrange upon Babylon around all to tread bow to give thanks to(wards) her not to spare to(wards) arrow for to/for LORD to sin
“Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
15 to shout upon her around to give: give hand: power her to fall: fall (foundation her *Q(k)*) to overthrow wall her for vengeance LORD he/she/it to avenge in/on/with her like/as as which to make: do to make: do to/for her
Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
16 to cut: eliminate to sow from Babylon and to capture sickle in/on/with time harvest from face: before sword [the] to oppress man: anyone to(wards) people his to turn and man: anyone to/for land: country/planet his to flee
Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
17 sheep to scatter Israel lion to banish [the] first to eat him king Assyria and this [the] last be vast him Nebuchadnezzar king Babylon
“Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
18 to/for so thus to say LORD Hosts God Israel look! I to reckon: punish to(wards) king Babylon and to(wards) land: country/planet his like/as as which to reckon: punish to(wards) king Assyria
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 and to return: rescue [obj] Israel to(wards) pasture his and to pasture [the] Carmel and [the] Bashan and in/on/with mountain: mount Ephraim and [the] Gilead to satisfy soul: appetite his
Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 in/on/with day [the] they(masc.) and in/on/with time [the] he/she/it utterance LORD to seek [obj] iniquity: crime Israel and nothing he and [obj] sin Judah and not to find for to forgive to/for which to remain
Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
21 upon [the] land: country/planet Merathaim to ascend: rise upon her and to(wards) to dwell Pekod to slay and to devote/destroy after them utterance LORD and to make: do like/as all which to command you
“Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
22 voice: sound battle in/on/with land: country/planet and breaking great: large
Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
23 how? to cut down/off and to break hammer all [the] land: country/planet how? to be to/for horror: appalled Babylon in/on/with nation
Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
24 to snare to/for you and also to capture Babylon and you(f. s.) not to know to find and also to capture for in/on/with LORD to stir up
Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
25 to open LORD [obj] treasure his and to come out: send [obj] article/utensil indignation his for work he/she/it to/for Lord YHWH/God Hosts in/on/with land: country/planet Chaldea
Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
26 to come (in): come to/for her from end to open granary her to build her like heap and to devote/destroy her not to be to/for her remnant
Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
27 to slay all bullock her to go down to/for slaughter woe! upon them for to come (in): come day their time punishment their
Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
28 voice to flee and survivor from land: country/planet Babylon to/for to tell in/on/with Zion [obj] vengeance LORD God our vengeance temple his
Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
29 to hear: proclaim to(wards) Babylon archer all to tread bow to camp upon her around not (to be to/for her *Q(K)*) survivor to complete to/for her like/as work her like/as all which to make: do to make: do to/for her for to(wards) LORD to boil to(wards) holy Israel
“Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
30 to/for so to fall: kill youth her in/on/with street/plaza her and all human battle her to silence: silent in/on/with day [the] he/she/it utterance LORD
Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
31 look! I to(wards) you arrogance utterance Lord YHWH/God Hosts for to come (in): come day your time to reckon: punish you
“Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
32 and to stumble arrogance and to fall: fall and nothing to/for him to arise: establish and to kindle fire in/on/with city his and to eat all around him
Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
33 thus to say LORD Hosts to oppress son: descendant/people Israel and son: descendant/people Judah together and all to take captive them to strengthen: hold in/on/with them to refuse to send: let go them
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
34 to redeem: redeem their strong LORD Hosts name his to contend to contend [obj] strife their because to rest [obj] [the] land: country/planet and to tremble to/for to dwell Babylon
Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
35 sword upon Chaldea utterance LORD and to(wards) to dwell Babylon and to(wards) ruler her and to(wards) wise her
Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
36 sword to(wards) [the] bluster and be foolish sword to(wards) mighty man her and to to be dismayed
Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
37 sword to(wards) horse his and to(wards) chariot his and to(wards) all [the] racial-mix which in/on/with midst her and to be to/for woman sword to(wards) treasure her and to plunder
Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
38 drought to(wards) water her and to wither for land: country/planet idol he/she/it and in/on/with terror to be foolish
Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
39 to/for so to dwell wild beast with wild beast and to dwell in/on/with her daughter ostrich and not to dwell still to/for perpetuity and not to dwell till generation and generation
“Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
40 like/as overthrow God [obj] Sodom and [obj] Gomorrah and [obj] neighboring her utterance LORD not to dwell there man: anyone and not to sojourn in/on/with her son: child man
Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
41 behold people to come (in): come from north and nation great: large and king many to rouse from flank land: country/planet
“Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
42 bow and javelin to strengthen: hold cruel they(masc.) and not to have compassion voice: sound their like/as sea to roar and upon horse to ride to arrange like/as man to/for battle upon you daughter Babylon
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
43 to hear: hear king Babylon [obj] report their and to slacken hand his distress to strengthen: hold him agony like/as to beget
Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
44 behold like/as lion to ascend: rise from pride [the] Jordan to(wards) pasture strong for to disturb (to run: run them *Q(K)*) from upon her and who? to choose to(wards) her to reckon: overseer for who? like me and who? to appoint me and who? this to pasture which to stand: stand to/for face: before my
Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
45 to/for so to hear: hear counsel LORD which to advise to(wards) Babylon and plot his which to devise: devise to(wards) land: country/planet Chaldea if: surely yes not to drag them little [the] flock if: surely yes not be desolate: appalled upon them pasture
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
46 from voice: sound to capture Babylon to shake [the] land: country/planet and outcry in/on/with nation to hear: hear
Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.

< Jeremiah 50 >