< Genesis 20 >
1 and to set out from there Abraham land: country/planet [to] [the] Negeb and to dwell between Kadesh and between Shur and to sojourn in/on/with Gerar
Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
2 and to say Abraham to(wards) Sarah woman: wife his sister my he/she/it and to send: depart Abimelech king Gerar and to take: take [obj] Sarah
ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
3 and to come (in): come God to(wards) Abimelech in/on/with dream [the] night and to say to/for him behold you to die upon [the] woman which to take: take and he/she/it rule: to marry master: men
Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
4 and Abimelech not to present: come to(wards) her and to say Lord nation also righteous to kill
Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
5 not he/she/it to say to/for me sister my he/she/it and he/she/it also he/she/it to say brother: male-sibling my he/she/it in/on/with integrity heart my and in/on/with innocence palm my to make: do this
Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
6 and to say to(wards) him [the] God in/on/with dream also I to know for in/on/with integrity heart your to make: do this and to withhold also I [obj] you from to sin to/for me upon so not to give: allow you to/for to touch to(wards) her
Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
7 and now to return: return woman: wife [the] man for prophet he/she/it and to pray about/through/for you and to live and if nothing you to return: return to know for to die to die you(m. s.) and all which to/for you
Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
8 and to rise Abimelech in/on/with morning and to call: call to to/for all servant/slave his and to speak: speak [obj] all [the] word: thing [the] these in/on/with ear: to ears their and to fear [the] human much
Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
9 and to call: call to Abimelech to/for Abraham and to say to/for him what? to make: do to/for us and what? to sin to/for you for to come (in): bring upon me and upon kingdom my sin great: large deed which not to make: do to make: do with me me
Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
10 and to say Abimelech to(wards) Abraham what? to see: see for to make: do [obj] [the] word: thing [the] this
Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
11 and to say Abraham for to say except nothing fear God in/on/with place [the] this and to kill me upon word: because woman: wife my
Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
12 and also truly sister my daughter father my he/she/it surely not daughter mother my and to be to/for me to/for woman: wife
Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
13 and to be like/as as which to go astray [obj] me God from house: home father my and to say to/for her this kindness your which to make: do with me me to(wards) all [the] place which to come (in): come there [to] to say to/for me brother: male-sibling my he/she/it
Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
14 and to take: take Abimelech flock and cattle and servant/slave and maidservant and to give: give to/for Abraham and to return: return to/for him [obj] Sarah woman: wife his
Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
15 and to say Abimelech behold land: country/planet my to/for face: before your in/on/with pleasant in/on/with eye: appearance your to dwell
Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
16 and to/for Sarah to say behold to give: give thousand silver: money to/for brother: male-sibling your behold he/she/it to/for you covering eye to/for all which with you and with all and to rebuke
Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
17 and to pray Abraham to(wards) [the] God and to heal God [obj] Abimelech and [obj] woman: wife his and maidservant his and to beget
Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
18 for to restrain to restrain LORD about/through/for all womb to/for house: household Abimelech upon word: because Sarah woman: wife Abraham
Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.