< Jeremiah 33 >
1 and to be word LORD to(wards) Jeremiah second and he/she/it still he to restrain in/on/with court [the] guardhouse to/for to say
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 thus to say LORD to make her LORD to form: formed [obj] her to/for to establish: establish her LORD name his
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 to call: call to to(wards) me and to answer you and to tell to/for you great: large and to gather/restrain/fortify not to know them
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 for thus to say LORD God Israel upon house: home [the] city [the] this and upon house: home king Judah [the] to tear to(wards) [the] mound and to(wards) [the] sword
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 to come (in): come to/for to fight with [the] Chaldea and to/for to fill them with corpse [the] man which to smite in/on/with face: anger my and in/on/with rage my and which to hide face my from [the] city [the] this upon all distress: evil their
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 look! I to ascend: establish to/for her health and healing and to heal them and to reveal: reveal to/for them abundance peace: well-being and truth: certain
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 and to return: rescue [obj] captivity Judah and [obj] captivity Israel and to build them like/as in/on/with first
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 and be pure them from all iniquity: guilt their which to sin to/for me and to forgive (to/for all *Q(K)*) iniquity: guilt their which to sin to/for me and which to transgress in/on/with me
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 and to be to/for me to/for name rejoicing to/for praise and to/for beauty to/for all nation [the] land: country/planet which to hear: hear [obj] all [the] welfare which I to make: do [obj] them and to dread and to tremble upon all [the] welfare and upon all [the] peace: well-being which I to make: offer to/for her
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 thus to say LORD still to hear: hear in/on/with place [the] this which you(m. p.) to say desolate he/she/it from nothing man and from nothing animal in/on/with city Judah and in/on/with outside Jerusalem [the] be desolate: destroyed from nothing man and from nothing to dwell and from nothing animal
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 voice rejoicing and voice joy voice son-in-law and voice daughter-in-law: bride voice to say to give thanks [obj] LORD Hosts for pleasant LORD for to/for forever: enduring kindness his to come (in): bring thanksgiving house: temple LORD for to return: rescue [obj] captivity [the] land: country/planet like/as in/on/with first to say LORD
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 thus to say LORD Hosts still to be in/on/with place [the] this [the] desolate from nothing man and till animal and in/on/with all city his pasture to pasture to stretch flock
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 in/on/with city [the] mountain: hill country in/on/with city [the] Shephelah and in/on/with city [the] Negeb and in/on/with land: country/planet Benjamin and in/on/with around Jerusalem and in/on/with city Judah still to pass [the] flock upon hand to count to say LORD
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 behold day to come (in): come utterance LORD and to arise: establish [obj] [the] word: promised [the] pleasant which to speak: promise to(wards) house: household Israel and upon house: household Judah
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 in/on/with day [the] they(masc.) and in/on/with time [the] he/she/it to spring to/for David branch righteousness and to make: do justice and righteousness in/on/with land: country/planet
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 in/on/with day [the] they(masc.) to save Judah and Jerusalem to dwell to/for security and this which to call: call by to/for her LORD Righteousness our
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 for thus to say LORD not to cut: lack to/for David man to dwell upon throne house: household Israel
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 and to/for priest [the] Levi not to cut: lack man from to/for face: before my to ascend: offer up burnt offering and to offer: burn offering and to make sacrifice all [the] day: always
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 and to be word LORD to(wards) Jeremiah to/for to say
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 thus to say LORD if to break [obj] covenant my [the] day and [obj] covenant my [the] night and to/for lest to be by day and night in/on/with time their
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 also covenant my to break with David servant/slave my from to be to/for him son: descendant/people to reign upon throne his and with [the] Levi [the] priest to minister me
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 which not to recount army [the] heaven and not to measure sand [the] sea so to multiply [obj] seed: children David servant/slave my and [obj] [the] Levi to minister [obj] me
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 and to be word LORD to(wards) Jeremiah to/for to say
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 not to see: see what? [the] people [the] this to speak: speak to/for to say two [the] family which to choose LORD in/on/with them and to reject them and [obj] people my to spurn [emph?] from to be still nation to/for face: before their
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 thus to say LORD if not covenant my by day and night statute heaven and land: country/planet not to set: make
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 also seed: children Jacob and David servant/slave my to reject from to take: take from seed: children his to rule to(wards) seed: children Abraham Isaac and Jacob for (to return: rescue *Q(K)*) [obj] captivity their and to have compassion them
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”