< Isaiah 58 >

1 to call: call out in/on/with throat not to withhold like/as trumpet to exalt voice your and to tell to/for people my transgression their and to/for house: household Jacob sin their
“Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
2 and [obj] me day: daily day: daily to seek [emph?] and knowledge way: conduct my to delight in [emph?] like/as nation which righteousness to make: do and justice: judgement God his not to leave: forsake to ask me justice righteousness nearness God to delight in [emph?]
Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
3 to/for what? to fast and not to see: see to afflict soul: myself our and not to know look! in/on/with day fast your to find pleasure and all worker your to oppress
Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
4 look! to/for strife and strife to fast and to/for to smite in/on/with fist wickedness not to fast like/as day to/for to hear: hear in/on/with height voice your
Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
5 like/as this to be fast to choose him day to afflict man soul: myself his to/for to bend like/as bulrush head his and sackcloth and ashes to lay to/for this to call: call by fast and day acceptance to/for LORD
Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
6 not this fast to choose him to open bond wickedness to free band yoke and to send: let go to crush free and all yoke to tear
“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
7 not to divide to/for hungry food: bread your and afflicted wandering to come (in): bring house: home for to see: see naked and to cover him and from flesh your not to conceal
Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
8 then to break up/open like/as dawn light your and health your haste to spring and to go: went to/for face: before your righteousness your glory LORD to gather you
Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
9 then to call: call to and LORD to answer to cry and to say look! I if to turn aside: turn aside from midst your yoke to send: depart finger and to speak: speak evil: wickedness
Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
10 and to promote to/for hungry soul: myself your and soul: appetite to afflict to satisfy and to rise in/on/with darkness light your and darkness your like/as midday
Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
11 and to lead you LORD continually and to satisfy in/on/with scorched soul: appetite your and bone your to arm and to be like/as garden watered and like/as exit water which not to lie water his
Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
12 and to build from you desolation forever: antiquity foundation generation and generation to arise: establish and to call: call by to/for you to wall up/off breach to return: rescue path to/for to dwell
Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
13 if to return: repent from Sabbath foot your to make: do pleasure your in/on/with day holiness my and to call: call by to/for Sabbath delight to/for holy LORD to honor: honour and to honor: honour him from to make: do way: conduct your from to find pleasure your and to speak: speak word: thing
“Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
14 then to delight upon LORD and to ride you upon (high place *Q(k)*) land: country/planet and to eat you inheritance Jacob father your for lip LORD to speak: speak
mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.

< Isaiah 58 >