< Genesis 25 >
1 and to add Abraham and to take: marry woman: wife and name her Keturah
Abrahamu anakwatira mkazi wina dzina lake Ketura.
2 and to beget to/for him [obj] Zimran and [obj] Jokshan and [obj] Medan and [obj] Midian and [obj] Ishbak and [obj] Shuah
Iyeyu anamubalira Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa.
3 and Jokshan to beget [obj] Sheba and [obj] Dedan and son: descendant/people Dedan to be Asshurim and Letushim and Leummim
Yokisani anabereka Seba ndi Dedani ndipo zidzukulu za Dedani ndiwo Aasuri, Aletusi, ndi Aleumi.
4 and son: descendant/people Midian Ephah and Epher and Hanoch and Abida and Eldaah all these son: descendant/people Keturah
Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura.
5 and to give: give Abraham [obj] all which to/for him to/for Isaac
Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho.
6 and to/for son: child [the] concubine which to/for Abraham to give: give Abraham gift and to send: depart them from upon Isaac son: child his in/on/with still he alive east [to] to(wards) land: country/planet front: east
Koma pamene anali ndi moyo, Abrahamu anapereka mphatso kwa ana aakazi ake ena onse. Kenaka anawatumiza ku dziko la kummawa kuti akhale kutali ndi mwana wake Isake.
7 and these day year life Abraham which to live hundred year and seventy year and five year
Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175.
8 and to die and to die Abraham in/on/with greyheaded pleasant old and sated and to gather to(wards) kinsman his
Abrahamu anamwalira atakalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
9 and to bury [obj] him Isaac and Ishmael son: child his to(wards) cave [the] Machpelah to(wards) land: country Ephron son: child Zohar [the] Hittite which upon face: before Mamre
Ana ake, Isake ndi Ismaeli anamuyika mʼphanga la Makipela pafupi ndi Mamre, mʼmunda umene kale unali wa Efroni mwana wa Zohari Mhiti,
10 [the] land: country which to buy Abraham from with son: descendant/people Heth there [to] to bury Abraham and Sarah woman: wife his
uwu ndi munda umene Abrahamu anagula kwa Ahiti. Kumeneko Abrahamu anakayikidwa pamodzi ndi mkazi wake Sara.
11 and to be after death Abraham and to bless God [obj] Isaac son: child his and to dwell Isaac with Beer-lahai-roi Beer-lahai-roi Beer-lahai-roi
Atamwalira Abrahamu, Mulungu anadalitsa mwana wake Isake, amene ankakhala pafupi ndi Beeri-lahai-roi (chitsime cha Wamoyo Wondipenya).
12 and these generation Ishmael son: child Abraham which to beget Hagar [the] Egyptian maidservant Sarah to/for Abraham
Nazi zidzukulu za Ismaeli, mwana wa Abrahamu amene wantchito wa Sara, Hagara Mwigupto uja, anaberekera Abrahamu.
13 and these name son: child Ishmael in/on/with name their to/for generation their firstborn Ishmael Nebaioth and Kedar and Adbeel and Mibsam
Awa ndi mayina a ana a Ismaeli monga mwa mndandanda wa mabadwidwe awo: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli; kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu,
14 and Mishma and Dumah and Massa
Misima, Duma, Masa,
15 (Hadad *LA(BH)*) and Tema Jetur Naphish and Kedemah
Hadadi, Tema, Yeturi, Nafisi ndi Kedema;
16 these they(masc.) son: child Ishmael and these name their in/on/with village their and in/on/with encampment their two ten leader to/for people their
Amenewa ndi ana a Ismaeli ndi mayina awo monga mwa midzi ndi misasa yawo. Anali olamulira mafuko khumi ndi awiri.
17 and these year life Ishmael hundred year and thirty year and seven year and to die and to die and to gather to(wards) kinsman his
Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
18 and to dwell from Havilah till Shur which upon face: before Egypt to come (in): towards you Assyria [to] upon face: before all brother: male-relative his to fall: fall
Zidzukulu za Ismaeli zinkakhala mʼdera la pakati pa Havila ndi Suri, kummwera kwa Igupto, mukamapita cha ku Asuri. Choncho anakhala kummawa kwa abale awo.
