< Jeremiah 42 >
1 and to approach: approach all ruler [the] strength: soldiers and Johanan son: child Kareah and Jezaniah son: child Hoshaiah and all [the] people from small and till great: large
Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
2 and to say to(wards) Jeremiah [the] prophet to fall: presenting please supplication our to/for face: before your and to pray about/through/for us to(wards) LORD God your about/through/for all [the] remnant [the] this for to remain little from to multiply like/as as which eye your to see: see [obj] us
kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
3 and to tell to/for us LORD God your [obj] [the] way: conduct which to go: went in/on/with her and [obj] [the] word: thing which to make: do
Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
4 and to say to(wards) them Jeremiah [the] prophet to hear: hear look! I to pray to(wards) LORD God your like/as word: speaking your and to be all [the] word: thing which to answer LORD [obj] you to tell to/for you not to withhold from you word: thing
Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
5 and they(masc.) to say to(wards) Jeremiah to be LORD in/on/with us to/for witness truth: true and be faithful if not like/as all [the] word which to send: depart you LORD God your to(wards) us so to make: do
Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
6 if good and if bad: evil in/on/with voice LORD God our which (we *Q(K)*) to send: depart [obj] you to(wards) him to hear: obey because which be good to/for us for to hear: obey in/on/with voice LORD God our
Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
7 and to be from end ten day and to be word LORD to(wards) Jeremiah
Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
8 and to call: call to to(wards) Johanan son: child Kareah and to(wards) all ruler [the] strength: soldiers which with him and to/for all [the] people to/for from small and till great: large
Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
9 and to say to(wards) them thus to say LORD God Israel which to send: depart [obj] me to(wards) him to/for to fall: presenting supplication your to/for face: before his
Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
10 if to return: again to dwell in/on/with land: country/planet [the] this and to build [obj] you and not to overthrow and to plant [obj] you and not to uproot for to be sorry: relent to(wards) [the] distress: harm which to make: do to/for you
“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
11 not to fear from face of king Babylon which you(m. p.) afraid from face of his not to fear from him utterance LORD for with you I to/for to save [obj] you and to/for to rescue [obj] you from hand: power his
Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
12 and to give: give to/for you compassion and to have compassion [obj] you and to return: rescue [obj] you to(wards) land: soil your
Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
13 and if to say you(m. p.) not to dwell in/on/with land: country/planet [the] this to/for lest to hear: obey in/on/with voice LORD God your
“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
14 to/for to say not for land: country/planet Egypt to come (in): come which not to see: see battle and voice: sound trumpet not to hear: hear and to/for food: bread not be hungry and there to dwell
ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
15 and now to/for so to hear: hear word LORD remnant Judah thus to say LORD Hosts God Israel if you(m. p.) to set: put to set: make [emph?] face your to/for to come (in): come Egypt and to come (in): come to/for to sojourn there
Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
16 and to be [the] sword which you(m. p.) afraid from her there to overtake [obj] you in/on/with land: country/planet Egypt and [the] famine which you(m. p.) be anxious from him there to cleave after you Egypt and there to die
ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
17 and to be all [the] human which to set: make [obj] face their to/for to come (in): come Egypt to/for to sojourn there to die in/on/with sword in/on/with famine and in/on/with pestilence and not to be to/for them survivor and survivor from face: before [the] distress: harm which I to come (in): bring upon them
Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
18 for thus to say LORD Hosts God Israel like/as as which to pour face: anger my and rage my upon to dwell Jerusalem so to pour rage my upon you in/on/with to come (in): come you Egypt and to be to/for oath and to/for horror: appalled and to/for curse and to/for reproach and not to see: see still [obj] [the] place [the] this
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
19 to speak: speak LORD upon you remnant Judah not to come (in): come Egypt to know to know for to testify in/on/with you [the] day
“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
20 for (to go astray *Q(K)*) in/on/with soul: life your for you(m. p.) to send: depart [obj] me to(wards) LORD God your to/for to say to pray about/through/for us to(wards) LORD God our and like/as all which to say LORD God our so to tell to/for us and to make: do
kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
21 and to tell to/for you [the] day: today and not to hear: obey in/on/with voice LORD God your and to/for all which to send: depart me to(wards) you
Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
22 and now to know to know for in/on/with sword in/on/with famine and in/on/with pestilence to die in/on/with place which to delight in to/for to come (in): come to/for to sojourn there
Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”