< Genesis 33 >
1 and to lift: look Jacob eye his and to see: see and behold Esau to come (in): come and with him four hundred man and to divide [obj] [the] youth upon Leah and upon Rachel and upon two [the] maidservant
Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja.
2 and to set: put [obj] [the] maidservant and [obj] youth their first and [obj] Leah and youth her last and [obj] Rachel and [obj] Joseph last
Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe.
3 and he/she/it to pass to/for face: before their and to bow land: soil [to] seven beat till to approach: approach he till brother: male-sibling his
Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.
4 and to run: run Esau to/for to encounter: meet him and to embrace him and to fall: fall upon (neck his *Q(k)*) and to kiss him and to weep
Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira.
5 and to lift: look [obj] eye his and to see: see [obj] [the] woman and [obj] [the] youth and to say who? these to/for you and to say [the] youth which be gracious God [obj] servant/slave your
Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?” Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”
6 and to approach: approach [the] maidservant they(fem.) and youth their and to bow
Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi.
7 and to approach: approach also Leah and youth her and to bow and after to approach: approach Joseph and Rachel and to bow
Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.
8 and to say who? to/for you all [the] camp [the] this which to meet and to say to/for to find favor in/on/with eye: seeing lord my
Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?” Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”
9 and to say Esau there to/for me many brother: male-sibling my to be to/for you which to/for you
Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”
10 and to say Jacob not please if please to find favor in/on/with eye: seeing your and to take: recieve offering: gift my from hand my for as that: since as as to see: see face your like/as to see: see face God and to accept me
Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu.
11 to take: recieve please [obj] blessing my which to come (in): bring to/for you for be gracious me God and for there to/for me all and to press in/on/with him and to take: recieve
Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.
12 and to say to set out and to go: journey and to go: went to/for before you
Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”
13 and to say to(wards) him lord my to know for [the] youth tender and [the] flock and [the] cattle to nurse upon me and to beat them day one and to die all [the] flock
Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.
14 to pass please lord my to/for face: before servant/slave his and I (to guide *LBH(a)*) to/for softly my to/for foot [the] work which to/for face: before my and to/for foot [the] youth till which to come (in): come to(wards) lord my Seir [to]
Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”
15 and to say Esau to set please with you from [the] people which with me and to say to/for what? this to find favor in/on/with eye: seeing lord my
Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.” Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”
16 and to return: return in/on/with day [the] he/she/it Esau to/for way: road his Seir [to]
Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri.
17 and Jacob to set out Succoth [to] and to build to/for him house: home and to/for livestock his to make booth upon so to call: call by name [the] place Succoth
Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.
18 and to come (in): come Jacob complete city Shechem which in/on/with land: country/planet Canaan in/on/with to come (in): come he from Paddan (Paddan)-aram and to camp with face: before [the] city
Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo.
19 and to buy [obj] portion [the] land: country which to stretch there tent his from hand: to son: child Hamor father Shechem in/on/with hundred coin
Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva.
20 and to stand there altar and to call: call to to/for him El (Elohe) (LORD)-Elohe Jacob
Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.