19 and these generation Isaac son: child Abraham Abraham to beget [obj] Isaac
Iyi ndi mbiri ya Isake mwana wa Abrahamu. Abrahamu anabereka Isake
20 and to be Isaac son: aged forty year in/on/with to take: marry he [obj] Rebekah daughter Bethuel [the] Aramean from Paddan (Paddan)-aram sister Laban [the] Aramean to/for him to/for woman: wife
ndipo Isake anali ndi zaka makumi anayi pamene anakwatira Rebeka mwana wa Betueli Mwaramu wa ku Padanaramu mlongo wa Labani Mwaramu.
21 and to pray Isaac to/for LORD to/for before woman: wife his for barren he/she/it and to pray to/for him LORD and to conceive Rebekah woman: wife his
Isake anapempherera mkazi wake kwa Yehova popeza iye anali wosabereka. Yehova anayankha pemphero lake ndipo mkazi wake Rebeka anatenga pathupi.
22 and to crush [the] son: child in/on/with entrails: among her and to say if so to/for what? this I and to go: went to/for to seek [obj] LORD
Koma pamene anawo amalimbana mʼmimba mwake, iye anati, “Bwanji zikundichitikira zoterezi?” Choncho anapita kukafunsa kwa Yehova.
23 and to say LORD to/for her two (nation *Q(k)*) in/on/with belly: womb your and two people from belly your to separate and people from people to strengthen and many to serve little
Yehova anati kwa iye, “Udzabala mafuko awiri a anthu olimbana, ndipo magulu awiri a anthu ochokera mwa iwe adzasiyana; fuko limodzi lidzakhala la mphamvu kuposa linzake, ndipo wamkulu adzatumikira wamngʼono.”
24 and to fill day her to/for to beget and behold twin in/on/with belly: womb her
Pamene nthawi inakwana yakuti abeleke, Rebeka anaberekadi mapasa.
25 and to come out: produce [the] first red all his like/as clothing hair and to call: call by name his Esau
Woyamba kubadwa anali wofiira, ndipo thupi lake lonse linali ngati chovala cha ubweya; choncho anamutcha Esau.
26 and after so to come out: produce brother: male-sibling his and hand his to grasp in/on/with heel Esau and to call: call by name his Jacob and Isaac son: aged sixty year in/on/with to beget [obj] them
Kenaka mʼbale wake anabadwa atagwira chidendene cha Esau; choncho anamutcha Yakobo. Isake anali ndi zaka 60 pamene Rebeka anabereka mapasawa.
27 and to magnify [the] youth and to be Esau man to know wild game man land: country and Jacob man complete to dwell tent
Anyamatawo anakula ndipo Esau anakhala katswiri wosaka, munthu wamʼthengo, pamene Yakobo anali munthu wofatsa, wokonda kukhala pa nyumba.
28 and to love: lover Isaac [obj] Esau for wild game in/on/with lip his and Rebekah to love: lover [obj] Jacob
Isake ankakonda Esau chifukwa cha nyama za kutchire zomwe ankakonda kudya, koma Rebeka ankakonda Yakobo.
29 and to boil Jacob stew and to come (in): come Esau from [the] land: country and he/she/it faint
Tsiku lina pamene Yakobo ankaphika chakudya, Esau anabwera kuchokera kuthengo ali wolefuka ndi njala.
30 and to say Esau to(wards) Jacob to eat me please from [the] red stuff [the] red stuff [the] this for faint I upon so to call: call by name his Edom
Iye anati kwa Yakobo, “Tandipatsako phala lofiiralo, ndimwe! Ndalefuka ndi njala.” (Nʼchifukwa chake amatchedwanso Edomu).
31 and to say Jacob to sell [emph?] like/as day: today [obj] birthright your to/for me
Yakobo anayankha, “Choyamba undigulitse ukulu wako.”
32 and to say Esau behold I to go: continue to/for to die and to/for what? this to/for me birthright
Esau anati, “Chabwino, ine ndatsala pangʼono kufa, ukulu undithandiza chiyani?”
33 and to say Jacob to swear [emph?] to/for me like/as day: today and to swear to/for him and to sell [obj] birthright his to/for Jacob
Koma Yakobo anati, “Lumbira kwa ine choyamba.” Kotero Esau analumbiradi, ndipo anagulitsa ukulu wake kwa Yakobo.
34 and Jacob to give: give to/for Esau food: bread and stew lentil and to eat and to drink and to arise: rise and to go: journey and to despise Esau [obj] [the] birthright
Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita. Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.