< Isaiah 30 >
1 woe! son: child to rebel utterance LORD to/for to make: do counsel and not from me and to/for to pour liquid and not spirit my because to snatch sin upon sin
Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine, nachita mgwirizano wawowawo koma osati motsogozedwa ndi Ine. Choncho amanka nachimwirachimwira.
2 [the] to go: went to/for to go down Egypt and lip: word my not to ask to/for to seek refuge in/on/with security Pharaoh and to/for to seek refuge in/on/with shadow Egypt
Amapita ku Igupto kukapempha thandizo koma osandifunsa; amathawira kwa Farao kuti awateteze, ku Igupto amafuna malo opulumulira.
3 and to be to/for you security Pharaoh to/for shame and [the] refuge in/on/with shadow Egypt to/for shame
Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu, malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.
4 for to be in/on/with Zoan ruler his and messenger his Hanes to touch
Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani, ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,
5 all (be ashamed *Q(K)*) upon people not to gain to/for them not to/for helper and not to/for to gain for to/for shame and also to/for reproach
aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi chifukwa cha anthu opanda nawo phindu, amene sabweretsa thandizo kapena phindu, koma manyazi ndi mnyozo.”
6 oracle animal Negeb in/on/with land: country/planet distress and anguish lion and lion from them viper and serpent to fly to lift: bear upon shoulder colt strength: rich their and upon hump camel treasure their upon people not to gain
Uthenga wonena za nyama za ku Negevi: Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa, mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi, mphiri ndi njoka zaululu. Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo, kupita nazo kwa mtundu wa anthu umene sungawathandize.
7 and Egypt vanity and vain to help to/for so to call: call by to/for this Rahab they(masc.) cessation
Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe. Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha Rahabe chirombo cholobodoka.
8 now to come (in): come to write her upon tablet with them and upon scroll: book to decree her and to be to/for day last to/for perpetuity till forever: enduring
Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita, ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha masiku a mʼtsogolo.
9 for people rebellion he/she/it son: child deceptive son: child not be willing to hear: hear instruction LORD
Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi osafuna kumvera malangizo a Yehova.
10 which to say to/for seer not to see: seer and to/for seer not to see to/for us upright to speak: speak to/for us smoothness to see deception
Iwo amawuza alosi kuti, ‘Musationerenso masomphenya!’ Ndipo amanena kwa mneneri kuti, ‘Musatinenerenso zoona,’ mutiwuze zotikomera, munenere za mʼmutu mwanu.
11 to turn aside: depart from way: journey to stretch from way to cease from face: before our [obj] holy Israel
Patukani pa njira ya Yehova, lekani kutsata njira ya Yehova; ndipo tisamvenso mawu a Woyerayo uja wa Israeli!”
12 to/for so thus to say holy Israel because to reject you in/on/with word [the] this and to trust in/on/with oppression and be devious and to lean upon him
Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti, “Popeza inu mwakana uthenga uwu, mumakhulupirira zopondereza anzanu ndipo mumadalira kuchita zoyipa,
13 to/for so to be to/for you [the] iniquity: crime [the] this like/as breach to fall: fall to enquire in/on/with wall to exalt which suddenly to/for suddenness to come (in): come breaking her
choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu pa khoma lalitali ndi lopendama limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.
14 and to break her like/as breaking bag to form: potter to crush not to spare and not to find in/on/with fragment his earthenware to/for to snatch up fire from to burn and to/for to strip water from cistern
Lidzaphwanyika ngati mbiya imene yanyenyekeratu, mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale lopalira moto mʼngʼanjo kapena lotungira madzi mʼchitsime.”
15 for thus to say Lord YHWH/God holy Israel in/on/with returning and quietness to save [emph?] in/on/with to quiet and in/on/with trust to be might your and not be willing
Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi: “Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka, ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu, koma inu munakana zimenezi.
16 and to say not for upon horse to flee upon so to flee [emph?] and upon swift to ride upon so to lighten to pursue you
Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa, tidzakwera pa akavalo aliwiro.’ Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro, koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.
