< Isaiah 66 >

1 thus to say LORD [the] heaven throne my and [the] land: country/planet footstool foot my where? this house: temple which to build to/for me and where? this place resting my
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 and [obj] all these hand my to make and to be all these utterance LORD and to(wards) this to look to(wards) afflicted and crippled spirit and trembling upon word my
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 to slaughter [the] cattle to smite man to sacrifice [the] sheep to break the neck dog to ascend: offer up offering blood swine to remember frankincense to bless evil: wickedness also they(masc.) to choose in/on/with way: conduct their and in/on/with abomination their soul their to delight in
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 also I to choose in/on/with caprice their and fear their to come (in): bring to/for them because to call: call to and nothing to answer to speak: speak and not to hear: hear and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye my and in/on/with in which not to delight in to choose
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 to hear: hear word LORD [the] trembling to(wards) word his to say brother: male-sibling your to hate you to put away you because name my to honor: honour LORD and to see: see in/on/with joy your and they(masc.) be ashamed
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 voice: sound roar from city voice: sound from temple voice: sound LORD to complete recompense to/for enemy his
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 in/on/with before to twist: writh in pain to beget in/on/with before to come (in): come pain to/for her and to escape male
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 who? to hear: hear like/as this who? to see: see like/as these to twist: writh in pain land: country/planet in/on/with day one if: surely no to beget nation beat one for to twist: writh in pain also to beget Zion [obj] son: child her
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 I to break and not to beget to say LORD if: surely no I [the] to beget and to restrain to say God your
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 to rejoice with Jerusalem and to rejoice in/on/with her all to love: lover her to rejoice with her rejoicing all [the] to mourn upon her
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 because to suckle and to satisfy from breast consolation her because to drink deeply and to delight from abundance glory her
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 for thus to say LORD look! I to stretch to(wards) her like/as river peace and like/as torrent: river to overflow glory nation and to suckle upon side to lift: bear and upon knee to delight
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 like/as man which mother his to be sorry: comfort him so I to be sorry: comfort you and in/on/with Jerusalem to be sorry: comfort
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 and to see: see and to rejoice heart your and bone your like/as grass to sprout and to know hand: power LORD with servant/slave his and be indignant [obj] enemy his
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 for behold LORD in/on/with fire to come (in): come and like/as whirlwind chariot his to/for to return: turn back in/on/with rage face: anger his and rebuke his in/on/with flame fire
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 for in/on/with fire LORD to judge and in/on/with sword his with all flesh and to multiply slain: killed LORD
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 [the] to consecrate: consecate and [the] be pure to(wards) [the] garden after (one *Q(K)*) in/on/with midst to eat flesh [the] swine and [the] detestation and [the] mouse together to cease utterance LORD
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 and I deed their and plot their to come (in): come to/for to gather [obj] all [the] nation and [the] tongue: language and to come (in): come and to see: see [obj] glory my
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 and to set: make in/on/with them sign: indicator and to send: depart from them survivor to(wards) [the] nation Tarshish Pul and Lud to draw bow Tubal and Greece [the] coastland [the] distant which not to hear: hear [obj] report my and not to see: see [obj] glory my and to tell [obj] glory my in/on/with Gentile
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 and to come (in): bring [obj] all brother: compatriot your from all [the] nation offering to/for LORD in/on/with horse and in/on/with chariot and in/on/with litter and in/on/with mule and in/on/with dromedary upon mountain: mount holiness my Jerusalem to say LORD like/as as which to come (in): bring son: descendant/people Israel [obj] [the] offering in/on/with article/utensil pure house: temple LORD
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 and also from them to take: take to/for priest to/for Levi to say LORD
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 for like/as as which [the] heaven [the] new and [the] land: country/planet [the] new which I to make to stand: stand to/for face: before my utterance LORD so to stand: stand seed: children your and name your
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 and to be from sufficiency month: new moon in/on/with month: new moon his and from sufficiency Sabbath in/on/with Sabbath his to come (in): come all flesh to/for to bow to/for face: before my to say LORD
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 and to come out: come and to see: see in/on/with corpse [the] human [the] to transgress in/on/with me for worm their not to die and fire their not to quench and to be abhorrence to/for all flesh
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

< Isaiah 66 >