< Genesis 35 >

1 and to say God to(wards) Jacob to arise: rise to ascend: rise Bethel Bethel and to dwell there and to make there altar to/for God [the] to see: see to(wards) you in/on/with to flee you from face: before Esau brother: male-sibling your
Tsono Mulungu anati kwa Yakobo, “Nyamuka uchoke kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ukamange guwa lansembe la Mulungu amene anadza kwa iwe pamene umathawa Esau, mʼbale wako.”
2 and to say Jacob to(wards) house: household his and to(wards) all which with him to turn aside: remove [obj] God [the] foreign which in/on/with midst your and be pure and to pass mantle your
Choncho Yakobo anawuza a pa banja pake ndi onse amene anali naye kuti, “Chotsani milungu yachilendo imene muli nayo, ndipo mudziyeretse nokha ndi kusintha zovala zanu.
3 and to arise: rise and to ascend: rise Bethel Bethel and to make there altar to/for God [the] to answer [obj] me in/on/with day distress my and to be with me me in/on/with way: journey which to go: went
Tiyeni tinyamuke kuchoka kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ndikamumangira guwa lansembe Mulungu amene anandithandiza pa nthawi za masautso anga, komanso amene wakhala nane mʼmayendedwe anga onse.”
4 and to give: give to(wards) Jacob [obj] all God [the] foreign which in/on/with hand: themselves their and [obj] [the] ring which in/on/with ear their and to hide [obj] them Jacob underneath: under [the] oak which with Shechem
Choncho anamupatsa Yakobo milungu yachilendo yonse imene anali nayo pamodzi ndi ndolo. Iye anazikwirira pansi pa mtengo wa thundu ku Sekemu.
5 and to set out and to be terror God upon [the] city which around them and not to pursue after son: child Jacob
Pamenepo ananyamuka, ndipo mtima woopa Mulungu unagwera anthu onse a mʼmizinda yozungulira, kotero kuti palibe aliyense amene anatsatira banja la Yakobo.
6 and to come (in): come Jacob Luz [to] which in/on/with land: country/planet Canaan he/she/it Bethel Bethel he/she/it and all [the] people which with him
Yakobo ndi anthu onse anali naye aja anafika ku Luzi (ku Beteli) mu dziko la Kanaani.
7 and to build there altar and to call: call to to/for place El-bethel El-bethel El-bethel for there to reveal: reveal to(wards) him [the] God in/on/with to flee he from face: before brother: male-sibling his
Kumeneko anamanga guwa lansembe nalitcha Eli Beteli, chifukwa kunali kumeneko kumene Mulungu anadziwulula yekha kwa Yakobo pamene ankathawa mʼbale wake.
8 and to die Deborah to suckle Rebekah and to bury from underneath: under to/for Bethel Bethel underneath: under [the] oak and to call: call by name his Allon-bacuth Allon-bacuth
Debora mlezi wa Rakele anamwalira komweko nayikidwa mʼmanda pansi pa mtengo wa thundu cha kumunsi kwa Beteli. Choncho panatchedwa Aloni-Bakuti (mtengo wamaliro).
9 and to see: see God to(wards) Jacob still in/on/with to come (in): come he from Paddan (Paddan)-aram and to bless [obj] him
Yakobo atabwera kuchokera ku Padanaramu, Mulungu anabweranso kwa iye namudalitsa.
10 and to say to/for him God name your Jacob not to call: call to (name your *LBH(a)*) still Jacob that if: except if: except Israel to be name your and to call: call to [obj] name his Israel
Mulungu anati kwa iye, “Dzina lako ndiwe Yakobo, koma sudzatchedwanso Yakobo; koma udzatchedwa Israeli.” Choncho anamutcha iye Israeli.
11 and to say to/for him God I God Almighty be fruitful and to multiply nation and assembly nation to be from you and king from loin your to come out: produce
Ndipo Mulungu anati kwa iye, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse; berekanani ndi kuchulukana. Mtundu wa anthu, inde, mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe, ndipo ena mwa zidzukulu zako adzakhala mafumu.
12 and [obj] [the] land: country/planet which to give: give to/for Abraham and to/for Isaac to/for you to give: give her and to/for seed: children your after you to give: give [obj] [the] land: country/planet
Dziko limene ndinapereka kwa Abrahamu ndi Isake ndiliperekanso kwa iwe. Lidzakhala lako ndi la zidzukulu zako.”