17 thousand one from face: because rebuke one from face: because rebuke five to flee till if: until to remain like/as mast upon head: top [the] mountain: mount and like/as ensign upon [the] hill
Anthu 1,000 mwa inu adzathawa poona mdani mmodzi; poona adani asanu okha nonsenu mudzathawa. Otsala anu adzakhala ngati mbendera pa phiri, ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”
18 and to/for so to wait LORD to/for be gracious you and to/for so to exalt to/for to have compassion you for God justice LORD blessed all to wait to/for him
Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima, iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo. Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo. Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!
19 for people in/on/with Zion to dwell in/on/with Jerusalem to weep not to weep be gracious be gracious you to/for voice: sound to cry out you like/as to hear: hear he to answer you
Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani.
20 and to give: give to/for you Lord food: bread distress and water oppression and not to corner still rain/teacher your and to be eye your to see: see [obj] rain/teacher your
Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo.
21 and ear your to hear: hear word from after you to/for to say this [the] way: road to go: walk in/on/with him for to turn right and for to go left
Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.”
22 and to defile [obj] plating idol silver: money your and [obj] ephod liquid gold your to scatter them like sick excrement to say to/for him
Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”
23 and to give: give rain seed your which to sow [obj] [the] land: soil and food: bread produce [the] land: soil and to be fat and rich to pasture livestock your in/on/with day [the] he/she/it pasture to enlarge
Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka.
24 and [the] cattle and [the] colt to serve: labour [the] land: soil fodder salted to eat which to scatter in/on/with shovel and in/on/with pitchfork
Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo.
25 and to be upon all mountain: mount high and upon all hill to lift: raise stream stream water in/on/with day slaughter many in/on/with to fall: fall tower
Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono.
26 and to be light [the] moon like/as light [the] heat and light [the] heat to be sevenfold like/as light seven [the] day in/on/with day to saddle/tie LORD [obj] breaking people his and wound wound his to heal
Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.
27 behold name LORD to come (in): come from distance to burn: burn face: anger his and heaviness smoke lips his to fill indignation and tongue his like/as fire to eat
Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali, ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka. Iye wayankhula mwaukali kwambiri, ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.
28 and spirit: breath his like/as torrent: river to overflow till neck to divide to/for to wave nation in/on/with sieve vanity: vain and bridle to go astray upon jaw people
Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira, wa madzi ofika mʼkhosi. Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza; Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo, kuti ziwasocheretse.
29 [the] song to be to/for you like/as night to consecrate: consecate feast and joy heart like/as to go: went in/on/with flute to/for to come (in): come in/on/with mountain: mount LORD to(wards) rock Israel
Ndipo inu mudzayimba mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika. Mudzasangalala ngati anthu oyimba zitoliro popita ku phiri la Yehova, thanthwe la Israeli.
30 and to hear: hear LORD [obj] splendor voice his and descent arm his to see: see in/on/with rage face: anger and flame fire to eat storm and storm and stone hail
Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa, mphenzi, namondwe ndi matalala.
31 for from voice LORD to to be dismayed Assyria in/on/with tribe: staff to smite
Asiriya adzaopa liwu la Yehova, ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.
32 and to be all ford tribe: rod appointment which to rest LORD upon him in/on/with tambourine and in/on/with lyre and in/on/with battle wave offering to fight (in/on/with them *Q(K)*)
Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo, anthu ake adzakhala akuvina nyimbo zoyimbira matambolini ndi azeze, Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.
33 for to arrange from previously burning-place also (he/she/it *Q(K)*) to/for king to establish: prepare be deep to enlarge pile her fire and tree: wood to multiply breath LORD like/as torrent: river brimstone to burn: burn in/on/with her
Malo otenthera zinthu akonzedwa kale; anakonzera mfumu ya ku Asiriya. Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu, ndipo muli nkhuni zambiri; mpweya wa Yehova, wangati mtsinje wa sulufule, udzayatsa motowo pa nkhunizo.