< Jeremiah 12 >

1 righteous you(m. s.) LORD for to contend to(wards) you surely justice: judgement to speak: speak with you why? way: journey wicked to prosper to prosper all to act treacherously treachery
Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
2 to plant them also to uproot to go: continue also to make fruit near you(m. s.) in/on/with lip their and distant from kidney their
Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
3 and you(m. s.) LORD to know me to see: see me and to test heart my with you to tear them like/as flock to/for slaughtered and to consecrate: prepare them to/for day slaughter
Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
4 till how to mourn [the] land: country/planet and vegetation all [the] land: country to wither from distress: evil to dwell in/on/with her to snatch animal and bird for to say not to see: see [obj] end our
Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
5 for with on foot to run: run and be weary you and how? to contend with [the] horse and in/on/with land: country/planet peace: well-being you(m. s.) to trust and how? to make: do in/on/with pride [the] Jordan
Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
6 for also brother: male-sibling your and house: household father your also they(masc.) to act treacherously in/on/with you also they(masc.) to call: call out after you full not be faithful in/on/with them for to speak: speak to(wards) you welfare
Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
7 to leave: forsake [obj] house: temple my to leave [obj] inheritance my to give: give [obj] beloved soul my in/on/with palm enemy her
“Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
8 to be to/for me inheritance my like/as lion in/on/with wood to give: cry out upon me in/on/with voice her upon so to hate her
Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
9 bird of prey variegated inheritance my to/for me bird of prey around upon her to go: went to gather all living thing [the] land: wildlife to come to/for food
Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 to pasture many to ruin vineyard my to trample [obj] portion my to give: make [obj] portion desire my to/for wilderness devastation
Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
11 to set: make her to/for devastated to mourn upon me devastation be desolate: destroyed all [the] land: country/planet for nothing man: anyone to set: put upon heart
Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
12 upon all bareness in/on/with wilderness to come (in): come to ruin for sword to/for LORD to eat from end land: country/planet and till end [the] land: country/planet nothing peace to/for all flesh
Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 to sow wheat and thorn to reap be weak: weak not to gain and be ashamed from produce your from burning anger face: anger LORD
Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
14 thus to say LORD upon all neighboring my [the] bad: evil [the] to touch in/on/with inheritance which to inherit [obj] people my [obj] Israel look! I to uproot them from upon land: soil their and [obj] house: household Judah to uproot from midst their
“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
15 and to be after to uproot I [obj] them to return: again and to have compassion them and to return: again them man: anyone to/for inheritance his and man: anyone to/for land: country/planet his
Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
16 and to be if to learn: learn to learn: teach [obj] way: conduct people my to/for to swear in/on/with name my alive LORD like/as as which to learn: learn [obj] people my to/for to swear in/on/with Baal and to build in/on/with midst people my
Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
17 and if not to hear: hear and to uproot [obj] [the] nation [the] he/she/it to uproot and to perish utterance LORD
Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

< Jeremiah 12 >