13 and to ascend: rise from upon him God in/on/with place which to speak: speak with him
Kenaka Mulungu anamusiya Yakobo.
14 and to stand Jacob pillar in/on/with place which to speak: speak with him pillar stone and to pour upon her drink offering and to pour: pour upon her oil
Yakobo anayika mwala wachikumbutso pa malo pamene Mulungu anayankhula naye paja. Iye anathirapo nsembe yachakumwa ndi yamafuta.
15 and to call: call by Jacob [obj] name [the] place which to speak: speak with him there God Bethel Bethel
Yakobo anawatcha malo amene Mulungu anayankhula naye aja kuti Beteli.
16 and to set out from Bethel Bethel and to be still distance [the] land: country/planet to/for to come (in): towards Ephrath and to beget Rachel and to harden in/on/with to beget she
Kenaka anachoka ku Beteli. Koma ali pafupi kufika ku Efurata nthawi yakuti Rakele aone mwana inakwana. Iye anavutika pobereka.
17 and to be in/on/with to harden she in/on/with to beget she and to say to/for her [the] to beget not to fear for also this to/for you son: child
Akanali chivutikire choncho, mzamba anamulimbikitsa nati, “Usaope pakuti ubala mwana wina wamwamuna.”
18 and to be in/on/with to come out: come soul her for to die and to call: call by name his Ben-oni Ben-oni and father his to call: call by to/for him Benjamin
Tsono pamene Rakele ankapuma wefuwefu (popeza ankamwalira) iye anatcha mwana uja kuti Beni-Oni. Koma abambo ake anamutcha kuti Benjamini.
19 and to die Rachel and to bury in/on/with way: road Ephrath he/she/it Bethlehem Bethlehem
Choncho Rakele anamwalira ndipo anayikidwa pa njira yopita ku Efurata (Kumeneko ndiye ku Betelehemu).
20 and to stand Jacob pillar upon tomb her he/she/it pillar tomb Rachel till [the] day: today
Pa manda ake, Yakobo anayimika mwala wachikumbutso wa pa manda ndipo ulipobe mpaka lero.
21 and to set out Israel and to stretch (tent his *Q(K)*) from further to/for tower of Eder tower of Eder
Israeli (Yakobo) anasunthanso nakamanga tenti yake kupitirira nsanja ya Ederi.
22 and to be in/on/with to dwell Israel in/on/with land: country/planet [the] he/she/it and to go: went Reuben (and to lie down: have sex *L(p)*) [obj] (Bilhah *L(p)*) concubine (father his *L(p)*) and to hear: hear (Israel *L(p)*) and to be son: child Jacob two ten
Israeli akanali mʼderali, Rubeni anapita nakagonana ndi Biliha, mdzakazi wa abambo ake. Yakobo uja anazimva zimenezi. Yakobo anali ndi ana aamuna khumi ndi awiri:
23 son: child Leah firstborn Jacob Reuben and Simeon and Levi and Judah and Issachar and Zebulun
Ana a Leya ndi awa: Rubeni anali mwana woyamba wa Yakobo, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, ndi Zebuloni.
24 son: child Rachel Joseph and Benjamin
Ana a Rakele ndi awa: Yosefe ndi Benjamini.
25 and son: child Bilhah maidservant Rachel Dan and Naphtali
Ana a Biliha, wantchito wa Rakele ndi awa: Dani ndi Nafutali.
26 and son: child Zilpah maidservant Leah Gad and Asher these son: child Jacob which to beget to/for him in/on/with Paddan (Paddan)-aram
Ana a Zilipa wantchito wa Leya ndi awa: Gadi ndi Aseri. Awa ndiwo ana a Yakobo amene anabadwira ku Padanaramu.
27 and to come (in): come Jacob to(wards) Isaac father his Mamre Kiriath-arba Kiriath-arba he/she/it Hebron which to sojourn there Abraham and Isaac
Yakobo anafika ku mudzi kwa abambo ake Isake ku Mamre, (kumene kunkatchedwa ku Kiriyati-Ariba kapenanso Hebroni) kumene Abrahamu ndi Isake anakhalako kale.
28 and to be day Isaac hundred year and eighty year
Isake anakhala ndi moyo zaka 180.
29 and to die Isaac and to die and to gather to(wards) kinsman his old and sated day and to bury [obj] him Esau and Jacob son: child his
Anamwalira ali wokalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. Ndipo ana ake Esau ndi Yakobo anamuyika mʼmanda.

< Genesis 35 >