< Isaiah 6 >
1 in/on/with year death [the] king Uzziah and to see: see [obj] Lord to dwell upon throne to exalt and to lift: raise and hem his to fill [obj] [the] temple
Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
2 Seraph to stand: stand from above to/for him six wing six wing to/for one in/on/with two to cover face his and in/on/with two to cover foot his and in/on/with two to fly
Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
3 and to call: call to this to(wards) this and to say holy holy holy LORD Hosts fullness all [the] land: country/planet glory his
Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
4 and to shake foundation [the] threshold from voice [the] to call: call to and [the] house: temple to fill smoke
Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
5 and to say woe! to/for me for to cease for man unclean lips I and in/on/with midst people unclean lips I to dwell for [obj] [the] king LORD Hosts to see: see eye my
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
6 and to fly to(wards) me one from [the] Seraph and in/on/with hand his glowing stone in/on/with tong to take: take from upon [the] altar
Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
7 and to touch upon lip my and to say behold to touch this upon lips your and to turn aside: remove iniquity: guilt your and sin your to atone
Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
8 and to hear: hear [obj] voice Lord to say [obj] who? to send: depart and who? to go: went to/for us and to say look! I to send: depart me
Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
9 and to say to go: went and to say to/for people [the] this to hear: hear to hear: hear and not to understand and to see: see to see: see and not to know
Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
10 to grow fat heart [the] people [the] this and ear his to honor: heavy and eye his to smear lest to see: see in/on/with eye his and in/on/with ear his to hear: hear and heart his to understand and to return: repent and to heal to/for him
Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
11 and to say till how Lord and to say till which if: until to crash city from nothing to dwell and house: home from nothing man and [the] land: soil to crash devastation
Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
12 and to remove LORD [obj] [the] man and to multiply [the] desolation in/on/with entrails: among [the] land: country/planet
mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
13 and still in/on/with her tenth and to return: again and to be to/for to burn: burn like/as oak and like/as oak which in/on/with felling pillar in/on/with them seed: children holiness pillar her
Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”